< Estere 8 >
1 Tsiku lomwelo mfumu Ahasiwero anamupatsa mfumukazi Estere nyumba ya Hamani, mdani wa Ayuda. Ndipo Mordekai anafika pamaso pa mfumu, popeza Estere anamuwuza ubale wawo.
Mhlalokho inkosi u-Ahasuweru yanika iNdlovukazi u-Esta impahla kaHamani, isitha samaJuda. UModekhayi weza phambi kwenkosi, ngoba u-Esta wayesechazile ngobuhlobo babo.
2 Mfumu inavula mphete yake yodindira imene analanda kwa Hamani ndipo Estere anamusankha Mordekai kukhala woyangʼanira nyumba ya Hamani.
Inkosi yakhupha indandatho yayo yophawu lobukhosi, eyayisiyithathele uHamani, yayipha uModekhayi. U-Esta wamkhetha uModekhayi ukuba aphathe impahla kaHamani.
3 Estere anayankhulanso ndi mfumu ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake. Uku akulira iye anapempha mfumu kuti iletse choyipa, makamaka chiwembu chimene Hamani Mwagagi anakonza kuti awononge a Yuda.
U-Esta wabuye wancenga enkosini, eziwisela ezinyaweni zayo njalo ekhala. Wayicela ukuba inqabele icebo elibi likaHamani umʼAgagi, ayelicebe ngamaJuda.
4 Ndipo mfumu inamuloza Estere ndi ndodo yake yagolide ndipo Estere anadzuka ndi kuyima pamaso pake.
Inkosi yasiselulela intonga yayo yegolide ku-Esta owasukuma wama phambi kwayo.
5 Iye anati, “Ngati chikomera mfumu ndi kukukondweretsani, ngati pempho langa muliona kuti ndi loyenera ndi kuti mukondwera nane tsono mfumu ilole kuti lamulo lilembedwe kusintha mawu a mʼmakalata amene Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, anatumiza ku zigawo zonse za mfumu. Paja Hamani analemba kuti Ayuda onse awonongedwe.
Wathi, “Nxa kuyithokozisa inkosi, njalo nxa ingamukela ngokuthokoza ibona kuyinto efanele ukwenziwa, njalo nxa ithokoza ngami, akubhalwe umlayo ozachitha izincwadi ezalotshwa nguHamani indodana kaHamedatha, umʼAgagi, ezazibhalwe ngezimiso zokuchitha amaJuda kuzozonke izabelo zenkosi.
6 Kodi ndingapirire bwanji pamene ndi kuona tsoka likugwera anthu a mtundu wanga? Ndingapirire bwanji pamene abale anga akuwonongedwa?”
Kambe kungavuma njani ukubona incithakalo isehlela abantu bakithi? Kungavuma njani ukuba ngibone incithakalo yemuli yakithi?”
7 Mfumu Ahasiwero anamuyankha mfumukazi Estere ndi Mordekai Myuda kuti, “Ndapereka nyumba ya Hamani kwa Estere ndipo Hamaniyo amupachika kale pa mtanda chifukwa anafuna kuwononga Ayuda.
Inkosi u-Ahasuweru waphendula iNdlovukazi loModekhayi umJuda ngokuthi, “Ngoba uHamani ehlasele amaJuda, sengiphe u-Esta impahla yakhe, njalo sebemlengise esakhiweni sokulengisa.
8 Tsono inu awiri, lembani za Ayudawo monga mufunira. Mulembe mʼdzina la mfumu ndipo musindikize chizindikiro cha mphete ya mfumu popeza kuti cholembedwa mʼdzina la mfumu ndi kusindikizidwa ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu sichingasinthidwe.”
Ngakho-ke bhala omunye umlayo ngebizo lenkosi usenzela amaJuda njengokubona kwakho, ubusuyingcina ngophawu lwendandatho yenkosi, ngoba awukho umbiko olotshwe ngebizo lenkosi wangcinwa ngophawu lwendandatho yayo ongadilizwa.”
9 Nthawi yomweyo, pa tsiku la 23 la mwezi wachitatu wa Sivani, mfumu inayitana alembi ake. Analemba zonse zokhudza Ayuda monga ananenera Mordekai. Analembera akazembe, abwanamkubwa ndi nduna za zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. Zimene analamula Mordekai zinalembedwa mʼzilembo za chigawo chilichonse ndi chiyankhulo cha mtundu uliwonse wa anthu. Ayudanso anawalembera mʼmalemba awo ndi chiyankhulo chawo.
