< Eksodo 10 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao, pakuti Ine ndawumitsa mtima wake ndi mitima ya nduna zake kuti ndichite zizindikiro zozizwitsa pakati pawo
А Господ рече Мојсију: Иди к Фараону, јер сам ја учинио да отврдне срце његово и срце слуга његових, да учиним ове знаке своје међу њима,
2 kuti inu mudzawuze ana ndi zidzukulu zanu za mmene ndinawakhawulitsira Aigupto ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinachita pakati pawo ndiponso kuti inu mudziwe kuti ine ndine Yehova.”
И да приповедаш синовима својим и унуцима својим шта учиних у Мисиру и какве знаке своје показах на њима, да бисте знали да сам ја Господ.
3 Ndipo Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kukanena kuti, “Yehova Mulungu wa Ahebri, akuti: ‘Kodi udzakanabe kudzichepetsa pamaso panga mpaka liti? Alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
И отиде Мојсије и Арон к Фараону, и рекоше му: Овако вели Господ Бог јеврејски: Докле ћеш се противити да се не понизиш преда мном? Пусти народ мој да ми послужи.
4 Ngati ukana kuwalola, ndigwetsa dzombe mʼdziko lako lino mawa.
Јер ако нећеш пустити народ мој, ево сутра ћу нанети скакавце на земљу твоју;
5 Dzombeli lidzakuta nthaka yonse moti sidzaoneka konse. Lidzadya kalikonse kakangʼono kamene sikanawonongedwe ndi matalala aja, kuphatikizapo mitengo yonse imene ikumera mʼminda yanu.
И покриће сву земљу да се неће видети земља, и појешће остатак што се сачувао, који вам је остао иза града, и појешће сва дрвета што вам расту у пољу.
6 Dzombeli lidzadzaza nyumba zako ndi za nduna zako ndiponso za Aigupto onse, chinthu chimene ngakhale makolo anu kapena makolo awo sanachionepo kuyambira tsiku limene anakhala mʼdzikoli mpaka lero.’” Ndipo Mose ndi Aaroni anatembenuka ndi kumusiya Farao.
И напуниће их се куће твоје и куће свих слуга твојих и куће свих Мисираца, шта нису видели оци твоји ни оци отаца твојих, откако су постали на земљи до данас. И окренувши се отиде од Фараона.
7 Nduna za Farao zinamufunsa kuti, “Kodi munthu uyu adzativutitsa mpaka liti? Aloleni anthuwa apite, kuti akapembedze Yehova Mulungu wawo. Kodi simukuona kuti dziko la Igupto lawonongeka?”
А слуге рекоше Фараону: Докле ће нас тај мучити? Пусти их нека послуже Господу Богу свом. Зар још не видиш где пропаде Мисир?
8 Choncho Mose ndi Aaroni anayitanidwanso kwa Farao ndipo anati, “Pitani kapembedzeni Yehova Mulungu wanu. Koma ndani amene adzapite?”
И дозваше опет Мојсија и Арона пред Фараона, и рече им: Идите, послужите Господу Богу свом. А који су што ће ићи?
9 Mose anayankha kuti, “Ife tidzapita tonse pamodzi; angʼonoangʼono ndi akuluakulu, ana athu aamuna ndi aakazi, ndiponso ziweto zathu ndi ngʼombe chifukwa tikakhala ndi chikondwerero cha kwa Yehova.”
А Мојсије рече: С децом својом и са старцима својим ићи ћемо, са синовима својим и са кћерима својим, са стоком својом ситном и крупном ићи ћемо, јер имамо празник Господњи.
10 Farao anati, “Yehova akhale ndi inu ngati ndingakuloleni kupita pamodzi ndi akazi ndi ana anu! Zikuoneka kuti mwakonzeka kuchita choyipa.
А он им рече: Тако био Господ с вама, како ћу вас ја пустити с децом вашом! Видите да зло мислите.
11 Ndakana! Amuna okha ndiwo apite ndi kukapembedza Yehova pakuti izi ndi zimene mwakhala mukupempha.” Kenaka Mose ndi Aaroni anathamangitsidwa pamaso pa Farao.
Неће бити тако; него ви људи идите и послужите Господу, јер то иштете. И отера их од себе Фараон.
12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Tambalitsa dzanja lako pa dziko la Igupto kuti dzombe lidze pa dziko la Igupto ndi kuwononga chilichonse chimene chikumera mʼminda ndi chilichonse chimene chinatsala pa nthawi ya matalala.”
Тада рече Господ Мојсију: Пружи руку своју на земљу мисирску, да дођу скакавци на земљу мисирску и поједу све биље по земљи, шта год оста иза града.
13 Kotero Mose anakweza ndodo yake pa dziko la Igupto, ndipo Yehova anawutsa mphepo ya kummawa imene inawomba pa dziko usana ndi usiku wonse. Mmene kumacha nʼkuti mphepoyo itabweretsa dzombe.
