< Eksodo 11 >
1 Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
Amalalu, Hina Gode da Mousesema amane sia: i, “Na da Felou (Idibidi hina bagade) amola ea fi dunu ilima eno afae fawane se nabasu imunu. Amo ba: sea, e da dili fisidigimu. Amo baligili, e da dili gadili sefasimu.
2 Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
Be wali Isala: ili dunuma sia: ma. Ilia da Idibidi na: iyado ilima gouli, silifa amola muni liligi ilima ima: ne sia: ma.”
3 Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
Hina Gode da Idibidi dunu ilia asigi dawa: su afadenene, ilia da Isala: ili dunuma nodone dawa: i. Idibidi eagene ouligisu dunu amola dunu huluane da Mousese da dunu mimogo bagadedafa dawa: i.
4 Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
Amalalu, Mousese da Felouma amane sia: i, “Hina Gode da amane sia: sa, ‘Na da gasimogoa gadenene Idibidi soge ganodini lafidalomusa: masunu.
5 Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
Amola magobo mano huluane Idibidi soge ganodini esalebe da bogogia: mu. Felou ea magobo mano (e da fa: no Idibidi hina bagade hamomu galu) amola udigili hawa: hamosu uda (amo da gagoma goudasa) ilia magobo mano huludafa da bogogia: mu. Amola bulamagau huluane ilia magobo mano da bogomu.
6 Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
Idibidi soge ganodini didigia: su bagadedafa nabimu. Agoai didigia: su da musa: hame ba: i amola hobea bu hamedafa ba: mu.
7 Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
Be Isala: ili fi da se hame nabimu. Wa: me da ilima amola ilia ohe fi ilima hame yeyamu. Amasea, Na da Isala: ili dunu da hisu amola Idibidi dunu da hisu amo ba: sa, amo dilia da dawa: mu.”
8 Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
Mousese da ea sia: dagomusa: , amane sia: i, “Dia ouligisu hina dunu huluane da nama misini, nama beguduli, na da na fi dunu lale gadili oule masa: ne nama ha: giwane edegemu. Amalalu, na da yolesili masunu.” Amalalu, Mousese da bagadewane ougili, Felou yolesili asi.
9 Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
Be Hina Gode da musa: Mousesema sia: i dagoi, “Felou da mae fisili, dia sia: hamedafa nabimu. Bai Na da Idibidi soge ganodini Na musa: hame ba: su hou eno amo soge ganodini hamomu galebe.”
10 Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.
Mousese amola Elane da amo musa: hame ba: su hou huluane Felou ba: ma: ne hamosu. Be Hina Gode da ea hou gawamaga: i agoane hamoi. Amola e da Isala: ili dunu ea soge fisili gadili masa: ne hame fisidigi.