< Estere 1 >

1 Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
А в дните на Асуира, (оня Асуир, който царуваше от Индия дори до Етиопия над сто и двадесет и седем области),
2 Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
в ония дни, когато цар Асуир бе седнал на престола на царството си в столицата Суса,
3 ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
в третата година от царуването си, той направи угощение на всичките си първенци и на слугите си, (като пред него бяха най-силните персийски и мидийски мъже, големците и първенците на областта),
4 Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
Когато за дълго време, сто и осемдесет дни, показваше богатството на славното ти царство и блясъка на превъзходното си величие.
5 Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
И когато се изминаха тия дни, царят направи седемдневно угощение на всичките люде, които се намираха в столицата Суса, от голям до малък, в двора на градината на царския палат,
6 Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
Който бе украсил със завеси от бял, зелен и син плат, прострени на висонени и морави върви, окачени със сребърни колелца на мраморни стълбове, и със златни и сребърни канапета върху настилка от порфир и от бял мрамор, от алабастър и от черен мрамор.
7 Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
И наливаха им в златни чаши, (като бяха чашите различни едни от други); и имаше изобилно царско вино, както подобаваше на царя.
8 Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
А пиенето ставаше според една издадена заповед, че никой не бива да принуждава, защото царят беше заповядал така на всичките си домостроители, да постъпват според волята на всекиго.
9 Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
А и царица Астин направи на жените угощение в царската къща на царя Асуира.
10 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
А на седмия ден, когато сърцето на царя бе се развеселило от виното, той заповяда на Меумана, на Визата, на Арвона, на Вигта, на Авагта, на Зетара и на Харкаса, седемте скопци, които слугуваха пред цар Асуира,
11 kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
да доведат царица Астин пред царя, носеща царската корона, за да покаже хубостта й на людете и на първенците; защото тя бе красива на глед.
12 Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
Но царица Астин отказа да дойде по царската заповед чрез скопците; за това царят се разяри твърде много, и гневът му пламна в него.
13 Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
Тогава рече царят на мъдреците, които познаваха времената, (защото царят имаше обичай така да се носи спрямо всички, които знаеха закон и съд;
14 Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
А втори след него бяха Карсена, Сетар, Адмата, Тарсис, Мерес, Марсена и Мемукан, седем персийски и мидийски първенци, които имаха достъп при царя и заемаха първо място в царството):
15 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
Що можем, според закона, да направим на царица Астин за гдето не изпълни заповедта на царя Асуира чрез скопците?
16 Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
И Мемукан, отговори пред царя и първенците: Царица Астин не е обидила само царя, но и всичките първенци и всичките племена, които са по всичките области на цар Асуира.
17 Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
Защото тая постъпка на царицата ще се разчуе между всичките жени, така щото, когато се разнесе слух, че цар Асуир заповядал да се доведе царица Астин пред него, а тя не дошла, това ще направи мъжете им презрени пред очите им.
18 Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
И днес персийските и мидийските съпруги, които ще са чули за постъпката на царицата, ще говорят по същия начин на всичките царски първенци; и от това ще произлезе голямо презрение и гняв.
19 “Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
Ако е угодно на царя, нека се издаде от него царска заповед, която да се впише между персийските и мидийските закони, за да се не отменява, според която Астин да не дохожда вече пред цар Асуира; и царят нека даде царското й достойнство на друга по-добра от нея.
20 Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
И когато указът, който царят ще издаде, бъде обнародван по цялото му царство, (защото е голямо), всичките жени ще отдават чест на мъжете си, на голям и на малък.
21 Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
И тая дума се хареса на царя и на първенците; и царят стори според каквото каза Мемукан.
22 Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.
Той прати писма по всичките царски области, във всяка област според азбуката й, и на всеки народ според езика му, за да може всеки мъж да бъде господар в дома си, и в него да говори по езика на людете си.

< Estere 1 >