< Eksodo 13 >
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
“Ngahlukanisela wonke amazibulo esilisa. Konke okuzalwa kuqala phakathi kwabako-Israyeli kungokwami, kungaba ngumuntu loba isifuyo.”
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
Ngakho uMosi wasesithi ebantwini, “Lugcineni lube lusuku lwesikhumbuzo lolu, ilanga elaphuma ngalo eGibhithe, liphuma elizweni lobugqili, ngoba uThixo walikhupha khona ngamandla amakhulu. Lingadli lutho olulemvubelo.
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
Lamuhla ngenyanga ka-Abhibhi, liyasuka.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
Kuzakuthi uThixo angalifikisa elizweni lamaKhenani, amaHithi, ama-Amori, amaHivi lamaJebusi, ilizwe afunga kubokhokho benu ukuthi uzalinika lona, ilizwe eligeleza uchago loluju, kufanele liwugcine lumkhosi ngayonale inyanga.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
Okwensuku eziyisikhombisa lidle isinkwa esingelamvubelo kuthi ngosuku lwesikhombisa lithakazelele umkhosi kaThixo;
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
kungabonwa lutho olulemvubelo phakathi kwenu, kuvele kungabonwa mvubelo elizweni lenu lonke.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
Ngalelolanga ngulowo lalowo atshele indodana yakhe athi, ‘Lokhu ngikwenza ngenxa yalokho uThixo angenzela khona ekuphumeni kwami eGibhithe.’
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
Lesisikhumbuzo kuwe sizakuba luphawu esandleni sakho lesikhumbuzo ebunzini lakho ukuthi umlayo kaThixo ube sezindebeni zakho. Ngoba uThixo wakukhupha eGibhithe ngesandla sakhe esilamandla amakhulu.
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
Kalibosigcina lesisimiso ngesikhathi esimisiweyo minyaka yonke.
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
Nxa uThixo eselingenisile elizweni lamaKhenani walinika lona njengokuthembisa kwakhe kini lakubokhokho benu,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
kumele lahlukanisele uThixo konke okuzalwa kuqala yizo zonke izibeletho. Wonke amazibulo esilisa ezifuyo zenu ngakaThixo.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
Lizahlenga izibulo likababhemi ngezinyane, kodwa nxa lingalihlenganga lephuleni intamo. Lihlenge njalo wonke amadodana enu angamazibulo.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
Nxa indodana yakho ikubuza ngesikhathi esizayo isithi, ‘Kutshoni lokhu?’ ubokuthi kuyo, ‘uThixo wasikhupha eGibhithe ngesandla sakhe esilamandla amakhulu, wasikhupha elizweni lobugqili.
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
Kwathi uFaro eqholoza esala ukuthi sihambe, uThixo wabulala wonke amazibulo eGibhithe, awabantu lawezinyamazana. Yikho-nje nginikela kuThixo izibulo lesilisa lenzalo yonke ngiphinde ngihlenge wonke amadodana ami angamazibulo.’
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
Lokhu kuzakuba njengophawu esandleni sakho lesibonelo ebunzini lakho ukuthi uThixo wakukhupha eGibhithe ngesandla sakhe esilamandla amakhulu.”
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
UFaro esebavumele abantu ukuthi bahambe, uNkulunkulu kabakhokhelanga ngendlela edabula elizweni lamaFilistiya loba yona yayiquma. Ngoba uNkulunkulu wathi, “Nxa behlangana lempi mhlawumbe bangethuka babuyele eGibhithe.”
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
Yikho uNkulunkulu wabahola ngendlela yenkangala eya oLwandle Olubomvu. Abako-Israyeli baphuma eGibhithe behlomele impi.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
UMosi wawathwala amathambo kaJosefa ngoba uJosefa wayenze isifungo lamadodana ka-Israyeli wathi, “Ngempela uNkulunkulu uzalikhulula. Lapho-ke libowathwala amathambo ami lisuke lawo kule indawo.”
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
Sebesukile eSukhothi bayamisa e-Ethamu indawo egudlene lenkangala.
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
Emini uThixo wahamba phambi kwabo ngensika yeyezi ebahola endleleni yabo, kwathi ebusuku wabahola ngensika yomlilo ukubakhanyisela ukuze bahambe emini lebusuku.
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
Insika yeyezi emini loba insika yomlilo ebusuku kakuzange kusuke endaweni yakho phambi kwabantu.