< Eksodo 12 >

1 Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni elizweni leGibhithe, isithi:
2 “Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
Le inyanga kayibe kini yinhloko yezinyanga, ibe kini ngeyokuqala yenyanga zomnyaka.
3 Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
Khulumani kunhlangano yonke yakoIsrayeli lithi: Ngolwetshumi lwalinyanga bazazithathela ngulowo iwundlu, ngokwezindlu zaboyise, iwundlu ngendlu.
4 Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
Uba-ke indlu incinyane kakhulu ewundlwini, kakuthi yena athathe lomakhelwane wakhe, oseduze lendlu yakhe, njengobunengi bemiphefumulo; ngulowo njengokudla kwakhe, lizabalela iwundlu.
5 Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
Lizakuba lezinyane elingelasici, eliduna, elilomnyaka owodwa; lithatheni ezimvini loba ezimbuzini.
6 Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
Njalo lizaligcina kuze kufike usuku lwetshumi lane lwaleyonyanga, njalo ibandla lonke lenhlangano yakoIsrayeli izalihlaba kusihlwa.
7 Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
Bazathatha-ke okwegazi, bakufake emigubazini yomibili lekhothameni, ezindlini abazalidlela kuzo.
8 Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
Njalo bazakudla inyama ngalobobusuku, yosiwe ngomlilo, lesinkwa esingelamvubelo, lemibhida ebabayo bazayidla.
9 Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
Lingadli okwalo kuluhlaza kumbe kuphekiwe lokuphekwa ngamanzi, kodwa yosiwe ngomlilo; inhloko yalo lemilenze yalo, kanye lemibilini yalo.
10 Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
Njalo lingatshiyi lutho kulo kuze kube sekuseni, kodwa okusalayo kulo kuze kube sekuseni lizakutshisa ngomlilo.
11 Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
Ngokunjalo-ke lizalidla, inkalo zenu zibotshiwe, izicathulo zenu zisenyaweni zenu, lendondolo zenu zisezandleni zenu; lizalidla ngokuphangisa; kuliphasika leNkosi.
12 “Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
Ngoba ngizadabula phakathi kwelizwe leGibhithe ngalobubusuku, ngitshaye wonke amazibulo elizweni leGibhithe, kusukela emuntwini kusiya enyamazaneni, ngizakwenza izigwebo kubo bonke onkulunkulu beGibhithe; mina ngiyiNkosi.
13 Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
Legazi lizakuba kini yisibonakaliso ezindlini lapho elikhona; nxa ngibona igazi ngizadlula phezu kwenu, njalo kungehleli kini inhlupheko yokuchitha, mhla ngitshaya ilizwe leGibhithe.
14 “Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
Njalo lolusuku luzakuba kini yisikhumbuzo; njalo lizalugcina lube ngumkhosi eNkosini; lizalugcina ezizukulwaneni zenu ngokomthetho wanininini.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
Insuku eziyisikhombisa lizakudla isinkwa esingelamvubelo. Yebo ngosuku lokuqala lizakhupha imvubelo ezindlini zenu; ngoba wonke odla okuvutshelweyo kusukela kusuku lokuqala kuze kufike usuku lwesikhombisa, lowomphefumulo uzaqunywa usuke koIsrayeli.
16 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
Njalo ngosuku lokuqala kuzakuba khona inhlangano ebiziweyo engcwele, langosuku lwesikhombisa lizakuba lenhlangano ebiziweyo engcwele; kungenziwa msebenzi ngazo, kuphela lokho wonke umphefumulo okudlayo, lokho kodwa kungenziwa yini.
17 “Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
Ngakho gcinani izinkwa ezingelamvubelo; ngoba ngalona lolosuku ngikhuphile amabutho enu elizweni leGibhithe. Ngakho lizagcina lolosuku ezizukulwaneni zenu ngesimiso saphakade.
18 Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
Kweyokuqala, osukwini lwetshumi lane lwenyanga kusihlwa lizakudla isinkwa esingelamvubelo, kuze kufike usuku lwamatshumi amabili lanye lwenyanga kusihlwa.
19 Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
Insuku eziyisikhombisa kakungaficwa imvubelo ezindlini zenu; ngoba wonke odla okuvutshelweyo lowomphefumulo uzaqunywa usuke kunhlangano yakoIsrayeli, loba engowemzini loba engowokuzalwa elizweni.
20 Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
Lingadli lutho oluvutshelweyo; emizini yenu yonke lizakudla isinkwa esingelamvubelo.
21 Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
UMozisi wasebiza bonke abadala bakoIsrayeli, wathi kubo: Hudulani lizithathele amawundlu ngokwensapho zenu, lihlabe iphasika,
22 Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
lithathe ilixha lehisope, liligxamuze egazini elisemganwini, lininde ekhothameni lemigubazini emibili ngegazi elisemganwini; lina-ke, kakungaphumi muntu endlini yakhe kuze kube sekuseni.
23 Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
Ngoba iNkosi izadabula ukutshaya amaGibhithe; nxa ibona igazi ekhothameni lemigubazini yomibili, iNkosi izadlula phezu komnyango, ingavumeli umchithi ukuthi angene ezindlini zenu ukutshaya.
