< Estere 9 >

1 Pa mwezi wa 12, mwezi wa Adara pa tsiku la 13 la mwezi womwewo, tsiku limene lamulo loyamba lija la mfumu linayembekezereka kuti litsatidwe, pamene adani a Ayuda anati awononge Ayudawo, zinthu zinasintha. Ayuda ndiwo anawononga adani awo.
A dwunastego [miesiąca], czyli miesiąca Adar, trzynastego dnia tego miesiąca, gdy nadszedł czas wypełnienia rozkazu króla i jego dekretu, tego dnia, kiedy wrogowie Żydów spodziewali się, że będą panować nad nimi, stało się wprost przeciwnie, ponieważ Żydzi panowali nad tymi, którzy ich nienawidzili.
2 Ayuda anasonkhana mʼmizinda ya zigawo zonse za Mfumu Ahasiwero kuthira nkhondo onse amene anafuna kuwawononga. Palibe amene akanalimbana nawo chifukwa anthu onse a mitundu ina anachita nawo mantha.
Żydzi bowiem zebrali się w swoich miastach we wszystkich prowincjach króla Aswerusa, aby podnieść rękę na tych, którzy pragnęli ich zguby. A nikt nie mógł im stawić oporu, gdyż strach przed nimi padł na wszystkie ludy.
3 Ndipo akuluakulu onse a zigawo, akalonga, akazembe ndi ogwira ntchito za mfumu anathandiza Ayuda, chifukwa anachita mantha ndi Mordekai.
I wszyscy przełożeni prowincji, satrapowie, namiestnicy i urzędnicy królewscy popierali Żydów, bo padł na nich strach przed Mardocheuszem.
4 Pajatu Mordekai anali munthu wamkulu mʼnyumba ya ufumu. Mbiri yake inafalikira zigawo zonse, ndipo mphamvu zake zinakulirakulirabe.
Mardocheusz był bowiem wielki w domu króla, a jego sława rozchodziła się po wszystkich prowincjach, gdyż Mardocheusz stawał się coraz większy.
5 Motero Ayuda anakantha adani awo onse ndi lupanga, kuwapha ndi kuwawononga, ndipo anachita chimene chinawakomera kwa adani awo.
Tak to Żydzi zabili wszystkich swoich wrogów mieczem, mordując i niszcząc, a czynili z tymi, co ich nienawidzili, według swego upodobania.
6 Ku likulu la mzinda wa Susa, Ayuda anapha ndi kuwononga anthu 500.
Nawet i w pałacu Suza Żydzi zabili i wytracili pięciuset mężczyzn;
7 Ayuda anaphanso Parisandata, Dalifoni, Asipata,
I Parszandatę, Dalfona i Aspatę;
8 Porata, Adaliya, Aridata,
I Poratę, Adalię i Arydata;
9 Parimasita, Arisai, Aridai ndi Vaisata,
I Parmasztę, Arisaja, Aridaja i Wajezatę;
10 ana khumi a Hamani, mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande katundu wawo.
Tych dziesięciu synów Hamana, syna Hammedaty, wroga Żydów, zabili, ale po łupy nie wyciągnęli swej ręki.
11 Tsiku lomwelo anawuza mfumu chiwerengero cha anthu amene anaphedwa mu likulu la mzinda wa Susa.
Tego samego dnia dotarła do króla wiadomość o liczbie zabitych w pałacu Suza.
12 Mfumu inati kwa mfumukazi Estere, “Ayuda apha ndi kuwononga anthu 500 ndi ana khumi a Hamani mu likulu la mzinda wa Susa. Nanga ku zigawo zina zonse za mfumu achitako chiyani? Kodi tsopano ukupemphanso chiyani? Chimene ukupempha ndidzakupatsa. Kodi ukufuna chiyani? Chimene ukufuna ndidzakupatsa.”
I król powiedział do królowej Estery: W pałacu Suza Żydzi zabili i wytracili pięciuset mężczyzn oraz dziesięciu synów Hamana. [A] w pozostałych prowincjach królewskich, cóż uczynili? Jaką masz jeszcze prośbę, a będzie spełniona. Czego jeszcze sobie życzysz, a stanie ci się.
