< Eksodo 1 >

1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
以色列的兒子們,各帶了家眷,同雅各伯來到埃及;他們的名字記載如下:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
勒烏本、西默盎、勒末和猶大,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
依撒加爾,則步隆和本雅明丹,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
和納裴塔里,加得和阿協爾。
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
他們全是雅各伯所生的,一共七十人;若瑟那時已經在埃及。
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
若瑟和他的眾兄弟,以及這一代的人死了以後,
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
以色列的子孫生育繁殖,數目增多,極其強盛,佈滿了那地。受壓迫
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
有位不認識若瑟的新王興起,統治了埃及。
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
他對自己的人民說:「看以色列子民,比我們又多又強。
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
來,我們要用智謀對付他們,免得他們繁盛起來,一遇戰爭,就去與我們的敵人聯合,攻擊我們,然後離開此地。」
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
於是派定督工管制他們,以苦役壓迫他們,叫他們給法朗建築丕通和辣默色斯兩做貯貨城。
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
但是越壓迫他們,他們越增多,也越繁殖,以至埃及人都怕以色列子民。
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
於是埃及人更嚴厲地強迫以色列子民做苦工,
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
強迫他們作和泥做磚的苦工,田間的一切勞工,以及種種苦工,使他們的生活十分痛苦。殘害男嬰
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
埃及王又吩咐為希伯來女人接生的收生婆,一個名叫史斐辣,一個名叫普亞的說
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
「你們為希伯來女人接生時,要看著她們臨盆! 若是男孩,就殺死;若是女孩,就讓她活著。」
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
但是收生婆敬畏天主,沒有照埃及王的吩咐去作,保留了男孩的性命。
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
埃及王將收生婆召來,問她們說:「你們為什麼這樣做,竟叫男孩活著呢﹖」
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
‧收收婆回答法朗說:「希伯來女人和埃及女人不同,她們富有生機,收生婆還沒有來,她們已生產了。」
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
天主遂恩待了收生婆。以色列的子民更加增多起來,更加強盛。
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
因為收生婆敬畏天主,天主就使她們家門興旺。
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
法朗於是訓令他的全體人民說:「凡希伯來人所生的男孩,你們應把他丟在尼羅河裏;凡是女孩,留她活著! 」

< Eksodo 1 >