< Eksodo 14 >
1 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Uza Aisraeli abwerere ndi kukagona pafupi ndi Pihahiroti, pakati pa Migidoli ndi nyanja. Inu mumange zithando mʼmbali mwa nyanja moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
Speak to [the] people of Israel so they may turn back and they may encamp before Pi-hahiroth between Migdol and between the sea before Baal-Zephon opposite it you will encamp at the sea.
3 Farao adzaganiza kuti ‘Aisraeli asokonezeka nʼkumangozungulirazungulira mu dzikomo, chipululu chitawazinga.’
And he will say Pharaoh of [the] people of Israel [are] wandering in confusion they in the land it has shut on them the wilderness.
4 Ndidzawumitsa mtima wa Farao ndipo adzathamangira Aisraeliwo. Choncho ndikadzagonjetsa Farao ndi gulu lake lonse la nkhondo, Ine ndidzalemekezedwa.” Choncho Aisraeli aja anachita zimenezi.
And I will make strong [the] heart of Pharaoh and he will pursue after them and I will gain honor by Pharaoh and by all army his and they will know Egypt that I [am] Yahweh and they did so.
5 Farao, mfumu ya Igupto atamva kuti anthu aja athawa, iye pamodzi ndi nduna zake anasintha maganizo awo pa Israeli ndipo anati, “Ife tachita chiyani? Tawalola Aisraeli kuti apite ndi kuleka kutitumikira?”
And it was told to [the] king of Egypt that it had fled the people and it was changed [the] heart of Pharaoh and servants his to the people and they said what? this have we done that we have let go Israel from serving us.
6 Choncho anakonzetsa galeta lake ndipo ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake.
And he harnessed chariot his and people his he took with him.
7 Iye anatenga magaleta 600 abwino kwambiri pamodzi ndi magaleta ena a dziko la Igupto. Anatenganso akuluakulu onse ankhondo.
And he took six hundred chariot[s] chosen and all [the] chariotry of Egypt and officers [were] over all of it.
8 Yehova anawumitsa mtima wa Farao mfumu ya dziko la Igupto, kotero iye anawathamangira Aisraeli amene ankachoka mʼdzikomo mosavutika.
And he made strong Yahweh [the] heart of Pharaoh [the] king of Egypt and he pursued after [the] people of Israel and [the] people of Israel [were] going out with a hand raised.
9 Aigupto aja (kutanthauza akavalo ndi magaleta onse a Farao, okwera akavalowo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo) analondola Aisraeli aja ndipo anakawapeza pamalo pamene anamanga zithando paja, mʼmbali mwa nyanja, pafupi ndi Pihahiroti, moyangʼanana ndi Baala-Zefoni.
And they pursued Egypt after them and they overtook them encamped at the sea every horse of [the] chariotry of Pharaoh and horsemen his and army his at Pi-hahiroth before Baal-Zephon.
10 Tsono Farao anayandikira. Ndipo Aisraeli ataona kuti Aigupto akuwatsatira, anachita mantha aakulu ndipo anafuwula kwa Yehova.
And Pharaoh he drew near and they lifted up [the] people of Israel eyes their and there! Egypt - [was] marching after them and they were afraid exceedingly and they cried out [the] people of Israel to Yahweh.
11 Iwo anafunsa Mose kuti, “Kodi nʼchifukwa chakuti kunalibe manda ku dziko la Igupto kuti iwe utibweretse muno mʼchipululu kuti tidzafe? Chimene watichitachi nʼchiyani, kutitulutsa mʼdziko la Igupto?
And they said to Moses ¿ because not there not [were] graves in Egypt you brought us to die in the wilderness what? this have you done to us by bringing out us from Egypt.
12 Kodi sindizo zimene tinakuwuza mʼdziko la Igupto? Ife tinati, ‘Tileke titumikire Aigupto?’ Zikanatikomera kutumikira Aigupto kulekana ndi kufa mʼchipululu muno.”
¿ Not [is] this the word which we spoke to you in Egypt saying cease from us so let us serve Egypt for [is] better for us serving Egypt than to die us in the wilderness.
13 Mose anayankha anthu kuti, “Musachite mantha. Imani, ndipo muone chipulumutso chimene Yehova akuchitireni lero. Aigupto amene mukuwaona lerowa simudzawaonanso.
And he said Moses to the people may not you be afraid stand firm and see [the] deliverance of Yahweh which he will bring about for you this day for which you have seen Egypt this day not you will repeat to see them again until perpetuity.
14 Yehova adzakumenyerani nkhondo. Inu mungokhala chete.”
Yahweh he will fight for you and you you will keep quiet!
15 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Chifukwa chiyani ukufuwulira kwa ine? Uwuze Aisraeli aziyenda.
And he said Yahweh to Moses why? are you crying out to me speak to [the] people of Israel so they may set out.
16 Nyamula ndodo yako ndi kutambasula dzanja lako kuloza ku nyanja, kugawa madzi kuti Aisraeli awoloke powuma.
And you raise staff your and stretch out hand your over the sea and divide it so they may go [the] people of Israel in [the] middle of the sea on the dry ground.
