< Eksodo 15 >
1 Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi: “Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wakwezeka mʼchigonjetso. Kavalo ndi wokwera wake, Iye wawaponya mʼnyanja.
Тогава запяха Моисей и израилтяните тая песен Господу, като говориха с тия думи: - Ще пея Господу, защото славно възтържествува; Коня и ездача му хвърли в морето.
2 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamutamanda, Mulungu wa makolo anga, ine ndidzamukweza.
Господ е сила моя, песен моя. И стана ми Спасител; Той ми е Бог и ще Го прославя, Бащиният ми Бог, и ще Го превъзвиша.
3 Yehova ndi wankhondo; Yehova ndilo dzina lake.
Господ е силен Воевател; Името Му е Иеова.
4 Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo Iye wawaponya mʼnyanja. Akatswiri ankhondo amphamvu a Farao amizidwa mʼNyanja Yofiira.
Колесниците Фараонови и войската му хвърли в морето; Отборните му полководци потънаха в Червеното море.
5 Nyanja yakuya inawaphimba; Iwo anamira pansi ngati mwala.”
Дълбочините ги покриха Като камък слязоха в бездните.
6 Yehova, dzanja lanu lamanja ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake. Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja linaphwanya mdani.
Десницата Ти, Господи, се прослави в сила Десницата Ти, Господи, смаза неприятеля.
7 Ndi ulemerero wanu waukulu, munagonjetsa okutsutsani. Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu; ndipo unawapsereza ngati udzu.
С превъзходното Си величие изтребил си противниците Си Пратил си гнева Си, и пояде ги като слама.
8 Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu madzi anawunjikana pamodzi. Nyanja yakuya ija inasanduka madzi owuma gwaa kufika pansi.
От духането на ноздрите Ти вадите се струпаха на куп, Вълните застанаха като грамада, Бездните се сгъстиха всред морето.
9 Mdaniyo anati, “Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira. Ndidzagawa chuma chawo; ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa. Ine ndidzasolola lupanga langa, ndi mkono wanga ndidzawawononga.”
Неприятелят рече: Ще погна, ще стигна, ще разделя користите; Похотта ми ще се насити върху тях; Ще изтръгна ножа си, ръката ми ще ги погуби.
10 Koma Inu munawuzira mphepo yanu, ndipo nyanja inawaphimba. Iwo anamira ngati chitsulo mʼmadzi amphamvu.
Подухнал си с вятъра Си, и морето ги покри; Потънаха като олово в силните води.
11 Ndithu Yehova, pakati pa milungu, ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera, ndiponso wotamandika wolemekezeka, chifukwa cha ntchito zanu, zazikulu ndi zodabwitsa?
Кой е подобен на Тебе, Господи, между боговете? Дивен та да Те възпяват, правещ чудеса?
12 Munatambasula dzanja lanu lamanja ndipo dziko linawameza.
Прострял си десницата Си, И земята ги погълна.
13 Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera anthu amene munawawombola. Ndi mphamvu zanu munawatsogolera ku malo anu woyera.
С милостта Си водил си людете, които си откупил; Упътил си ги със силата Си към светото Си обиталище.
14 Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha, mantha woopsa agwira anthu a dziko la Filisiti.
Племената ще чуят и ще затреперят; Ужас ще обладае филистимските жители,
15 Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu, otsogolera a dziko la Mowabu akunjenjemera ndi mantha, ndipo anthu a ku Kanaani asungunuka ndi mantha.
Тогава ще се уплашат едомските началници; Трепет ще обземе моавските силни; Всичките жители на Ханаан ще се стопят.
16 Onse agwidwa ndi mantha woopsa. Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu, iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu, Inu Yehova atadutsa; inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.
Страх и трепет ще нападне на тях; Чрез великата Ти мишца ще станат неподвижни като камък. Догде заминат людете ти, Господи, Догде заминат людете, които си придобил.
17 Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa pa phiri lanu. Pa malo pamene Inu Yehova munawapanga kuti muzikhalapo; malo wopatulika amene Inu Ambuye munawakonza ndi manja anu.
Ще ги въведеш и насадиш в хълма - Твоето наследство, На мястото, Господи, което си приготвил за свое обиталище, В светилището, Господи, което ръцете Ти утвърдиха.
18 “Yehova adzalamula mpaka muyaya.”
Господ ще царува до вечни векове.
19 Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma.
Защото, като бяха влезли в морето Фараоновите коне с колесниците му и с конниците му, Господ беше повърнал върху тях водите на морето; а израилтяните бяха преминали през сред морето.
20 Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.
Тогава пророчицата Мариам, Аароновата сестра, взе в ръката си тъпанче, и всички жени излязоха подир нея с тъпанчета и хороиграния,
21 Miriamu anawayimbira nyimbo iyi: “Imbirani Yehova, chifukwa iye wapambana. Kavalo ndi wokwerapo wake Iye wawamiza mʼnyanja.”
а Мариам им пееше ответно: Пейте Господу, защото славно възтържествува; Коня и ездача му хвърли в морето.
22 Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi.
Тогава Моисей дигна израилтяните от Червеното Море и излязоха към пустинята Сур; и като вървяха три дена в пустинята не намериха вода.
23 Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara).
После дойдоха в Мера, но не можеха да пият от водата на Мера защото беше горчива; (затова се наименува Мера).
24 Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”
Тогава людете роптаеха против Моисея, казвайки: Що да пием?
25 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino. Kumeneko Yehova anawayikira lamulo ndi maweruziro. Kumenekonso Yehova anawayesa.
А той извика към Господа, и Господ му показа дърво; и като го хвърли във водата, водата се подслади. Там им положи повеление и наредба и там ги опита, като рече:
26 Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”
Ако прилежно слушаш гласа на Господа своя Бог, и вършиш онова, което Му е угодно, и слушаш заповедите Му, и пазиш всичките Му повеления, то не ще ти нанеса ни една от болестите, които нанесох върху египтяните; защото Аз съм Господ, Който те изцелявам.
27 Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.
После дойдоха в Елим, гдето имаше дванадесет палмови дървета; и там се разположиха на стан при водите.