< Eksodo 12 >

1 Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
Rzekł jeszcze Pan do Mojżesza i do Aarona w ziemi Egipskiej, mówiąc:
2 “Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
Miesiąc ten będzie wam początkiem miesięcy: pierwszy wam będzie między miesiącami w roku.
3 Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
Rzeczcie do wszystkiego zgromadzenia Izraelskiego, mówiąc: Dziesiątego dnia miesiąca tego weźmie sobie każdy baranka według familii, baranka według domu.
4 Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
A jeźliby mniejszy był dom niżeliby zjeść mogli baranka, tedy przybierze i sąsiada swego, który jest najbliższy domu jego, według liczby dusz, naliczywszy tyle osób, ileby ich zjeść mogło baranka.
5 Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
Baranka zupełnego, samca rocznego, mieć będziecie; z owiec albo z kóz weźmiecie go.
6 Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
I będziecie go chowali aż do czternastego dnia miesiąca tego; a zabije go wszystko zebranie zgromadzenia Izraelskiego między dwoma wieczorami.
7 Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
I wezmą ze krwi jego, i pokropią obydwa podwoje i nadprożnik u domu; w którym go będą spożywać.
8 Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
I będą jeść mięso onej nocy pieczone przy ogniu, i przaśniki, z zioły gorzkiemi będą go jeść.
9 Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
Nie jedzcie z niego nic surowego, ani warzonego w wodzie, ale upieczone przy ogniu. Głowę jego z nogami jego, z wnętrznościami jego.
10 Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
A nie zostanie z niego nic do jutra; a jeźliby co z niego do jutra zostało, ogniem spalicie.
11 Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
Tak go tedy pożywać będziecie: Biodra swe przepaszecie, obuwie wasze będzie na nogach waszych, a laska wasza w ręce waszej, a jeść go będziecie spieszno, albowiem przejście jest Pańskie.
12 “Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
Gdyż przejdę przez ziemię Egipską tej nocy, i zabiję wszelkie pierworodne w ziemi Egipskiej, od człowieka aż do bydlęcia, i nad wszystkimi bogi Egipskimi wykonam sądy, Ja Pan.
13 Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
A będzie wam ona krew na znak na domach, w których będziecie; bo ujrzawszy krew, minę was, że nie będzie u was plaga ku zatraceniu, gdy będę zabijał w ziemi Egipskiej.
14 “Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
A będzie wam ten dzień na pamiątkę; i będziecie go obchodzić za święto Panu w narodziech waszych; ustawą wieczną obchodzić go będziecie.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
Przez siedem dni przaśniki jeść będziecie, a pierwszego dnia zaraz wypróżnicie kwas z domów waszych; bo ktobykolwiek jadł co kwaszonego od pierwszego dnia aż do dnia siódmego, wytracona będzie dusza ona z Izraela.
16 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
W tenże dzień pierwszy będzie zebranie święte, także dnia siódmego zgromadzenie święte mieć będziecie; żadnej roboty nie będziecie w nich czynić, oprócz tego, czego każdy do jedzenia używa, to samo gotować będziecie.
17 “Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
I będziecie przestrzegać przaśników; albowiem w ten dzień wywiodłem wojska wasze z ziemi Egipskiej; przetoż przestrzegać będziecie dnia tego w narodziech waszych ustawą wieczną.
18 Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
Pierwszego miesiąca, czternastego dnia tegoż miesiąca, na wieczór jeść będziecie przaśniki aż do dnia dwudziestego pierwszego tegoż miesiąca na wieczór.
19 Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
Przez siedem dni kwas niech się nie znajduje w domach waszych; bo ktobykolwiek jadł co kwaszonego, wytracona będzie dusza jego z zgromadzenia Izraelskiego, tak przychodzień, jako i zrodzony w ziemi.
20 Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
Nic kwaszonego jeść nie będziecie; we wszystkich mieszkaniach waszych jeść będziecie przaśniki.
21 Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
Wezwał tedy Mojżesz wszystkich starszych Izraelskich, i rzekł do nich: Odłączcie, a weźmijcie sobie baranka według familii swych, a zarznijcie na święto przejścia.
22 Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
Weźmiecie też snopek hysopu, i omoczycie we krwi, która będzie w miednicy, a pokropicie odrzwi, i oba podwoje oną krwią, która będzie w miednicy; a z was nie wynijdzie żaden ze drzwi domu swego aż do poranku.
23 Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
Bo przejdzie Pan zabijając Egipt; a ujrzawszy krew na odrzwiach i na obu podwojach, przestąpi Pan drzwi, i nie dopuści morderzowi, wchodzić do domów waszych zabijać was.