13 Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni mfumu, apatseni chilolezo Ayuda okhala mu Susa kuti achitenso zimene achita lerozi mawa, potsata lamulo ndipo mulole kuti ana khumi a Hamani aja mitembo yawo ipachikidwe pa mtanda.”
Estera odpowiedziała: Jeśli się królowi spodoba, niech wolno będzie jutro Żydom, którzy są w Suzie, uczynić według dekretu dzisiejszego i niech powieszą dziesięciu synów Hamana na szubienicy.
14 Choncho mfumu inalamula kuti izi zichitike. Anapereka lamulo mu Susa ndipo mitembo ya ana khumi a Hamani anayipachika pa mtanda.
I król rozkazał, aby tak uczyniono. Ogłoszono dekret w Suzie i powieszono dziesięciu synów Hamana.
15 Ayuda a mu mzinda wa Susa anasonkhana pamodzi pa tsiku la 14 la mwezi wa Adara ndipo anapha anthu 300 mu Susa, koma sanatenge katundu wawo.
A Żydzi, którzy [byli] w Suzie, zgromadzili się także dnia czternastego miesiąca Adar i zabili w Suzie trzystu mężczyzn, lecz po łupy nie wyciągnęli swojej ręki.
16 Tsono Ayuda ena onse amene anali mu zigawo za mfumu anasonkhananso kudziteteza ndipo sanasautsidwenso ndi adani popeza anapha anthu 75,000 koma sanalande zofunkha zawo.
Pozostali zaś Żydzi, którzy byli w prowincjach królewskich, zebrali się w obronie swojego życia i mieli odpoczynek od swoich wrogów. Zabili siedemdziesiąt pięć tysięcy swoich wrogów, lecz po łupy nie wyciągnęli swojej ręki;
17 Zonsezi zinachitika pa tsiku la 13 la mwezi wa Adara ndipo pa tsiku la 14 anapumula ndi kupanga tsikuli kuti likhale la madyerero ndi chikondwerero.
W dniu trzynastym miesiąca Adar, a odpoczywali czternastego [dnia] tego [miesiąca] i obchodzili go jako dzień uczty i wesela.
18 Koma Ayuda okhala mu Susa anasonkhana pa tsiku la 13 ndi la 14 ndipo anakonza tsiku la 15 kuti likhale tsiku la madyerero ndi chikondwerero.
Ale Żydzi, którzy byli w Suzie, zebrali się dnia trzynastego i czternastego tego miesiąca, a piętnastego [dnia] odpoczęli i obchodzili go jako dzień uczty i wesela.
19 Ichi ndi chifukwa chake Ayuda a ku midzi, amene amakhala mʼzithando amasunga tsiku la 14 la mwezi wa Adara ngati la madyerero ndi chikondwerero, tsiku lopatsana mphatso.
Dlatego Żydzi mieszkający we wsiach i w miasteczkach nieobwarowanych obchodzą czternasty dzień miesiąca Adar jako dzień radości, uczty i jako doniosły dzień, w którym posyłają sobie dary żywnościowe.
20 Mordekai analemba mawu awa mʼmakalata ndipo anawatumiza kwa Ayuda onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero, a pafupi ndi a kutali:
A Mardocheusz spisał te wydarzenia i rozesłał listy do wszystkich Żydów, którzy [byli] we wszystkich prowincjach króla Aswerusa, bliskich i dalekich;
21 Anati chaka chilichonse, Ayudawo azisunga tsiku la 14 ndi 15 la mwezi wa Adara,
Zobowiązując ich, aby obchodzili czternasty dzień miesiąca Adar i piętnasty dzień tego samego [miesiąca], rokrocznie;
22 ngati masiku amene Ayuda anapulumutsidwa kwa adani awo, ndiponso ngati mwezi umene chisoni chawo chinasandulika chimwemwe ndi kulira kwawo kunasandulika chikondwerero. Anawalembera kuti azisunga masikuwa ngati masiku a madyerero ndi chikondwerero, masiku opatsana mphatso zachakudya kwa wina ndi mnzake komanso opereka mphatso kwa osauka.
Jako dni, w których Żydzi odpoczęli od swoich wrogów, i miesiąc, który obrócił się im ze smutku w radość, a z płaczu w dzień radości – aby obchodzili je jako dni uczty i wesela oraz posyłania sobie darów żywnościowych, a ubogim darów.
