< Eksodo 12 >

1 Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
Now the LORD spoke to Moses and Aaron in the land of Egypt, saying,
2 “Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
"This month shall be to you the beginning of months. It shall be the first month of the year to you.
3 Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
Speak to all the congregation of Israel, saying, 'On the tenth day of this month, they shall take to them every man a lamb, according to their fathers' houses, a lamb for a household;
4 Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
and if the household is too little for a lamb, then he and his neighbor next to his house shall take one according to the number of the souls; according to what everyone can eat you shall make your count for the lamb.
5 Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
Your lamb shall be without blemish, a male in its first year. You shall take it from the sheep, or from the goats:
6 Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
and you shall keep it until the fourteenth day of the same month; and the whole assembly of the congregation of Israel shall kill it at evening.
7 Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
They shall take some of the blood, and put it on the two doorposts and on the lintel, on the houses in which they shall eat it.
8 Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
They shall eat the flesh in that night, roasted with fire, and unleavened bread. They shall eat it with bitter herbs.
9 Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
Do not eat it raw, nor boiled at all with water, but roasted with fire; with its head, its legs and its inner parts.
10 Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
You shall let nothing of it remain until the morning; but that which remains of it until the morning you shall burn with fire.
11 Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
This is how you shall eat it: with your waist girded, your shoes on your feet, and your staff in your hand; and you shall eat it in haste: it is the LORD's Passover.
12 “Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
For I will go through the land of Egypt in that night, and will strike all the firstborn in the land of Egypt, both man and animal. Against all the gods of Egypt I will execute judgments: I am the LORD.
13 Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
The blood shall be to you for a token on the houses where you are: and when I see the blood, I will pass over you, and there shall no plague be on you to destroy you, when I strike the land of Egypt.
14 “Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
This day shall be to you for a memorial, and you shall keep it a feast to the LORD: throughout your generations you shall keep it a feast by an ordinance forever.
15 Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
"'Seven days you shall eat unleavened bread; even the first day you shall put away yeast out of your houses, for whoever eats leavened bread from the first day until the seventh day, that soul shall be cut off from Israel.
16 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
In the first day there shall be to you a holy convocation, and in the seventh day a holy convocation; no manner of work shall be done in them, except that which every man must eat, that only may be done by you.
17 “Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
You shall observe the feast of unleavened bread; for in this same day have I brought your regiments out of the land of Egypt: therefore you shall observe this day throughout your generations by an ordinance forever.
18 Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
In the first month, on the fourteenth day of the month at evening, you shall eat unleavened bread, until the twenty first day of the month at evening.
19 Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
For seven days yeast must not be found in your houses, for whoever eats that which is leavened, that person must be cut off from the congregation of Israel, whether he is a foreigner, or one who is born in the land.
20 Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
You must eat nothing leavened. In all your places where you live you must eat unleavened bread.'"
21 Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
Then Moses called for all the elders of the children of Israel, and said to them, "Go and select lambs according to your clans, and kill the Passover lamb.
22 Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
And you are to take a bunch of hyssop and dip it in the blood that is in the basin, and apply it on the top and on both sides of the doorframe with the blood that is in the basin. And none of you is to go out of the door of his house until morning.
23 Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
For the LORD will pass through to strike the Egyptians, and when he sees the blood on the top and sides of the doorframe, the LORD will pass over the door and will not allow the destroyer to enter your houses to strike you.
24 “Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
And you must observe this as an ordinance for you and your children forever.
25 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
And it shall come to pass when you enter the land which the LORD will give you, as he has promised, you must keep this ceremony.
26 Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
And it shall be, when your children ask you, 'What do you mean by this ceremony?'
27 Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
that you shall say, 'It is the sacrifice of the LORD's Passover, because he passed over the houses of the children of Israel in Egypt, when he struck the Egyptians but spared our houses.'" And the people bowed down and worshiped.
28 Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
Then the children of Israel went away and did as the LORD had commanded Moses and Aaron, so they did.
29 Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
And it came to pass at midnight that the LORD killed all the firstborn in the land of Egypt, from the firstborn of Pharaoh who sat on his throne to the firstborn of the prisoner who was in the prison, and all the firstborn of livestock.
30 Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
And Pharaoh got up during the night, he, and all his servants, and all Egypt, and there was loud wailing in Egypt, for there was not a house where there was not someone dead.
31 Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
Then he summoned for Moses and Aaron during the night, and said, "Get up, get out from among my people, both you and the children of Israel; and go, serve the LORD, as you have requested.
32 Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
Take your flocks and your herds, as you have requested, and be gone, but bless me also."
33 Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
The Egyptians were urgent with the people to send them out of the land quickly, for they said, "We will all be dead."
34 Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
So the people took their dough before it was leavened, with their kneading bowls wrapped in their clothing on their shoulders.
35 Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
Now the children of Israel did according to what Moses told them, for they had asked the Egyptians for articles of silver and articles of gold and clothing.
36 Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
And the LORD gave the people favor in the sight of the Egyptians, and they gave them whatever they wanted. And so they plundered Egypt.
37 Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
And the children of Israel traveled from Rameses to Succoth, about six hundred thousand men on foot, besides their dependents.
38 Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
And a mixed crowd also went up with them, and a huge number of livestock, both flocks and herds.
39 Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
And they baked unleavened loaves using the dough that they had brought out of Egypt; for it wasn't leavened, because they were thrust out of Egypt, and couldn't wait, nor had they prepared any provisions for themselves.
40 Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
Now the time that the children of Israel lived in Egypt was four hundred and thirty years.
41 Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
And it came to pass at the end of four hundred thirty years, to the day, it came to pass that all the regiments of the LORD went out from the land of Egypt.
42 Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
It was a night when the LORD kept vigil to bring them out from the land of Egypt. So on this night all the children of Israel must keep a vigil to the LORD throughout their generations.
43 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
And the LORD said to Moses and Aaron, "This is the ordinance of the Passover. No foreigner may eat of it,
44 Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
but every man's servant who is bought for money, after you have circumcised him, may he eat of it.
45 Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
A foreigner and a hired servant must not eat of it.
46 “Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
It is to be eaten in one house. You must not take any of the meat outside the house, and you are not to break any of its bones.
47 Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
All the congregation of Israel is to keep it.
48 “Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
If a foreigner lives with you and wants to keep the Passover to the LORD, all his males must be circumcised, and then he may take part and observe it, and he will be like one who is born in the land. But no uncircumcised person may eat of it.
49 Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
The same law will apply to the native-born and to the foreigner who lives among you."
50 “Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
So all the children of Israel did as the LORD commanded Moses and Aaron, so they did.
51 Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”
And it happened on this very day that the LORD brought the children of Israel out of the land of Egypt by their regiments.

< Eksodo 12 >