17 Ine ndidzawumitsa mitima ya Aigupto kotero kuti adzatsatirabe Aisraeli. Ndipo ine ndikadzagonjetsa Farao ndi asilikali ake onse ankhondo, okwera magaleta ndi akavalo, ndidzapeza ulemerero.
And I here I [am] about to make strong [the] heart of Egypt so they may go after them and I will gain honor by Pharaoh and by all army his by chariot[s] his and by horsemen his.
18 Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova akadzaona mmene ndipambanire Farao ndi magaleta ndi owayendetsa ake.”
And they will know Egypt that I [am] Yahweh when gain honor I by Pharaoh by chariot[s] his and by horsemen his.
19 Ndipo mngelo wa Mulungu amene amayenda patsogolo pa gulu lankhondo la Israeli anachoka ndi kupita kumbuyo kwawo. Chipilala cha mtambo chinasunthanso kuchoka kutsogolo ndi kupita kumbuyo kwawo.
And he set out [the] angel of God who had been going before [the] camp of Israel and he went behind them and it set out [the] pillar of cloud from before them and it stood behind them.
20 Choncho mtambowo unakhala pakati pa asilikali ankhondo a dziko la Igupto ndi a dziko la Israeli. Choncho panali mdima motero kuti magulu awiri ankhondowa sanathe kuyandikizana usiku wonse.
And it went between - [the] camp of Egypt and between [the] camp of Israel and it was the cloud and the darkness and it lit up the night and not it drew near this to this all the night.
21 Kenaka Mose anatambalitsa dzanja lake pa nyanja, ndipo Yehova pogwiritsa ntchito mphepo yamphamvu ya kummawa imene inawomba usiku wonse anabweza madzi ndi kuwumitsa nyanja ija. Choncho nyanja ija inagawanika.
And he stretched out Moses hand his over the sea and he drove Yahweh - the sea by a wind an east wind strong all the night and he made the sea into dry ground and they were divided the waters.
22 Ndipo Aisraeli anawoloka pakati pa nyanja powuma, madzi atasanduka khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
And they went [the] people of Israel in [the] middle of the sea on the dry ground and the water for them [was] a wall from right their and from left their.
23 Aigupto onse, Farao, ndi onse okwera pa magaleta ndi akavalo anawalondola ndipo analowa mʼmadzi.
And they pursued Egypt and they went after them every horse of Pharaoh chariotry his and horsemen his into [the] middle of the sea.
24 Kutatsala pangʼono kucha, Yehova ali mu chipilala chamoto ndi chamtambo, anayangʼana asilikali ankhondo a Igupto ndipo anabweretsa chisokonezo pakati pawo.
And it was in [the] watch of the morning and he looked down Yahweh to [the] camp of Egypt in a pillar of fire and cloud and he confused [the] camp of Egypt.
25 Yehova anamanga matayala a magaleta kotero kuti ankavutika kuyenda. Ndipo Aigupto anati, “Tiyeni tiwathawe Aisraeli! Yehova akuwamenyera nkhondo kulimbana nafe.”
And he turned aside [the] wheel[s] of chariots its and he caused to drive it with difficulty and it said Egypt let me flee from before Israel for Yahweh [is] fighting for them (against Egypt. *LB(ha)*)
26 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasula dzanja lako pa nyanja kuti madzi amize Aigupto ndi magaleta awo ndi okwera pa akavalo.”
And he said Yahweh to Moses stretch out hand your over the sea so they may return the waters over Egypt over chariot[s] its and over horsemen its.
27 Mose anatambasula dzanja lake pa nyanja, ndipo mmene kumacha nyanja inabwerera mʼmalo mwake. Aigupto pothawa anakumana nayo, ndipo Yehova anawakokera mʼnyanja momwemo.
And he stretched out Moses hand his over the sea and it returned the sea to [the] turning of morning to normal [state] its and Egypt [were] fleeing to meet it and he shook off Yahweh Egypt in [the] middle of the sea.
28 Madzi anabwerera ndi kumiza magaleta ndi okwera akavalo, asilikali ankhondo onse amene anatsatira Aisraeli mʼnyanja, palibe ndi mmodzi yemwe amene anapulumuka.
And they returned the waters and they covered the chariot[s] and the horsemen to all [the] army of Pharaoh which had gone after them in the sea not it remained among them up to one.
29 Koma Aisraeli aja anawoloka nyanja pansi pali powuma, madzi atachita khoma kumanja ndi kumanzere kwawo.
And [the] people of Israel they walked on the dry ground in [the] middle of the sea and the water for them [was] a wall from right their (and from left their *LB(ah)*)
30 Tsiku limeneli Yehova anapulumutsa Israeli mʼmanja mwa Aigupto ndipo Israeli anaona Aigupto ali lambalamba mʼmbali mwa nyanja atafa
and he delivered Yahweh on the day that Israel from [the] hand of Egypt and it saw Israel Egypt dead on [the] shore of the sea.
31 Choncho Aisraeli anaona dzanja lamphamvu la Yehova limene linagonjetsa Aigupto aja, ndipo iwo anaopa Yehova ndi kumukhulupirira pamodzi ndi mtumiki wake Mose.
And it saw Israel the hand great which he had used Yahweh on Egypt and they feared the people Yahweh and they believed in Yahweh and in Moses servant his.