< Estere 8 >
1 Tsiku lomwelo mfumu Ahasiwero anamupatsa mfumukazi Estere nyumba ya Hamani, mdani wa Ayuda. Ndipo Mordekai anafika pamaso pa mfumu, popeza Estere anamuwuza ubale wawo.
Onoga istog dana kralj Ahasver preda kraljici Esteri kuću Hamana, progonitelja Židova, a Mordokaj je stupio pred kraljevo lice, jer je Estera objasnila kralju što joj je on.
2 Mfumu inavula mphete yake yodindira imene analanda kwa Hamani ndipo Estere anamusankha Mordekai kukhala woyangʼanira nyumba ya Hamani.
Kralj skinu pečatni prsten, koji je već bio oduzeo Hamanu, i dade ga Mordokaju, a Estera postavi Mordokaja nad Hamanovom kućom.
3 Estere anayankhulanso ndi mfumu ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake. Uku akulira iye anapempha mfumu kuti iletse choyipa, makamaka chiwembu chimene Hamani Mwagagi anakonza kuti awononge a Yuda.
Estera tada ponovo progovori kralju. Baci mu se pred noge; rasplaka se i najvruće ga zamoli da osujeti zlo Hamana Agađanina i naum opaki što ga bijaše zasnovao protiv Židova.
4 Ndipo mfumu inamuloza Estere ndi ndodo yake yagolide ndipo Estere anadzuka ndi kuyima pamaso pake.
Kralj pruži prema Esteri zlatno žezlo. Estera se diže, stade pred kraljem
5 Iye anati, “Ngati chikomera mfumu ndi kukukondweretsani, ngati pempho langa muliona kuti ndi loyenera ndi kuti mukondwera nane tsono mfumu ilole kuti lamulo lilembedwe kusintha mawu a mʼmakalata amene Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, anatumiza ku zigawo zonse za mfumu. Paja Hamani analemba kuti Ayuda onse awonongedwe.
i reče: "Ako je kralju po volji, ako sam našla milost pred licem njegovim, ako je kralju pravo te ako sam mila u njegovim očima, neka pismeno opozove sve što napisa Haman, sin Hamdatin, Agađanin, u opakoj nakani da se pobiju Židovi koji se nalaze u svim pokrajinama kraljevstva.
6 Kodi ndingapirire bwanji pamene ndi kuona tsoka likugwera anthu a mtundu wanga? Ndingapirire bwanji pamene abale anga akuwonongedwa?”
TÓa kako bih ja mogla gledati nesreću koja bi pogodila moj narod? Kako bih mogla gledati zator roda svoga?"
7 Mfumu Ahasiwero anamuyankha mfumukazi Estere ndi Mordekai Myuda kuti, “Ndapereka nyumba ya Hamani kwa Estere ndipo Hamaniyo amupachika kale pa mtanda chifukwa anafuna kuwononga Ayuda.
Kralj Ahasver odgovori kraljici Esteri i Mordokaju Židovu: "Eto, poklonio sam Esteri kuću Hamanovu, a njega sam dao objesiti jer je bio digao svoju ruku na Židove,
8 Tsono inu awiri, lembani za Ayudawo monga mufunira. Mulembe mʼdzina la mfumu ndipo musindikize chizindikiro cha mphete ya mfumu popeza kuti cholembedwa mʼdzina la mfumu ndi kusindikizidwa ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu sichingasinthidwe.”
a vi u ime kraljevo napišite o Židovima što vam se sviđa i zapečatite kraljevim prstenom. Jer neopoziv je proglas koji je u kraljevo ime napisan te kraljevim pečatom zapečaćen."
9 Nthawi yomweyo, pa tsiku la 23 la mwezi wachitatu wa Sivani, mfumu inayitana alembi ake. Analemba zonse zokhudza Ayuda monga ananenera Mordekai. Analembera akazembe, abwanamkubwa ndi nduna za zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. Zimene analamula Mordekai zinalembedwa mʼzilembo za chigawo chilichonse ndi chiyankhulo cha mtundu uliwonse wa anthu. Ayudanso anawalembera mʼmalemba awo ndi chiyankhulo chawo.
