< Estere 8 >

1 Tsiku lomwelo mfumu Ahasiwero anamupatsa mfumukazi Estere nyumba ya Hamani, mdani wa Ayuda. Ndipo Mordekai anafika pamaso pa mfumu, popeza Estere anamuwuza ubale wawo.
薛西斯王當王就將猶太人的敵人哈曼的家業,賜給了艾斯德爾王后;艾斯德爾同時也說明了摩爾德開與她自己的關係,摩爾德開就來覲見君王。
2 Mfumu inavula mphete yake yodindira imene analanda kwa Hamani ndipo Estere anamusankha Mordekai kukhala woyangʼanira nyumba ya Hamani.
君王於是取下由哈曼那裏拿回來的指璽,給了摩爾德開,艾斯德爾以後叫摩爾德開管理哈曼的家業。
3 Estere anayankhulanso ndi mfumu ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake. Uku akulira iye anapempha mfumu kuti iletse choyipa, makamaka chiwembu chimene Hamani Mwagagi anakonza kuti awononge a Yuda.
艾斯德爾又去向君王求情,俯伏在他足下,含淚哀求他取消阿加格人哈曼所加的禍害,和他為害猶太人所設的陰謀。
4 Ndipo mfumu inamuloza Estere ndi ndodo yake yagolide ndipo Estere anadzuka ndi kuyima pamaso pake.
王向艾斯德爾伸出金杖,艾斯德爾就起來,站在君王前,
5 Iye anati, “Ngati chikomera mfumu ndi kukukondweretsani, ngati pempho langa muliona kuti ndi loyenera ndi kuti mukondwera nane tsono mfumu ilole kuti lamulo lilembedwe kusintha mawu a mʼmakalata amene Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, anatumiza ku zigawo zonse za mfumu. Paja Hamani analemba kuti Ayuda onse awonongedwe.
說「如果大王喜歡,如果我得陛下寵幸,如果大王認為合理且喜愛我,就請寫一道諭令,把大王為消滅全國各省的猶太人所頒下的文書,即阿加格人哈默大達的兒子哈曼的陰謀廢除。
6 Kodi ndingapirire bwanji pamene ndi kuona tsoka likugwera anthu a mtundu wanga? Ndingapirire bwanji pamene abale anga akuwonongedwa?”
事實上,我怎能忍見我的民族遭受迫害﹖我怎能忍見我的親屬消滅﹖」
7 Mfumu Ahasiwero anamuyankha mfumukazi Estere ndi Mordekai Myuda kuti, “Ndapereka nyumba ya Hamani kwa Estere ndipo Hamaniyo amupachika kale pa mtanda chifukwa anafuna kuwononga Ayuda.
薛西斯王對艾斯德爾后和猶太人摩爾德開說:「我已將哈曼的家業賜給了艾斯德爾,而他本人已被懸在刑架上,因為他竟要對猶太人下毒手。
8 Tsono inu awiri, lembani za Ayudawo monga mufunira. Mulembe mʼdzina la mfumu ndipo musindikize chizindikiro cha mphete ya mfumu popeza kuti cholembedwa mʼdzina la mfumu ndi kusindikizidwa ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu sichingasinthidwe.”
如今就照你們的意思,以君王的名義,為保護猶太人寫一道文書,蓋上君王的玉印。凡以君王名義所寫,且蓋有君王玉印的文書,決不得廢除。」
9 Nthawi yomweyo, pa tsiku la 23 la mwezi wachitatu wa Sivani, mfumu inayitana alembi ake. Analemba zonse zokhudza Ayuda monga ananenera Mordekai. Analembera akazembe, abwanamkubwa ndi nduna za zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. Zimene analamula Mordekai zinalembedwa mʼzilembo za chigawo chilichonse ndi chiyankhulo cha mtundu uliwonse wa anthu. Ayudanso anawalembera mʼmalemba awo ndi chiyankhulo chawo.
就在那時候,即在三月──「息汪」月二十三日,召集了眾御史,要依照摩爾德開為保護猶太人提示的一切,用各省的文字,各民族的語言,也給猶太人以他們的文字語言,寫了一道文書,公告由印度至雇士一百二十七省的猶太人、御史大臣、各省省長及首長。
10 Mordekai analemba makalatawo mʼdzina la mfumu Ahasiwero, nawadinda ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu. Ndipo anawatumiza ndi anthu amithenga amene anakwera pa akavalo a ufumu othamanga kwambiri obadwa mu khola la ufumu.
摩爾德開遂以薛西斯王的名義,寫了這道文書,蓋上君王的玉印,然後派遣驛使,騎著御廄裏的駿馬,傳遞文書。
11 Mʼmakalata amenewa mfumu inalola kuti Ayuda okhala mu mzinda uliwonse akhale ndi ufulu wokumana ndi kudzitchinjiriza komanso kuwononga, kupha ndi kufafaniziratu gulu lililonse la nkhondo la anthu a mtundu uliwonse kapena chigawo chimene chingawathire nkhondo. Ayudawo analoledwa kuwononga gulu lankhondo lija, ana awo ndi akazi awo komanso kuti afunkhe katundu wawo.
文書上載著:君王恩准在各城市的猶太人,有團結自衛的權利,也准許他們破壞、殺害、消滅那些侵害他們的各族和各省的軍民,也可殺他們的婦孺,搶奪他們的財產;
12 Ayuda analoledwa kuchita zimenezi mʼzigawo zonse za Mfumu Ahasiwero pa tsiku limodzi lokha la 13 la mwezi wa 12, mwezi wa Adara.
且應在十二月「阿達爾」十三日那一天,在薛西斯帝國各省內開始生效。
13 Mawu a mʼmakalatawo anayenera kudziwitsidwa kwa anthu a mtundu uliwonse mu chigawo chilichonse kuti ndi lamulo ndithu kwa anthu a mtundu uliwonse ndi kuti Ayuda adzakhale okonzeka pa tsikulo kulipsira kwa adani awo.
這道文書應視為法律,公佈在各省內,通告各民族一律遵守,好使猶太人準備在這一天,可向自己的敵人復仇。
14 Atawalamulira a mfumu, amithenga aja anapita nawo makalata mwachangu, atakwera pa akavalo a mfumu. Ndipo lamulolo analiperekanso ku likulu la mzinda wa Susa.
驛使迫於君令,騎著御馬,火速出發。這諭文同時也在穌撒禁城公佈。
15 Mordekai anachoka pamaso pa mfumu atavala zovala zaufumu zooneka ngati mtambo ndi zofewa zoyera, chipewa chachikulu cha golide ndi mkanjo wapepo. Ndipo mzinda wa Susa unafuwula mokondwa.
摩爾德開於是拜別君王出來,身穿紫白相間的御袍,戴著大金冠,披著純白和朱紅色的氅衣。此時穌撒城歡欣雀躍。
16 Kwa Ayuda inali nthawi ya nkhope zowala ndi za chimwemwe, chikondwerero ndi ulemu.
猶太人終於得到了光明、喜樂、幸福和榮耀。
17 Mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse, kumene mawu a mfumu onena za lamulo lake anafika, kunali chimwemwe ndi chikondwerero pakati pa Ayuda. Linali tsiku la phwando ndi chikondwerero. Ndipo anthu ambiri a mitundu ina anazitcha Ayuda chifukwa anachita mantha ndi Ayudawo.
在各省各城中,凡是君令、上諭所到之處,猶太人無不歡欣雀躍,休假宴飲;各地的異民有許多人因為害怕猶太人,而入了猶太籍。

< Estere 8 >