23 Choncho Ayuda anavomereza kusunga masikuwa ngati a chikondwerero monga analembera Mordekai.
[Wszyscy] Żydzi przyjęli to, co sami zaczęli czynić, a co napisał im Mardocheusz;
24 Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, mdani wa Ayuda onse, anakonza chiwembu chakupha ndi kuwononga Ayuda ndipo anachita maere otchedwa Purimu kuti awaphe ndi kuwawononga.
Haman bowiem, syn Hammedaty, Agagity, wróg wszystkich Żydów, wymyślił plan przeciw Żydom, aby ich wytracić, i rzucił Pur, czyli los, aby ich wytracić i zniszczyć;
25 Koma mfumu itazindikira za chiwembuchi, inalamula kuti zilembedwe mʼmakalata kuti chiwembu chimene Hamani anakonzera Ayuda chigwere pa iye mwini, ndi kuti iye pamodzi ndi ana ake apachikidwe pa mtanda.
Ale gdy Estera przyszła przed króla, ten wydał dekret na piśmie, aby jego niegodziwy zamiar, który obmyślił przeciwko Żydom, obrócił się na głowę jego, i aby powiesić jego i jego synów na szubienicy.
26 Ndi chifukwa chake masiku amenewa amatchedwa masiku a Purimu potsata dzina lakuti Purimu. Chifukwa cha kalata ya Mordekai ndiponso chifukwa cha zimene anaziona ndi kuwachitikira,
Dlatego nazwali te dni Purim, od nazwy Pur. A z powodu wszystkich słów tego listu oraz na podstawie tego, co widzieli i co ich spotkało;
27 Ayuda onse anagwirizana kukhazikitsa lamulo lokhudza iwo, zidzukulu zawo ndi onse amene adzapanga nawo ubale kuti asalephere kusunga masiku awiri amenewa chaka chilichonse monga zinalembedweramo ndiponso potsata nthawi imene anayika.
Żydzi postanowili i wzięli na siebie, na swoje potomstwo i na wszystkich, którzy się do nich przyłączyli, nieustający [obowiązek], aby obchodzono te dwa dni stosownie do pisma i zgodnie z ustalonym czasem każdego roku;
28 Azisunga ndi kukumbukira masiku amenewa mu mʼbado uliwonse ndi banja lililonse, mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse. Ndipo Ayuda asadzasiye kukondwerera masiku a Purimuwa ndiponso zidzukulu zawo zisadzaleke kuwakumbukira.
I że te dni [będą] wspominane i obchodzone we wszystkich pokoleniach, w każdej rodzinie, w każdej prowincji i w każdym mieście; że te dni Purim nie zaginą wśród Żydów, a pamięć o nich nie ustanie u ich potomstwa.
29 Choncho mfumukazi Estere, mwana wa mkazi wa Abihaili, pamodzi ndi Mordekai Myuda analemba ndi ulamuliro onse kutsimikizira kalata iyi yachiwiri yokhudza Purimu.
Królowa Estera, córka Abichaila, i Żyd Mardocheusz napisali z całą powagą, aby potwierdzić ten drugi list dotyczący Purim.
30 Ndipo Mordekai anatumiza makalata kwa Ayuda onse ku zigawo 127 za ufumu wa Ahasiwero. Kalatayi inali ya mawu a mtendere ndiponso a kukhulupirika
Mardocheusz posłał ten list do wszystkich Żydów, do stu dwudziestu siedmiu prowincji królestwa Aswerusa, ze słowami pokoju i prawdy;
31 kuti azisunga masiku a Purimu pa nyengo imene inavomerezeka monga mmene Mordekai Myuda ndi mfumukazi Estere anawalamulira ndiponso monga anadziyikira eni okha ndi zidzukulu zawo zonena za nthawi zawo za kusala zakudya ndi kulira.
Aby ustanowić te dni Purim w ustalonym czasie, jak to Żyd Mardocheusz i królowa Estera ustanowili je i jak zobowiązali samych siebie i swoje potomstwo, na pamiątkę postu i ich lamentacji.
32 Lamulo la Estere linakhazikitsa mwambo wa Purimuwu ndipo zinalembedwa mʼmabuku.
Nakaz Estery potwierdził ustawę dotyczącą tych [dni] Purim i zostało to zapisane [w] księdze.

< Estere 9 >