< Eksodo 13 >

1 Yehova anati kwa Mose,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
Ngingcwelisela lonke izibulo, elivula loba yisiphi isizalo phakathi kwabantwana bakoIsrayeli, elomuntu lelenyamazana, lingelami.
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
UMozisi wasesithi ebantwini: Khumbulani lolusuku eliphume ngalo eGibhithe, endlini yobugqili; ngoba ngamandla esandla iNkosi ilikhuphile lapha. Njalo kakungadliwa isinkwa esilemvubelo.
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
Ngalolusuku liyaphuma ngenyanga kaAbhibhi.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
Njalo kuzakuthi lapho iNkosi isikungenisile elizweni lamaKhanani lamaHethi lamaAmori lamaHivi lamaJebusi, afunga kuboyihlo ukukunika lona, ilizwe eligeleza uchago loluju, uzagcina linkonzo ngalinyanga.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
Insuku eziyisikhombisa uzakudla izinkwa ezingelamvubelo, langosuku lwesikhombisa kuzakuba khona umkhosi eNkosini.
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
Izinkwa ezingelamvubelo zizadliwa ngensuku eziyisikhombisa; njalo kakuyikubonwa kuwe okuvutshelweyo lemvubelo kayiyikubonwa kuwe kuwo wonke umngcele wakho.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
Njalo uzatshela indodana yakho ngalolosuku usithi: Ngenxa yalokho iNkosi eyakwenza kimi ekuphumeni kwami eGibhithe.
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
Futhi kuzakuba kuwe luphawu phezu kwesandla sakho lesikhumbuzo phakathi laphakathi kwamehlo akho, ukuze umlayo weNkosi ube semlonyeni wakho; ngoba ngesandla esilamandla iNkosi ikukhuphile eGibhithe.
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
Ngakho uzagcina lesisimiso ngesikhathi saso esimisiweyo iminyaka ngeminyaka.
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
Njalo kuzakuthi lapho iNkosi isikungenisile elizweni lamaKhanani, njengokufunga kwayo kuwe lakuboyihlo, isikunike lona,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
uzakwehlukanisela iNkosi konke okuvula isizalo; lalo lonke izibulo lomqegu wezifuyo olazo, amaduna azakuba ngaweNkosi.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
Lalo lonke izibulo likababhemi uzalihlenga ngewundlu; kodwa uba ungalihlengi, uzalephula intamo; lalo lonke izibulo lomuntu phakathi kwamadodana akho uzalihlenga.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
Njalo kuzakuthi lapho indodana yakho ikubuza ngesikhathi esizayo isithi: Kuyini lokhu? Uzakuthi kuyo: Ngamandla esandla iNkosi yasikhupha eGibhithe, endlini yobugqili.
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
Ngoba kwathi uFaro ezenza lukhuni ukuthi asiyekele sihambe, iNkosi yabulala lonke izibulo elizweni leGibhithe, kusukela kuzibulo lomuntu kusiya kuzibulo lezifuyo; ngakho ngiyahlabela iNkosi konke okuvula isizalo okuduna; kodwa lonke izibulo lamadodana ami ngiyalihlenga.
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
Njalo kuzakuba luphawu phezu kwesandla sakho lamafilakteriyu phakathi laphakathi kwamehlo akho, ngoba ngamandla esandla iNkosi yasikhupha eGibhithe.
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
Kwasekusithi uFaro eseyekele abantu bahambe, uNkulunkulu kabakhokhelanga ngendlela yelizwe lamaFilisti, lanxa yayiseduze; ngoba uNkulunkulu wathi: Hlezi abantu bazisole nxa bebona impi, babuyele eGibhithe.
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
Kodwa uNkulunkulu wababhodisa abantu ngendlela yenkangala yoLwandle oluBomvu. Abantwana bakoIsrayeli basebesenyuka besuka elizweni leGibhithe behlomile.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
UMozisi wasethatha amathambo kaJosefa wahamba lawo, ngoba wayebafungisile lokubafungisa abantwana bakoIsrayeli esithi: Isibili uNkulunkulu uzalihambela; futhi kalibokwenyusa lapha amathambo ami lihambe lawo.
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
Basebesuka eSukothi, bamisa inkamba eEthama, ekucineni kwenkangala.
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
INkosi yasihamba phambi kwabo emini ngensika yeyezi ukubakhokhela endleleni, lebusuku ngensika yomlilo ukubakhanyisela, ukuze bahambe emini lebusuku.
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
Kayiyisusanga insika yeyezi emini, lensika yomlilo ebusuku, phambi kwabantu.

< Eksodo 13 >