И пружи Мојсије штап свој на земљу мисирску, и Господ наведе устоку на земљу, те дува цели дан и целу ноћ; а кад свану, донесе устока скакавце.
14 Dzombelo linafika pa dziko lonse la Igupto ndi kukhala dera lililonse la dzikolo. Dzombe lambiri ngati limenelo silinakhaleponso nʼkale lonse ndipo silidzakhalapo ngakhale mʼtsogolo.
И дођоше скакавци на сву земљу мисирску, и попадаше по свим крајевима мисирским силни веома, каквих пре никада није било нити ће кад бити онаквих.
15 Dzombelo linaphimba nthaka yonse mpaka kuoneka kuti bii. Linadya zonse zimene zinatsala nthawi ya matalala, zomera za mʼmunda ndi zipatso. Panalibe chobiriwira chilichonse chimene chinatsala pa mtengo kapena pa chomera chilichonse mʼdziko lonse la Igupto.
И покрише сву земљу, да се земља не виђаше, и поједоше сву траву на земљи и сав род на дрветима, што оста иза града, и не оста ништа зелено од дрвета и од биља пољског у свој земљи мисирској.
16 Mwamsangamsanga, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Ine ndachimwira Yehova Mulungu wanu ndiponso inu.
Тада Фараон брже дозва Мојсија и Арона, и рече: Згреших Господу Богу вашем и вама.
17 Tsopano ndikhululukirenso tchimo langa kano konkha ndipo pempherani kwa Yehova Mulungu wanu kuti andichotsere mliri wosakazawu.”
Али ми још сада само опрости грех мој, и молите се Господу Богу свом да уклони од мене само ову смрт.
18 Mose anachoka kwa Farao nakapemphera kwa Yehova.
И отиде Мојсије од Фараона, и помоли се Господу.
19 Ndipo Yehova anasintha mphepo ija kuti ikhale ya mphamvu yochokera ku madzulo, ndipo inanyamula dzombe lija nʼkulikankhira mʼNyanja Yofiira. Panalibe dzombe ndi limodzi lomwe limene linatsala mu Igupto.
И окрену Господ ветар од запада врло јак, који узе скакавце и баци их у Црвено море, и не оста ниједан скакавац у целој земљи мисирској.
20 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli apite.
Али Господ учини те отврдну срце Фараону, и не пусти синове Израиљеве.
21 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasulira dzanja lako kumwamba kuti kukhale mdima umene udzaphimba dziko lonse la Igupto, mdima wandiweyani.”
И рече Господ Мојсију: Пружи руку своју к небу, и биће тама по земљи мисирској таква да ће је пипати.
22 Choncho Mose anakweza dzanja lake kumwamba ndipo mdima wandiweyani unaphimba dziko lonse la Igupto kwa masiku atatu.
И Мојсије пружи руку своју к небу, и поста густа тама по свој земљи мисирској за три дана.
23 Palibe amene anatha kuona mnzake kapena kuchoka pa khomo pake kwa masiku atatu. Koma kumalo kumene kumakhala Aisraeli kunali kowala.
Не виђаху један другог, и нико се не маче с места где беше за три дана; али се код свих синова Израиљевих видело по становима њиховим.
24 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kapembedzeni Yehova. Ngakhale akazi ndi ana anu apite pamodzi ndi inu. Koma musatenge ziweto zanu ndi ngʼombe zanu.”
Тада Фараон дозва Мојсија, и рече: Идите, послужите Господу; само стока ваша ситна и крупна нека остане, а деца ваша нека иду с вама.
25 Koma Mose anati, “Ndiye inu mutipatse nsembe zopsereza zoti tikapereke kwa Yehova Mulungu wathu.
А Мојсије рече: Треба да нам даш и шта ћемо принети и сажећи на жртву Господу Богу свом;
26 Koma ayi, ife tipita ndi ziweto zathu. Palibe chiweto chilichonse chimene chitatsale kuno, popeza tikasankha komweko ziweto zokapembedzera Yehova. Sitingadziwe zimene tikagwiritse ntchito popembedza Yehova mpaka titakafika kumeneko.”
Зато и стока наша нек иде с нама, да не остане ни папка, јер између ње треба да узмемо чим ћемо послужити Господу Богу свом, а не знамо којим ћемо послужити Господу докле не дођемо онамо.
27 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo sanafune kuwalola kuti apite.
Али Господ учини те отврдну срце Фараону, и не хте их пустити.
28 Farao anati kwa Mose, “Choka pamaso panga! Uwonetsetse kuti usadzaonekerenso pamaso panga! Tsiku limene ndidzakuonenso udzafa.”
И рече му Фараон: Иди од мене, и чувај се да ми више не дођеш на очи, јер ако ми дођеш на очи, погинућеш.
29 Mose anayankha kuti, “Monga momwe mwaneneramu, Ine sindidzaonekeranso pamaso panu.”
А Мојсије рече: Право си казао; нећу ти више доћи на очи.

< Eksodo 10 >