< Estere 7 >
1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
Napan ngarud ti ari ken ni Haman iti padaya ni Ester.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
Iti daytoy a maikadua nga aldaw, kabayatan nga idasdasarda ti arak, kinuna ti ari kenni Ester, “Ania ti dawatmo, Reyna Ester? Maipaayto daytoy kenka. Ania ti kiddawmo? Agingga iti kagudua ti pagarian, maipaayto daytoy.”
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
Ket simmungbat ni Reyna Ester, “No nakasarakak iti pabor kadagiti matam, ari, ken no makaay-ayo daytoy kenka, ipalubosmo a maited kaniak ti biagko—daytoy ti dawatko, ken kiddawek met daytoy para kadagiti tattaok.
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
Ta nailakokami, siak ken dagiti tattaok, tapno madadael, mapapatay, ken mapukaw. No nailakokami laeng iti pannakatagabu, a kas tagabu a lallaki ken babbai, agulimekak latta koman ta saan nga umno a rengrengen ti ari gapu laeng iti kastoy a riribuk.”
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
Ket kinuna ni Ari Ahasuero kenni Ester a reyna, “Siasino isuna? Sadino ti ayan dayta a tao a natured a nangpanunot tapno aramidenna ti kasta a banag?”
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
Kinuna ni Ester, “Ti naunget a lalaki, dayta a kabusor, ket daytoy managdakdakes a ni Haman!” Ket kasta unay ti buteng ni Haman iti sangoanan ti ari ken ti reyna.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
Sipupungtot a timmakder ti ari gapu iti panaginomna iti arak iti dayta a pannangan ket napan iti minuyongan ti palasio, ngem nagtalinaed ni Haman tapno agpakaasi kenni Reyna Ester para iti biagna. Nadlawna nga ikedkeddengen ti ari ti didigra a maibusor kenkuana.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
Kalpasanna, nagsubli ti ari iti siled manipud iti minuyongan ti palasio a nakaidasaran ti arak. Nakapakleb ni Haman iti sofa nga isu ti ayan ni Ester. Kinuna ti ari, “Ramesenna kadi ti reyna iti imatangko, iti bukodko a balay?” Apaman a naisao ti ari daytoy, inabungotan dagiti adipen ti rupa ni Haman.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
Ket kinuna ni Harbona, a maysa kadagiti opisial nga agserserbi iti ari, “Maysa a pagbitayan a lima a cubico ti kangatona ti nakatakder iti abay ti balay ni Haman. Inaramidna daytoy para kenni Mardokeo, daydiay a nagsarita tapno masalakniban ti ari.” Kinuna ti ari, “Bitayenyo isuna sadiay.”
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
Isu nga imbitinda ni Haman iti pagbitayan nga insaganana para kenni Mardokeo. Ket bimmaaw ti pungtot ti ari.