Onobhala besigodlweni bahle babizwa masinyane, ngelanga lamatshumi amabili lantathu ngenyanga yesithathu, inyanga ethiwa nguSivana. Babhala yonke imilayo kaModekhayi kumaJuda, lakuziphathamandla, kubabusi lakuzikhulu kuzozonke izabelo ezilikhulu elilamatshumi amabili lesikhombisa kusukela e-Indiya kuze kuyefika eTopiya. Imilayo leyo yayibhalwe ngombhalo walelo lalelo lizwe ngolimi lwalabobantu njalo lakubaJuda ngombhalo wabo lolimi lwabo.
10 Mordekai analemba makalatawo mʼdzina la mfumu Ahasiwero, nawadinda ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu. Ndipo anawatumiza ndi anthu amithenga amene anakwera pa akavalo a ufumu othamanga kwambiri obadwa mu khola la ufumu.
UModekhayi wabhala ngebizo leNkosi u-Ahasuweru, wangcina izincwadi lezo ngophawu lwendandatho yenkosi, wathuma izithunywa ezazigada amabhiza ayelesiqubu efuyelwe ukusetshenziswa yinkosi.
11 Mʼmakalata amenewa mfumu inalola kuti Ayuda okhala mu mzinda uliwonse akhale ndi ufulu wokumana ndi kudzitchinjiriza komanso kuwononga, kupha ndi kufafaniziratu gulu lililonse la nkhondo la anthu a mtundu uliwonse kapena chigawo chimene chingawathire nkhondo. Ayudawo analoledwa kuwononga gulu lankhondo lija, ana awo ndi akazi awo komanso kuti afunkhe katundu wawo.
Isimiso somlayo wenkosi sasinika amaJuda kuwo wonke amadolobho imvumo yokuhlangana lokuzivikela; ukuchitha, ukubulala babhubhise yonke impi ehlomileyo eyaloba yisiphi isizwe loba isifunda esasingabahlasela kanye labesifazane labantwana; lokuthi baphange impahla yezitha zabo.
12 Ayuda analoledwa kuchita zimenezi mʼzigawo zonse za Mfumu Ahasiwero pa tsiku limodzi lokha la 13 la mwezi wa 12, mwezi wa Adara.
Ilanga elamiswayo ukuba amaJuda enze lokho kuzozonke izabelo zeNkosi u-Ahasuweru lalingeletshumi lantathu ngenyanga yetshumi lambili, inyanga ethiwa ngu-Adari.
13 Mawu a mʼmakalatawo anayenera kudziwitsidwa kwa anthu a mtundu uliwonse mu chigawo chilichonse kuti ndi lamulo ndithu kwa anthu a mtundu uliwonse ndi kuti Ayuda adzakhale okonzeka pa tsikulo kulipsira kwa adani awo.
Isimiso somlayo lowo sasizakhutshwa sibe ngumthetho kuzozonke izabelo, umenyezelwe ebantwini bezizwe zonke ukuze amaJuda ahlale elungele ngalelolanga ukuphindisela ezitheni zawo.
14 Atawalamulira a mfumu, amithenga aja anapita nawo makalata mwachangu, atakwera pa akavalo a mfumu. Ndipo lamulolo analiperekanso ku likulu la mzinda wa Susa.
Izithunywa zaphuma ngokuphangisa zigade amabhiza esigodlweni, zifuqwa ngumlayo wenkosi. Isimiso somlayo samenyezelwa edolobheni laseSusa.
15 Mordekai anachoka pamaso pa mfumu atavala zovala zaufumu zooneka ngati mtambo ndi zofewa zoyera, chipewa chachikulu cha golide ndi mkanjo wapepo. Ndipo mzinda wa Susa unafuwula mokondwa.
UModekhayi wasuka phambi kwenkosi egqoke izembatho zobukhosi ezilombala oluhlaza okwesibhakabhaka lomhlophe, umqhele wegolide omkhulu kanye lesembatho esiyibubende eselembu lelineni elihle. Kwaba ledili lentokozo edolobheni laseSusa.
16 Kwa Ayuda inali nthawi ya nkhope zowala ndi za chimwemwe, chikondwerero ndi ulemu.
Kwaba yisikhathi sokuthaba lokuthokoza, injabulo lodumo kubaJuda.
17 Mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse, kumene mawu a mfumu onena za lamulo lake anafika, kunali chimwemwe ndi chikondwerero pakati pa Ayuda. Linali tsiku la phwando ndi chikondwerero. Ndipo anthu ambiri a mitundu ina anazitcha Ayuda chifukwa anachita mantha ndi Ayudawo.
Kuzozonke izabelo lakuwo wonke amadolobho, ingqe lapho isimiso somlayo wenkosi esaya khona, kwaba lentokozo lenjabulo kubaJuda, kwaba lamadili kwadliwa. Abantu abanengi bakwezinye izizwe baba ngabaJuda ngenxa yokwesaba amaJuda.