< Estere 9 >

1 Pa mwezi wa 12, mwezi wa Adara pa tsiku la 13 la mwezi womwewo, tsiku limene lamulo loyamba lija la mfumu linayembekezereka kuti litsatidwe, pamene adani a Ayuda anati awononge Ayudawo, zinthu zinasintha. Ayuda ndiwo anawononga adani awo.
And in the twelfth month, that is, the month Adar, on the thirteenth day thereof, when the king's commandment and his decree drew near to be put in execution, in the day that the enemies of the Jews hoped to have power over them (but it was turned to the contrary, that the Jews had power over them that hated them),
2 Ayuda anasonkhana mʼmizinda ya zigawo zonse za Mfumu Ahasiwero kuthira nkhondo onse amene anafuna kuwawononga. Palibe amene akanalimbana nawo chifukwa anthu onse a mitundu ina anachita nawo mantha.
the Jews gathered themselves together in their cities throughout the provinces of king Ahasuerus, to lay hand on such as sought their hurt. And no man could withstand them; for the fear of them had fallen upon all the peoples.
3 Ndipo akuluakulu onse a zigawo, akalonga, akazembe ndi ogwira ntchito za mfumu anathandiza Ayuda, chifukwa anachita mantha ndi Mordekai.
And all the princes of the provinces, and the satraps, and the governors and officers of the king, helped the Jews; for the fear of Mordecai had fallen upon them.
4 Pajatu Mordekai anali munthu wamkulu mʼnyumba ya ufumu. Mbiri yake inafalikira zigawo zonse, ndipo mphamvu zake zinakulirakulirabe.
For Mordecai was great in the king's house, and his fame went forth throughout the provinces; for the man Mordecai became continually greater.
5 Motero Ayuda anakantha adani awo onse ndi lupanga, kuwapha ndi kuwawononga, ndipo anachita chimene chinawakomera kwa adani awo.
And the Jews smote all their enemies with the stroke of the sword and slaughter and destruction, and did what they would to those that hated them.
6 Ku likulu la mzinda wa Susa, Ayuda anapha ndi kuwononga anthu 500.
And in Shushan the fortress the Jews slew and destroyed five hundred men.
7 Ayuda anaphanso Parisandata, Dalifoni, Asipata,
And Parshandatha, and Dalphon, and Aspatha,
8 Porata, Adaliya, Aridata,
and Poratha, and Adalia, and Aridatha,
9 Parimasita, Arisai, Aridai ndi Vaisata,
and Parmashta, and Arisai, and Aridai, and Vajezatha,
10 ana khumi a Hamani, mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande katundu wawo.
the ten sons of Haman the son of Hammedatha, the oppressor of the Jews, they slew; but they laid not their hands on the prey.
11 Tsiku lomwelo anawuza mfumu chiwerengero cha anthu amene anaphedwa mu likulu la mzinda wa Susa.
On that day the number of those that were slain in Shushan the fortress was brought before the king.
12 Mfumu inati kwa mfumukazi Estere, “Ayuda apha ndi kuwononga anthu 500 ndi ana khumi a Hamani mu likulu la mzinda wa Susa. Nanga ku zigawo zina zonse za mfumu achitako chiyani? Kodi tsopano ukupemphanso chiyani? Chimene ukupempha ndidzakupatsa. Kodi ukufuna chiyani? Chimene ukufuna ndidzakupatsa.”
And the king said to Esther the queen, The Jews have slain and destroyed five hundred men in Shushan the fortress, and the ten sons of Haman; what have they done in the rest of the king's provinces? And what is thy petition? and it shall be granted thee; and what is thy request further? and it shall be done.
13 Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni mfumu, apatseni chilolezo Ayuda okhala mu Susa kuti achitenso zimene achita lerozi mawa, potsata lamulo ndipo mulole kuti ana khumi a Hamani aja mitembo yawo ipachikidwe pa mtanda.”
And Esther said, If it please the king, let it be granted to the Jews that are in Shushan to do to-morrow also according to this day's decree, and let Haman's ten sons be hanged upon the gallows.
14 Choncho mfumu inalamula kuti izi zichitike. Anapereka lamulo mu Susa ndipo mitembo ya ana khumi a Hamani anayipachika pa mtanda.
And the king commanded it so to be done: and the decree was given at Shushan; and they hanged Haman's ten sons.
15 Ayuda a mu mzinda wa Susa anasonkhana pamodzi pa tsiku la 14 la mwezi wa Adara ndipo anapha anthu 300 mu Susa, koma sanatenge katundu wawo.
And the Jews that were in Shushan gathered themselves together on the fourteenth day also of the month Adar, and slew three hundred men at Shushan; but they laid not their hand on the prey.
16 Tsono Ayuda ena onse amene anali mu zigawo za mfumu anasonkhananso kudziteteza ndipo sanasautsidwenso ndi adani popeza anapha anthu 75,000 koma sanalande zofunkha zawo.
And the other Jews that were in the king's provinces gathered themselves together, and stood for their life, and had rest from their enemies; and they slew of them that hated them seventy-five thousand (but they laid not their hand on the prey),
17 Zonsezi zinachitika pa tsiku la 13 la mwezi wa Adara ndipo pa tsiku la 14 anapumula ndi kupanga tsikuli kuti likhale la madyerero ndi chikondwerero.
on the thirteenth day of the month Adar; and on the fourteenth of the same they rested, and made it a day of feasting and joy.
18 Koma Ayuda okhala mu Susa anasonkhana pa tsiku la 13 ndi la 14 ndipo anakonza tsiku la 15 kuti likhale tsiku la madyerero ndi chikondwerero.
