< Eksodo 1 >
1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Voici les noms des fils d'Israël qui vinrent en Égypte (chaque homme et sa famille vinrent avec Jacob):
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Ruben, Siméon, Lévi et Juda,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issacar, Zabulon et Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan et Nephtali, Gad et Asher.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Toutes les âmes qui sortirent du corps de Jacob étaient au nombre de soixante-dix, et Joseph était déjà en Égypte.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
Joseph mourut, ainsi que tous ses frères et toute cette génération.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
Les enfants d'Israël furent féconds, ils augmentèrent en abondance, ils se multiplièrent, ils devinrent extrêmement puissants, et le pays fut rempli d'eux.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Or, il se leva un nouveau roi sur l'Égypte, qui ne connaissait pas Joseph.
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
Il dit à son peuple: « Voici que le peuple des enfants d'Israël est plus nombreux et plus puissant que nous.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Venez, traitons-les avec sagesse, de peur qu'ils ne se multiplient et que, lorsqu'une guerre éclatera, ils ne se joignent à nos ennemis, ne nous combattent et ne s'échappent du pays. »
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
Ils établirent donc sur eux des maîtres de corvées pour les accabler de leurs fardeaux. Ils construisirent des villes de stockage pour Pharaon: Pithom et Raamsès.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
Mais plus ils les accablaient, plus ils se multipliaient et plus ils s'étendaient. Ils se mirent à redouter les enfants d'Israël.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
Les Égyptiens firent servir les enfants d'Israël sans pitié,
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
et ils leur rendirent la vie amère par un dur service dans le mortier et dans la brique, et par toutes sortes de services dans les champs, tous leurs services, dans lesquels ils les firent servir sans pitié.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
Le roi d'Égypte parla aux sages-femmes hébraïques, dont l'une s'appelait Shiphrah et l'autre Puah,
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
et il dit: « Lorsque vous exercerez la fonction de sage-femme auprès des femmes hébraïques et que vous les verrez sur l'escabeau, si c'est un fils, vous le tuerez; mais si c'est une fille, elle vivra. »
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
Mais les sages-femmes craignirent Dieu et ne firent pas ce que le roi d'Égypte leur avait ordonné, mais elles sauvèrent les petits garçons vivants.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
Le roi d'Égypte fit venir les sages-femmes et leur dit: « Pourquoi avez-vous fait cela et sauvé les garçons en vie? ».
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
Les sages-femmes dirent à Pharaon: « Parce que les femmes hébreues ne sont pas comme les Egyptiennes, car elles sont vigoureuses et accouchent avant que la sage-femme ne vienne les voir. »
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Dieu traita bien les sages-femmes, et le peuple se multiplia et devint très puissant.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
Comme les sages-femmes craignaient Dieu, il leur donna des familles.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Pharaon donna cet ordre à tout son peuple: « Vous jetterez dans le fleuve tout fils qui naîtra, et vous sauverez vivante toute fille. »