< Eksodo 1 >

1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
These are the names of the sons of Israel, who went into Egypt with Jacob. They entered, each one with his house:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Reuben, Simeon, Levi, Judah,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issachar, Zebulun, and Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan and Naphtali, Gad and Asher.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Therefore, all the souls of those who went forth from Jacob’s thigh were seventy. Now Joseph was in Egypt.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
When he had died, along with all of his brothers and all of that generation,
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
the sons of Israel increased, and they multiplied like seedlings. And having been strengthened exceedingly, they filled the land.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Meanwhile, there arose a new king over Egypt, who was ignorant of Joseph.
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
And he said to his people: “Behold, the people of the sons of Israel are many, and they are stronger than we are.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Come, let us wisely oppress them, lest they multiply; and if any war should advance against us, they may be added to our enemies, and having fought against us, they might depart from the land.”
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
And so he set over them masters of the works, in order to afflict them with burdens. And they built for Pharaoh the cities of the tabernacles: Pithom and Raamses.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
And the more they oppressed them, so much more did they multiply and increase.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
And the Egyptians hated the sons of Israel, and they afflicted them and mocked them.
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
And they led their life directly into bitterness, with hard work in clay and brick, and with all kinds of servitude, so that they were being overwhelmed with the works of the land.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
Then the king of Egypt spoke to the midwives of the Hebrews, (one of whom one was called Shiphrah, another Puah)
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
instructing them: “When you will act as a midwife to the Hebrew women, and the time of delivery has arrived: if it is male, put it to death; if it is female, retain it.”
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
But the midwives feared God, and so they did not act according to the precept of the king of Egypt, but they kept the males safe.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
And summoning them, the king said, “What did you intend to do, so that you would save the boys?”
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
They responded: “The Hebrew women are not like the Egyptian women. For they themselves have the wisdom of a midwife, and so they give birth before we can come to them.”
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Therefore, God acted favorably toward the midwives. And the people increased, and they were strengthened exceedingly.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
And because the midwives feared God, he built houses for them.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Therefore, Pharaoh instructed all his people, saying: “Whatever will be born of the male sex, cast it into the river; whatever will be born of the female sex, retain it.”

< Eksodo 1 >