< Eksodo 13 >
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
Sanctify unto me all the first-born, whatsoever openeth the womb among the children of Israel, both of man and of beast: it is mine.
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
And Moses said unto the people, Remember this day, on which ye came out from Egypt, out of the house of slavery; for by strength of hand the Lord brought you out from here: and no leavened bread shall be eaten.
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
This day go ye out, in the month of Abib.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
And it shall be, when the Lord doth bring thee into the land of the Canaanites, and the Hittites, and the Emorites, and the Hivites, and the Jebusites, which he hath sworn unto thy fathers to give unto thee, a land flowing with milk and honey, that thou shalt perform this service in this month.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
Seven days shalt thou eat unleavened bread, and on the seventh day shall be a feast to the Lord.
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
Unleavened bread shall be eaten these seven days; and there shall not be seen with thee any leavened bread, neither shall there be seen with thee any leaven in all thy boundaries.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
And thou shalt tell thy son on that day, saying, This is done for the sake of that which the Lord did unto me when I came forth out of Egypt.
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
And it shall be unto thee for a sign upon thy hand, and for a memorial between thy eyes, in order that the law of the Lord may be in thy mouth; for with a strong hand hath the Lord brought thee forth out of Egypt.
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
And thou shalt keep this ordinance in its season, from year to year.
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
And it shall be, when the Lord doth bring thee into the land of the Canaanites, as he hath sworn unto thee and to thy fathers, and giveth it to thee,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
That thou shalt set apart all that openeth the womb unto the Lord; and every firstling that cometh of a beast which thou shalt have, the males, shall belong to the Lord.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
And every firstling of an ass shalt thou redeem with a lamb; and if thou wilt not redeem it, then shalt thou break its neck: and all the first-born of man among thy children shalt thou redeem.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
And it shall be, when thy son asketh thee in time to come, saying, What is this? that thou shalt say unto him, By strength of hand the Lord brought us forth out of Egypt, out of the house of slavery;
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
And it came to pass, when Pharaoh obstinately refused to let us go, that the Lord slew all the first-born in the land of Egypt, both the first-born of man, and the first-born of beast; therefore do I sacrifice to the Lord all that openeth the womb, being males; but all the first-born of my children must I redeem.
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
And it shall be for a sign upon thy hand, and for frontlets between thy eyes; that by strength of hand the Lord brought us forth out of Egypt.
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
And it came to pass, when Pharaoh let the people go, that God did not lead them the way through the land of the Philistines, because it was near; for God said, Lest peradventure the people repent when they see war, and return to Egypt.
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
But God led the people about, by the way of the wilderness to the Red Sea: and the children of Israel went up armed out of the land of Egypt.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
And Moses took the bones of Joseph with him; for he had caused the children of Israel to swear, saying, God will surely visit you, and ye shall then carry up my bones away hence with you.
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
And they took their journey from Succoth, and encamped in Etham, at the edge of the wilderness.
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
And the Lord went before them by day in a pillar of cloud, to lead them the way; and by night in a pillar of fire, to give light to them; that they might go by day and by night:
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
He took not away the pillar of cloud by day, nor the pillar of fire by night, from before the people.