24 “Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
Njalo lizagcina le into, kube yisimiso kini lakubantwana benu kuze kube phakade.
25 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
Njalo kuzakuthi lapho lifika elizweni iNkosi ezalinika lona njengokukhuluma kwayo, lizagcina linkonzo.
26 Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
Kuzakuthi-ke lapho abantwana benu besithi kini: Iyini linkonzo elilayo?
27 Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
Lizakuthi-ke: Lo ngumhlatshelo wephasika leNkosi, eyedlula phezu kwezindlu zabantwana bakoIsrayeli eGibhithe mhla itshaya amaGibhithe, wophula izindlu zethu. Njalo abantu bakhothama bakhonza.
28 Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
Abantwana bakoIsrayeli basebehamba, bayakwenza njengalokhu iNkosi yayibalayile oMozisi loAroni, benza njalo.
29 Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
Kwasekusithi phakathi kobusuku iNkosi yatshaya wonke amazibulo elizweni leGibhithe, kusukela kuzibulo likaFaro elalizahlala esihlalweni sakhe sobukhosi kuze kube kuzibulo lesibotshwa esasisentolongweni, lamazibulo wonke ezifuyo.
30 Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
UFaro wasesukuma ebusuku, yena lenceku zakhe zonke lamaGibhithe wonke. Kwasekusiba khona isililo esikhulu eGibhithe, ngoba kwakungekho ndlu lapho okwakungelamufi khona.
31 Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
Wasebiza oMozisi loAroni ebusuku, wathi: Sukumani, liphume phakathi kwabantu bami, lonke lina labantwana bakoIsrayeli, lihambe liyekhonza iNkosi njengokutsho kwenu.
32 Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
Thathani lani izimvu zenu lenkomo zenu njengokutsho kwenu, lihambe; futhi lingibusise lami.
33 Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
Njalo amaGibhithe ayebakhuthaza abantu ebahaluzelisa ukuthi baphume elizweni, ngoba athi: Sonke sifile.
34 Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
Abantu-ke bathatha inhlama yabo ingakavutshelwa, betshata imiganu yabo yokuxovela ibotshelwe ezembathweni zabo.
35 Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
Abantwana bakoIsrayeli basebesenza njengelizwi likaMozisi; bacela kumaGibhithe izinto zesiliva lezinto zegolide lezigqoko.
36 Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
INkosi yasibapha abantu umusa emehlweni amaGibhithe, aze abanika izicelo zabo. Basebewaphundla amaGibhithe.
37 Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
Abantwana bakoIsrayeli basebesuka eRamesesi besiya eSukothi; amadoda angaba zinkulungwane ezingamakhulu ayisithupha ahamba ngenyawo, ngaphandle kwabantwana.
38 Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
Kwasekusenyuka labo lexuku lenhlobonhlobo, lezimvu lezinkomo, lezifuyo ezinengi kakhulu.
39 Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
Basebebhaka izinkwa ezingelamvubelo ngenhlama abayikhupha eGibhithe, ngoba ingavutshelwanga, ngoba baxotshwa eGibhithe, ngoba babengelakulibala, futhi bengazilungiselelanga umphako.
40 Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
Isikhathi sokuhlala-ke kwabantwana bakoIsrayeli abasihlala eGibhithe sasiyiminyaka engamakhulu amane lamatshumi amathathu.
41 Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
Kwasekusithi ekupheleni kweminyaka engamakhulu amane lamatshumi amathathu, kwathi ngalona lolosuku wonke amabutho eNkosi aphuma elizweni leGibhithe.
42 Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
Kuyibusuku bemilindo eNkosini ngokubakhupha elizweni leGibhithe; lobu yibusuku beNkosi bemilindo yabo bonke abantwana bakoIsrayeli ezizukulwaneni zabo.
43 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
INkosi yasisithi kuMozisi loAroni: Lesi yisimiso sephasika. Kakho owezizwe ongalidla;
44 Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
kodwa sonke isigqili sawo wonke umuntu, esathengwa ngemali, nxa usisokile, ngalesosikhathi sizakudla kulo.
45 Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
Owezizwe loqhatshiweyo bangadli kulo.
46 “Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
Lizadlelwa endlini yinye; ungakhupheli phandle kwendlu okwenyama, ungephuli thambo lalo.
47 Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
Inhlangano yonke yakoIsrayeli izakwenza lokhu.
48 “Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
Uba owemzini ohlala lani njengowezizwe egcinela iNkosi iphasika, kabasokwe bonke abesilisa laye, abesesondela-ke aligcine, uzakuba njengowokuzalwa elizweni; kodwa kakho ongasokwanga ozalidla.
49 Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
Umlayo munye uzakuba kowokuzalwa elizweni lakowemzini ohlala phakathi kwenu njengowezizwe.
50 “Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
Bonke abantwana bakoIsrayeli basebesenza njengalokhu iNkosi yayibalayile oMozisi loAroni; benza njalo.
51 Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”
Kwasekusithi ngalona lolosuku iNkosi yabakhupha abantwana bakoIsrayeli elizweni leGibhithe ngamabutho abo.

< Eksodo 12 >