< Eksodo 15 >

1 Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi: “Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wakwezeka mʼchigonjetso. Kavalo ndi wokwera wake, Iye wawaponya mʼnyanja.
Da sang Mose og Israels Børn denne Sang for Herren og sagde: Jeg vil synge for Herren; thi han er højt ophøjet; Hesten og den, som red derpaa, har han nedstyrtet i Havet.
2 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamutamanda, Mulungu wa makolo anga, ine ndidzamukweza.
Herren er min Styrke og Lovsang, og han blev mig til Frelse; denne er min Gud, og jeg vil prise ham, min Faders Gud, og jeg vil ophøje ham.
3 Yehova ndi wankhondo; Yehova ndilo dzina lake.
Herren er en Krigsmand, „Herre” er hans Navn.
4 Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo Iye wawaponya mʼnyanja. Akatswiri ankhondo amphamvu a Farao amizidwa mʼNyanja Yofiira.
Han kastede Faraos Vogne og hans Hær i Havet, og hans udvalgte Høvedsmænd bleve druknede i det røde Hav.
5 Nyanja yakuya inawaphimba; Iwo anamira pansi ngati mwala.”
Afgrundene skjulte dem; de sank ned i de dybe Vande som en Sten.
6 Yehova, dzanja lanu lamanja ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake. Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja linaphwanya mdani.
Herre! din højre Haand har vist sig at være herlig med Styrke; Herre! du knuser Fjenden med din højre Haand.
7 Ndi ulemerero wanu waukulu, munagonjetsa okutsutsani. Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu; ndipo unawapsereza ngati udzu.
Og du nedstøder dine Modstandere med din store Højhed; du udsender din Vrede, den fortærer dem som Straa.
8 Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu madzi anawunjikana pamodzi. Nyanja yakuya ija inasanduka madzi owuma gwaa kufika pansi.
Og ved din Vredes Vejr ophobedes Vandene, Strømmene stode som en Dynge; Bølgerne stivnede midt i Havet.
9 Mdaniyo anati, “Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira. Ndidzagawa chuma chawo; ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa. Ine ndidzasolola lupanga langa, ndi mkono wanga ndidzawawononga.”
Fjenden sagde: Jeg vil forfølge, gribe, dele Rovet; min Sjæl skal stille sin Lyst paa dem, jeg vil uddrage mit Sværd, min Haand skal udrydde dem.
10 Koma Inu munawuzira mphepo yanu, ndipo nyanja inawaphimba. Iwo anamira ngati chitsulo mʼmadzi amphamvu.
Du blæste med dit Vejr, Havet skjulte dem; de sank som Bly i de mægtige Vande.
11 Ndithu Yehova, pakati pa milungu, ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera, ndiponso wotamandika wolemekezeka, chifukwa cha ntchito zanu, zazikulu ndi zodabwitsa?
Hvo er som du iblandt Guderne, Herre? hvo er som du, herlig bevist i Hellighed, forfærdelig at berømme, underfuld i Gerning!
12 Munatambasula dzanja lanu lamanja ndipo dziko linawameza.
Du udrakte din højre Haand, Jorden opslugte dem.
13 Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera anthu amene munawawombola. Ndi mphamvu zanu munawatsogolera ku malo anu woyera.
Du har ved din Miskundhed ført dette Folk, som du har genløst; du ledsagede dem med din Kraft til din Helligheds Bolig.
14 Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha, mantha woopsa agwira anthu a dziko la Filisiti.
Folkene hørte det, de bævede; Angest betog dem, som bo i Palæstina.
15 Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu, otsogolera a dziko la Mowabu akunjenjemera ndi mantha, ndipo anthu a ku Kanaani asungunuka ndi mantha.
Da forfærdedes Edoms Fyrster, Bæven betog de vældige i Moab, alle Indbyggere i Kanaan bleve mistrøstige.
16 Onse agwidwa ndi mantha woopsa. Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu, iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu, Inu Yehova atadutsa; inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.
Forfærdelse og Frygt skal falde over dem, ved din Arms Magt skulle de blive tavse som en Sten, indtil dit Folk, Herre! kommer over, til det Folk kommer over, som du har forhvervet.
17 Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa pa phiri lanu. Pa malo pamene Inu Yehova munawapanga kuti muzikhalapo; malo wopatulika amene Inu Ambuye munawakonza ndi manja anu.
Du skal føre dem ind og plante dem paa din Arvs Bjerg; du har gjort en Bolig, hvori du vil bo, o Herre! en Helligdom, Herre! har dine Hænder beredt.
18 “Yehova adzalamula mpaka muyaya.”
Herren skal regere evindelig og altid.
19 Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma.
Thi Faraos Heste droge ind med hans Vogne og hans Ryttere i Havet, og Herren lod Havets Vande komme tilbage over dem; men Israels Børn gik paa det tørre midt igennem Havet.
20 Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.
Og Maria, den Profetinde, Arons Søster, tog en Pauke i sin Haand; og alle Kvinder gik ud efter hende med Pauker og Dans.
21 Miriamu anawayimbira nyimbo iyi: “Imbirani Yehova, chifukwa iye wapambana. Kavalo ndi wokwerapo wake Iye wawamiza mʼnyanja.”
Og Maria svarede dem: Synger for Herren, thi han er højt ophøjet; Hesten og den, som red derpaa, har han nedstyrtet i Havet.
22 Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi.
Og Mose lod Israel drage frem fra det røde Hav, og de droge ud til den Ørk Sur, og de vandrede tre Dage i Ørkenen og fandt ikke Vand.
23 Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara).
Saa kom de til Mara; men de kunde ikke drikke Vandet i Mara, thi det var besk; derfor kaldte han dens Navn Mara.
24 Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”
Da knurrede Folket imod Mose og sagde: Hvad skulle vi drikke?
25 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino. Kumeneko Yehova anawayikira lamulo ndi maweruziro. Kumenekonso Yehova anawayesa.
Saa raabte han til Herren, og Herren viste ham et Træ, og han kastede det i Vandet, og saa blev Vandet sødt. Der satte han dem Lov og Ret, og der forsøgte han dem.
26 Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”
Og han sagde: Om du flitteligen hører Herren din Guds Røst, og gør det, som Ret er for hans Øjne, og vender dine Øren til hans Bud og holder alle hans Befalinger, da vil jeg ikke lægge paa dig nogen af de Sygdomme, som jeg lagde paa Ægypterne; thi jeg er Herren, som læger dig.
27 Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.
Og de kom til Elim, og der var tolv Vandkilder og halvfjerdsindstyve Palmetræer; og der lejrede de sig ved Vandet.

< Eksodo 15 >