< Eksodo 13 >

1 Yehova anati kwa Mose,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
Consacre-moi tout premier né qui ouvre un sein parmi les enfants d’Israël, tant d’entre les hommes que d’entre les bêtes: car à moi sont toutes choses.
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
Et Moïse dit au peuple: Souvenez-vous de ce jour auquel vous êtes sortis de l’Egypte et de la maison de servitude; car par une main puissante le Seigneur vous a retirés de ce lieu: vous ne mangerez donc point de pain fermenté.
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
Vous sortez aujourd’hui dans le mois des nouveaux grains.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
Et quand le Seigneur t’aura introduit dans la terre du Chananéen, de l’Héthéen, de l’Amorrhéen, de l’Hévéen et du Jébuséen, terre qu’il a juré à tes pères qu’il te donnerait, terre où coulent du lait et du miel, tu célébreras cette pratique sacrée en ce mois.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
Pendant sept jours tu te nourriras d’azymes, et le septième jour sera une solennité du Seigneur.
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
Vous mangerez des azymes pendant sept jours; il ne paraîtra point de pain fermenté chez toi, ni dans tous tes confins.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
Et tu le raconteras à ton fils en ce jour-là, disant: Voilà ce qu’a fait pour moi le Seigneur, quand je suis sorti de l’Egypte.
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
Et ce sera comme un signe en ta main, et comme un monument devant tes yeux, et afin que la loi du Seigneur soit toujours en ta bouche; car c’est avec une main puissante que le Seigneur t’a retiré de l’Egypte.
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
Tu observeras un culte de cette sorte au temps marqué d’année en année,
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
Et lorsque le Seigneur t’aura introduit dans la terre du Chananéen, comme il l’a juré à toi à tes pères, et qu’il te l’aura donnée,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
Tu sépareras pour le Seigneur tout ce qui ouvre un sein et ce qui est primitif dans tes troupeaux; tout ce que tu auras du sexe masculin, tu le consacreras au Seigneur.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
Tu échangeras le premier-né de l’âne pour une brebis: que si tu ne le rachètes point, tu le tueras. Mais tout premier-né de l’homme d’entre tes fils, c’est avec de l’argent que tu le rachèteras.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
Et quand ton fils t’interrogera demain, disant: Qu’est-ce que ceci? tu lui répondras: Par une main puissante le Seigneur nous a retirés de la terre d’Egypte, de la maison de servitude.
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
Car comme Pharaon s’était endurci, et qu’il ne voulait pas nous laisser aller, le Seigneur tua tout premier-né dans la terre d’Egypte, depuis le premier-né de l’homme jusqu’au premier-né des bêtes: c’est pourquoi j’immole au Seigneur tout mâle qui ouvre un sein, et je rachète tous les premiers-nés de mes fils.
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
Ce sera donc comme un signe en ta main, et comme quelque chose de suspendu entre tes yeux, pour souvenir; parce que par une main puissante le Seigneur nous a retirés de l’Egypte.
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
Or, quand Pharaon eut laissé aller le peuple. Dieu ne les conduisit point par le chemin de la terre des Philistins qui est voisine, pensant que peut-être il se repentirait, s’il voyait des guerres s’élever contre lui, et qu’il retournerait en Egypte.
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
Mais il leur fit faire un détour par la voie du désert, qui est près de la mer Rouge: ainsi les enfants d’Israël montèrent armés de la terre d’Egypte.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
Moïse emporta aussi avec lui les os de Joseph, parce que Joseph avait adjuré les enfants d’Israël, disant: Dieu vous visitera; emportez d’ici mes os avec vous.
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
Partis donc de Socoth, ils campèrent à Etham, à l’extrémité du désert.
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
Or le Seigneur les précédait pour montrer la voie, le jour dans une colonne de nuée, et la nuit dans une colonne de feu; afin qu’il fût leur guide dans l’un et l’autre temps.
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
Jamais la colonne de nuée ne disparut devant le peuple durant le jour, ni la colonne de feu durant la nuit.

< Eksodo 13 >