Tada, dvadeset i trećeg dana trećega mjeseca, to jest mjeseca Sivana, budu sazvani pisari kraljevi i prema svemu što bijaše naredio Mordokaj napisa se Židovima, namjesnicima, upravljačima i knezovima pokrajina od Indije do Etiopije, a bijaše sto dvadeset i sedam pokrajina, svakoj pokrajini njezinim pismom, svakom narodu njegovim jezikom, pa i Židovima njihovim pismom i njihovim jezikom.
10 Mordekai analemba makalatawo mʼdzina la mfumu Ahasiwero, nawadinda ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu. Ndipo anawatumiza ndi anthu amithenga amene anakwera pa akavalo a ufumu othamanga kwambiri obadwa mu khola la ufumu.
On napisa pisma u ime kralja Ahasvera i zapečati ih kraljevim prstenom pa ih razasla po skorotečama koji su jahali na konjima, pastusima iz kraljevske ergele.
11 Mʼmakalata amenewa mfumu inalola kuti Ayuda okhala mu mzinda uliwonse akhale ndi ufulu wokumana ndi kudzitchinjiriza komanso kuwononga, kupha ndi kufafaniziratu gulu lililonse la nkhondo la anthu a mtundu uliwonse kapena chigawo chimene chingawathire nkhondo. Ayudawo analoledwa kuwononga gulu lankhondo lija, ana awo ndi akazi awo komanso kuti afunkhe katundu wawo.
Kralj je dopustio Židovima po svim gradovima da se mogu sastajati, braniti svoj život te uništiti, ubiti i zatrti svaku vojsku narodnu ili pokrajinsku koja bi ih napala, ne štedeći ni djecu ni žene, a slobodno im je oplijeniti njihova dobra;
12 Ayuda analoledwa kuchita zimenezi mʼzigawo zonse za Mfumu Ahasiwero pa tsiku limodzi lokha la 13 la mwezi wa 12, mwezi wa Adara.
sve istoga dana u svim pokrajinama kraljevstva Ahasverova: trinaestog dana dvanaestoga mjeseca, to jest mjeseca Adara.
13 Mawu a mʼmakalatawo anayenera kudziwitsidwa kwa anthu a mtundu uliwonse mu chigawo chilichonse kuti ndi lamulo ndithu kwa anthu a mtundu uliwonse ndi kuti Ayuda adzakhale okonzeka pa tsikulo kulipsira kwa adani awo.
Prijepis pisma, koje je imalo postati zakonom u svakoj pokrajini, bijaše objavljen među svim narodima, kako bi Židovi toga dana bili spremni osvetiti se svojim neprijateljima.
14 Atawalamulira a mfumu, amithenga aja anapita nawo makalata mwachangu, atakwera pa akavalo a mfumu. Ndipo lamulolo analiperekanso ku likulu la mzinda wa Susa.
Skoroteče, konjanici na kraljevskim pastusima, krenuše odmah i pojuriše, po kraljevoj zapovijedi. Naredba je bila objavljena i u tvrđavi Suzi.
15 Mordekai anachoka pamaso pa mfumu atavala zovala zaufumu zooneka ngati mtambo ndi zofewa zoyera, chipewa chachikulu cha golide ndi mkanjo wapepo. Ndipo mzinda wa Susa unafuwula mokondwa.
Mordokaj izađe od kralja odjeven u grimiznu i lanenu kraljevsku haljinu, s velikom zlatnom krunom i s ogrtačem od fine tkanine i crvena skrleta. Grad je Suza klicao i veselio se.
16 Kwa Ayuda inali nthawi ya nkhope zowala ndi za chimwemwe, chikondwerero ndi ulemu.
Bio je to za Židove dan svjetla, veselja, kliktanja i slavlja.
17 Mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse, kumene mawu a mfumu onena za lamulo lake anafika, kunali chimwemwe ndi chikondwerero pakati pa Ayuda. Linali tsiku la phwando ndi chikondwerero. Ndipo anthu ambiri a mitundu ina anazitcha Ayuda chifukwa anachita mantha ndi Ayudawo.
U svakoj pokrajini, u svakom gradu i mjestu do kojega je dopro kraljev ukaz i zakon, zavlada među Židovima veselje, radost, gozba i blagdan, i mnogi među pucima zemlje postadoše Židovi jer ih je spopao strah od Židova.