< Eksodo 1 >
1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Et ce sont ici les noms des fils d’Israël qui entrèrent en Égypte; ils y entrèrent avec Jacob, chacun avec sa famille:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Ruben, Siméon, Lévi et Juda;
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issacar, Zabulon et Benjamin;
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan et Nephthali; Gad et Aser.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Et toutes les âmes issues des reins de Jacob étaient 70 âmes; or Joseph était en Égypte.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
Et Joseph mourut, et tous ses frères, et toute cette génération-là.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
Et les fils d’Israël fructifièrent et foisonnèrent, et multiplièrent, et devinrent extrêmement forts; et le pays en fut rempli.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Et un nouveau roi se leva sur l’Égypte, qui n’avait point connu Joseph.
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
Et il dit à son peuple: Voici, le peuple des fils d’Israël est plus nombreux et plus fort que nous.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Allons, soyons prudents à son égard, de peur qu’il ne se multiplie, et que, s’il arrivait une guerre, il ne se joigne, lui aussi, à nos ennemis, et ne fasse la guerre contre nous, et ne monte hors du pays.
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
Et ils établirent sur lui des chefs de corvées pour l’opprimer par leurs fardeaux. Et il bâtit pour le Pharaon des villes à greniers, Pithom et Ramsès.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
Et selon qu’ils l’opprimaient, il multipliait et croissait; et ils eurent peur des fils d’Israël.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
Et les Égyptiens firent servir les fils d’Israël avec dureté,
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
et ils leur rendirent la vie amère par un dur service, en argile, et en briques, et par toute sorte de service aux champs: tout le service dans lequel on les faisait servir était avec dureté.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
Et le roi d’Égypte parla aux sages-femmes hébreues, dont l’une avait nom Shiphra et la seconde se nommait Pua,
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
et il dit: Quand vous accoucherez les femmes hébreues et que vous les verrez sur les sièges, si c’est un fils, vous le ferez mourir, et si c’est une fille, elle vivra.
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
Mais les sages-femmes craignirent Dieu, et ne firent pas comme le roi d’Égypte leur avait dit; et elles laissèrent vivre les enfants mâles.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
Et le roi d’Égypte appela les sages-femmes, et leur dit: Pourquoi avez-vous fait cela, et avez-vous laissé vivre les enfants mâles?
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
Et les sages-femmes dirent au Pharaon: Parce que les femmes hébreues ne sont pas comme les Égyptiennes; car elles sont vigoureuses: avant que la sage-femme vienne vers elles, elles ont enfanté.
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Et Dieu fit du bien aux sages-femmes; et le peuple multiplia, et devint très fort.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
Et il arriva, parce que les sages-femmes craignirent Dieu, qu’il leur fit des maisons.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Et le Pharaon commanda à tout son peuple, disant: Tout fils qui naîtra, jetez-le dans le fleuve; mais toute fille, laissez-la vivre.