But the Jews that were at Shushan gathered themselves together on the thirteenth [day] thereof, and on the fourteenth thereof; and on the fifteenth of the same they rested, and made it a day of feasting and joy.
19 Ichi ndi chifukwa chake Ayuda a ku midzi, amene amakhala mʼzithando amasunga tsiku la 14 la mwezi wa Adara ngati la madyerero ndi chikondwerero, tsiku lopatsana mphatso.
Therefore the Jews of the villages that dwell in the country towns make the fourteenth of the month Adar a day of joy and feasting, and a good day, and on which they send portions one to another.
20 Mordekai analemba mawu awa mʼmakalata ndipo anawatumiza kwa Ayuda onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero, a pafupi ndi a kutali:
And Mordecai wrote these things, and sent letters to all the Jews near and far that were in all the provinces of king Ahasuerus,
21 Anati chaka chilichonse, Ayudawo azisunga tsiku la 14 ndi 15 la mwezi wa Adara,
to establish [this] among them, that they should keep the fourteenth day of the month Adar, and the fifteenth day of the same, yearly,
22 ngati masiku amene Ayuda anapulumutsidwa kwa adani awo, ndiponso ngati mwezi umene chisoni chawo chinasandulika chimwemwe ndi kulira kwawo kunasandulika chikondwerero. Anawalembera kuti azisunga masikuwa ngati masiku a madyerero ndi chikondwerero, masiku opatsana mphatso zachakudya kwa wina ndi mnzake komanso opereka mphatso kwa osauka.
as the days on which the Jews rested from their enemies, and the month that was turned to them from sorrow to joy, and from mourning into a good day; that they should make them days of feasting and joy, and of sending portions one to another, and gifts to the poor.
23 Choncho Ayuda anavomereza kusunga masikuwa ngati a chikondwerero monga analembera Mordekai.
And the Jews undertook to do as they had begun, and as Mordecai had written to them.
24 Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, mdani wa Ayuda onse, anakonza chiwembu chakupha ndi kuwononga Ayuda ndipo anachita maere otchedwa Purimu kuti awaphe ndi kuwawononga.
For Haman the son of Hammedatha the Agagite, the oppressor of all the Jews, had devised against the Jews to destroy them, and had cast Pur, that is, the lot, to consume them and to destroy them;
25 Koma mfumu itazindikira za chiwembuchi, inalamula kuti zilembedwe mʼmakalata kuti chiwembu chimene Hamani anakonzera Ayuda chigwere pa iye mwini, ndi kuti iye pamodzi ndi ana ake apachikidwe pa mtanda.
and when [Esther] came before the king, he commanded by letters that his wicked device, which he had devised against the Jews, should return upon his own head; and they hanged him and his sons on the gallows.
26 Ndi chifukwa chake masiku amenewa amatchedwa masiku a Purimu potsata dzina lakuti Purimu. Chifukwa cha kalata ya Mordekai ndiponso chifukwa cha zimene anaziona ndi kuwachitikira,
Therefore they called these days Purim after the name of Pur. Therefore, according to all the words of this letter, and for what they had seen concerning this matter and what had happened to them,
27 Ayuda onse anagwirizana kukhazikitsa lamulo lokhudza iwo, zidzukulu zawo ndi onse amene adzapanga nawo ubale kuti asalephere kusunga masiku awiri amenewa chaka chilichonse monga zinalembedweramo ndiponso potsata nthawi imene anayika.
the Jews ordained and took upon them, and upon their seed, and upon all such as joined themselves to them, so that it should not fail, that they would observe these two days according to their writing and according to their fixed time, every year;
28 Azisunga ndi kukumbukira masiku amenewa mu mʼbado uliwonse ndi banja lililonse, mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse. Ndipo Ayuda asadzasiye kukondwerera masiku a Purimuwa ndiponso zidzukulu zawo zisadzaleke kuwakumbukira.
and that these days should be remembered and observed throughout every generation, in every family, every province, and every city, and that these days of Purim should not fail from among the Jews, nor the memorial of them cease from among their seed.
29 Choncho mfumukazi Estere, mwana wa mkazi wa Abihaili, pamodzi ndi Mordekai Myuda analemba ndi ulamuliro onse kutsimikizira kalata iyi yachiwiri yokhudza Purimu.
And queen Esther the daughter of Abihail, and Mordecai the Jew, wrote with all authority to confirm this second letter of Purim.
30 Ndipo Mordekai anatumiza makalata kwa Ayuda onse ku zigawo 127 za ufumu wa Ahasiwero. Kalatayi inali ya mawu a mtendere ndiponso a kukhulupirika
And he sent letters to all the Jews, to the hundred and twenty-seven provinces of the kingdom of Ahasuerus, words of peace and truth,
31 kuti azisunga masiku a Purimu pa nyengo imene inavomerezeka monga mmene Mordekai Myuda ndi mfumukazi Estere anawalamulira ndiponso monga anadziyikira eni okha ndi zidzukulu zawo zonena za nthawi zawo za kusala zakudya ndi kulira.
to confirm these days of Purim in their fixed times, according as Mordecai the Jew and queen Esther had enjoined them, and as they had decreed for themselves and for their seed, as to the matters of the fastings and their cry.
32 Lamulo la Estere linakhazikitsa mwambo wa Purimuwu ndipo zinalembedwa mʼmabuku.
And the decree of Esther confirmed these matters of Purim; and it was written in the book.

< Estere 9 >