24 “Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
I przestrzegać będziecie tego za ustawę, tobie i synom twoim aż na wieki.
25 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
A gdy wnijdziecie do ziemi, którą wam da Pan, jako obiecał, tych obrzędów przestrzegać będziecie.
26 Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
A gdy wam rzeką synowie wasi: Co to za obrzędy wasze?
27 Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
Tedy rzeczecie: Ofiara to przejścia Pańskiego, który przestępował domy synów Izraelskich w Egipcie, gdy zabijał Egipt, a domy nasze wyzwalał. Zatem schylił się lud, i pokłonił się.
28 Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
I poszedłszy uczynili synowie Izraelscy, jako rozkazał Pan Mojżeszowi i Aaronowi, tak uczynili.
29 Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
I stało się o północy, że Pan zabijał wszystkie pierworodztwa w ziemi Egipskiej, i od pierworodnego Faraonowego, siedzącego na stolicy jego, aż do pierworodnego więźnia, który był w więzieniu, i wszelkie pierworodne z bydląt.
30 Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
Zatem wstał Farao onej nocy, i wszyscy słudzy jego, i wszystek Egipt, i wszczął się wielki krzyk w Egipcie; bo nie było domu, w którym by nie był umarły.
31 Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
A wezwawszy Farao Mojżesza i Aarona w nocy, rzekł: Wstańcie, wynijdźcie z pośrodku ludu mego, i wy i synowie Izraelscy, a poszedłszy służcie Panu, jakoście mówili.
32 Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
Nadto trzody wasze, i bydła wasze zabierzcie, jakoście żądali, a odchodząc, mnie też błogosławcie.
33 Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
I przynaglali Egipczanie ludowi, aby ich co rychlej wyprawili z ziemi; bo mówili: Pomrzemy wszyscy.
34 Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
Wziął tedy lud ciasta swe, pierwej niż zakisiały; a one ciasta swe uwinąwszy w szaty swe, kładli na ramiona swoje.
35 Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
Tedy synowie Izraelscy uczynili według rozkazania Mojżeszowego, i wypożyczali u Egipczan naczynia srebrnego, i naczynia złotego, i szat.
36 Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
A Pan dał łaskę ludowi w oczach Egipczanów, że im pożyczali; i złupili Egipt.
37 Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
Ciągnęli tedy synowie Izraelscy z Rameses do Suchotu, około sześć kroć sto tysięcy pieszych mężów tylko, okrom dzieci.
38 Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
Ale i ludu pospolitego wiele szło z nimi, i owiec, i bydła, dobytek bardzo wielki.
39 Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
I popiekli z ciasta zadziałanego, które wynieśli z Egiptu, placki przaśne; bo nie było zakwaszone, przeto że wygnani byli z Egiptu, a nie mogli zmieszkać; żywności też sobie byli nie przygotowali.
40 Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
A czasu mieszkania synów Izraelskich, którego mieszkali w Egipcie, było cztery sta lat, i trzydzieści lat.
41 Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
I stało się po czterech set lat i trzydziestu lat, stało się onegoż dnia, wyszły wszystkie wojska Pańskie z ziemi Egipskiej.
42 Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
Noc ta obchodzona ma być Panu, że je wywiódł ze ziemi Egipskiej. Ta tedy noc Panu obchodzona ma być od wszystkich synów Izraelskich w narodziech ich.
43 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
I rzekł Pan do Mojżesza i do Aarona: Ta jest ustawa święta przejścia: Żaden obcy nie będzie jadł z niego.
44 Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
Przetoż każdego sługę waszego, a za pieniądze kupionego, obrzeżecie go, tedy będzie jadł z niego.
45 Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
Przychodzień i najemnik nie będzie jadł z niego.
46 “Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
W domu jednym będzie jedzony; nie wyniesiesz nic z domu z mięsa jego, a kości nie złamiecie w nim.
47 Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
Wszystko zgromadzenie Izraelskie tak uczyni z nim.
48 “Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
A jeźliby kto z przychodniów był gościem u ciebie, i chciałby obchodzić święto przejścia Panu, pierwej obrzezany będzie każdy mężczyzna jego, a zatem przystąpi obchodzić je, i będzie jako urodzony w ziemi. A ktobykolwiek nie był obrzezany, nie będzie jadł z niego.
49 Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
Prawo jedno będzie w ziemi urodzonemu i przychodniowi, który jest gościem między wami.
50 “Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
Uczynili tedy wszyscy synowie Izraelscy, jako rozkazał Pan Mojżeszowi i Aaronowi, tak uczynili.
51 Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”
I stało się onegoż dnia, wywiódł Pan syny Izraelskie z ziemi Egipskiej z wojski ich.

< Eksodo 12 >