< Estere 7 >

1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
I tako doðe car i Aman na objed carici Jestiri.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
I reèe car Jestiri opet drugi dan napivši se vina: šta želiš, carice Jestiro? daæe ti se; i šta moliš? ako je i do polovine carstva, biæe.
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
Tada odgovori carica Jestira i reèe: ako sam našla milost pred tobom, care, i ako je caru ugodno, neka mi se pokloni život moj na moju želju i narod moj na moju molbu.
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
Jer smo prodani ja i moj narod da nas potru, pobiju i istrijebe. Da smo prodani da budemo sluge i sluškinje, muèala bih, premda neprijatelj ne bi mogao naknaditi štete caru.
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
A car Asvir progovori i reèe carici Jestiri: ko je taj? i gdje je taj koji se usudio tako èiniti?
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
A Jestira reèe: protivnik i neprijatelj ovaj je zlikovac Aman. A Aman se uplaši od cara i od carice.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
Tada car gnjevan usta od vina i otide u vrt kod dvora, a Aman osta da moli za život svoj caricu Jestiru, jer vidje da je car naumio zlo po nj.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
Potom se car vrati iz vrta dvorskoga u kuæu gdje bješe pio vino; a Aman bješe pao na odar gdje sjeðaše Jestira. I car reèe: eda li æe i caricu osramotiti kod mene u kuæi? Èim ta rijeè izide iz usta carevijeh, pokriše lice Amanu.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
I Arvona, jedan od dvorana carevijeh, reèe: evo i vješala što je naèinio Aman za Mardoheja koji je govorio dobro po cara stoje kod kuæe Amanove, visoka pedeset lakata. I reèe car: objesite ga na njih.
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
I tako objesiše Amana na vješala koja bješe pripravio Mardoheju. I gnjev carev utiša se.

< Estere 7 >