< Eksodo 13 >

1 Yehova anati kwa Mose,
Og HERREN talede til Moses og sagde:
2 “Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
»Du skal hellige mig alt det førstefødte, alt, hvad der aabner Moders Liv hos Israeliterne baade af Mennesker og Kvæg; det skal tilhøre mig!«
3 Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
Og Moses sagde til Folket: »Kom denne Dag i Hu, paa hvilken I vandrer ud af Ægypten, af Trællehuset, thi med stærk Haand førte HERREN eder ud derfra! Og der maa ikke spises syret Brød.
4 Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
I Dag vandrer I ud, i Abib Maaned.
5 Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
Naar nu HERREN fører dig til Kana'anæernes, Hetiternes, Amoriternes, Hivviternes og Jebusiternes Land, som han tilsvor dine Fædre at ville give dig, et Land, der flyder med Mælk og Honning, saa skal du overholde denne Skik i denne Maaned.
6 Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
I syv Dage skal du spise usyret Brød, og paa den syvende Dag skal der være Højtid for HERREN.
7 Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
I disse syv Dage skal der spises usyret Brød, og der maa hverken findes syret Brød eller Surdejg hos dig nogetsteds inden dine Landemærker.
8 Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
Og du skal paa den Dag fortælle din Søn, at dette sker i Anledning af, hvad HERREN gjorde for dig, da du vandrede ud af Ægypten!
9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
Det skal være dig som et Tegn paa din Haand og et Erindringsmærke paa din Pande, for at HERRENS Lov maa være i din Mund, thi med stærk Haand førte HERREN dig ud af Ægypten.
10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
Og du skal holde dig denne Anordning efterrettelig til den fastsatte Tid, Aar efter Aar.
11 “Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
Og naar HERREN fører dig til Kana'anæernes Land, saaledes som han tilsvor dig og dine Fædre, og giver dig det,
12 muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
da skal du overlade HERREN alt, hvad der aabner Moders Liv; alt det førstefødte, som falder efter dit Kvæg, for saa vidt det er et Handyr, skal tilhøre HERREN.
13 Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
Men alt det førstefødte af Æslerne skal du udløse med et Stykke Smaakvæg, og hvis du ikke udløser det, skal du sønderbryde dets Hals; og alt det førstefødte af Mennesker blandt dine Sønner skal du udløse.
14 “Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
Og naar din Søn i Fremtiden spørger dig: Hvad betyder dette? skal du svare ham: Med stærk Haand førte HERREN os ud af Ægypten, af Trællehuset;
15 Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
og fordi Farao gjorde sig haard og ikke vilde lade os drage bort, ihjelslog HERREN alt det førstefødte i Ægypten baade af Folk og Fæ; derfor ofrer vi HERREN alt, hvad der aabner Moders Liv, for saa vidt det er et Handyr, og alt det førstefødte blandt vore Sønner udløser vi!
16 Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
Og det skal være dig som et Tegn paa din Haand og et Erindringsmærke paa din Pande, thi med stærk Haand førte HERREN os ud af Ægypten.«
17 Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
Da Farao lod Folket drage bort, førte Gud dem ikke ad Vejen til Filisterlandet, som havde været den nærmeste, thi Gud sagde: »Folket kunde komme til at fortryde det, naar de ser, der bliver Krig, og vende tilbage til Ægypten.«
18 Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
Men Gud lod Folket gøre en Omvej til Ørkenen i Retning af det røde Hav. Israeliterne drog nu væbnede ud af Ægypten.
19 Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
Og Moses tog Josefs Ben med sig, thi denne havde taget Israels Sønner i Ed og sagt: »Naar Gud ser til eder, skal I føre mine Ben med eder herfra!«
20 Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
De brød op fra Sukkot og lejrede sig i Etam ved Randen af Ørkenen.
21 Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
Men HERREN vandrede foran dem, om Dagen i en Skystøtte for at vise dem Vej og om Natten i en Ildstøtte for at lyse for dem; saa kunde de rejse baade Dag og Nat.
22 Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.
Og Skystøtten veg ikke fra Folket om Dagen, ej heller Ildstøtten om Natten.

< Eksodo 13 >