< Eksodo 13 >

1 Yehova anati kwa Mose,
And YHWH speaks to Moses, saying,
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
“Sanctify to Me every firstborn, opening any womb among the sons of Israel, among man and among beast; it [is] Mine.”
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
And Moses says to the people, “Remember this day [in] which you have gone out from Egypt, from the house of servants, for by strength of hand YHWH has brought you out from this, and anything fermented is not eaten;
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
you are going out today, in the month of Abib.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
And it has been, when YHWH brings you to the land of the Canaanite, and of the Hittite, and of the Amorite, and of the Hivite, and of the Jebusite, which He has sworn to your fathers to give to you, a land flowing with milk and honey, that you have done this service in this month.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
Seven days you eat unleavened things, and in the seventh day [is] a celebration to YHWH;
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
unleavened things are eaten the seven days, and anything fermented is not seen with you; indeed, leaven is not seen with you in all your border.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
And you have declared to your son in that day, saying, [It is] because of what YHWH did to me, in my going out from Egypt,
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
and it has been to you for a sign on your hand, and for a memorial between your eyes, so that the Law of YHWH is in your mouth, for by a strong hand YHWH has brought you out from Egypt;
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
and you have kept this statute at its appointed time from days to days.
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
And it has been, when YHWH brings you to the land of the Canaanite as He has sworn to you and to your fathers, and has given it to you,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
that you have caused everyone opening a womb to pass over to YHWH, and every firstling—the increase of beasts which you have: the males [are] YHWH’s.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
And every firstling of a donkey you ransom with a lamb, and if you do not ransom [it], then you have beheaded it; and you ransom every firstborn of man among your sons.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
And it has been, when your son asks you hereafter, saying, What [is] this? That you have said to him, By strength of hand YHWH has brought us out from Egypt, from a house of servants;
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
indeed, it comes to pass, when Pharaoh has been pained to send us away, that YHWH slays every firstborn in the land of Egypt, from the firstborn of man even to the firstborn of beast; therefore I am sacrificing to YHWH all opening a womb who [are] males, and I ransom every firstborn of my sons;
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
and it has been for a token on your hand, and for frontlets between your eyes, for by strength of hand YHWH has brought us out of Egypt.”
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
And it comes to pass in Pharaoh’s sending the people away, that God has not led them the way of the land of the Philistines, for it [is] near; for God said, “Lest the people sigh in their seeing war, and have turned back toward Egypt”;
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
and God turns around the people the way of the wilderness of the Red Sea, and the sons of Israel have gone up by fifties from the land of Egypt.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
And Moses takes the bones of Joseph with him, for he certainly caused the sons of Israel to swear, saying, “God certainly inspects you, and you have brought up my bones from this [place] with you.”
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
And they journey from Succoth, and encamp in Etham at the extremity of the wilderness,
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
and YHWH is going before them by day in a pillar of a cloud, to lead them in the way, and by night in a pillar of fire, to give light to them, to go by day and by night;
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
He does not remove the pillar of the cloud by day, and the pillar of the fire by night, [from] before the people.

< Eksodo 13 >