< Estere 7 >

1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
Le roi et Haman vinrent donc au banquet avec la reine Esther.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
Le roi dit encore à Esther, le deuxième jour, au banquet du vin: « Quelle est ta demande, reine Esther? Elle te sera accordée. Quelle est ta requête? Elle sera exécutée jusqu'à la moitié du royaume. »
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
Alors la reine Esther prit la parole et dit: Si j'ai trouvé grâce à tes yeux, ô roi, et si le roi le trouve bon, que ma vie me soit accordée selon ma demande, et mon peuple selon ma requête.
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
Car nous sommes vendus, moi et mon peuple, pour être détruits, pour être tués et pour périr. Mais si nous avions été vendus pour des esclaves mâles et femelles, je me serais tu, bien que l'adversaire n'ait pu compenser la perte du roi. »
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
Alors le roi Assuérus dit à la reine Esther: « Qui est-il, et où est-il, celui qui a osé présumer dans son cœur d'agir ainsi? »
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
Esther dit: « Un adversaire et un ennemi, même ce méchant Haman! » Alors Haman eut peur devant le roi et la reine.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
Le roi, dans sa colère, se leva du banquet de vin et alla dans le jardin du palais. Haman se leva pour demander sa vie à la reine Esther, car il voyait que le roi avait décidé de lui faire du mal.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
Alors le roi revint du jardin du palais dans le lieu du banquet du vin, et Haman était tombé sur le divan où se trouvait Esther. Le roi dit alors: « Ira-t-il jusqu'à agresser la reine devant moi, dans la maison? » Comme la parole sortait de la bouche du roi, on couvrit le visage d'Haman.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
Alors Harbonah, l'un des eunuques qui étaient avec le roi, dit: « Voici que la potence haute de cinquante coudées, qu'Haman a fabriquée pour Mardochée, qui a dit du bien du roi, se trouve à la maison d'Haman. » Le roi a dit: « Pendez-le! »
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
Et ils pendirent Haman au gibet qu'il avait préparé pour Mardochée. Et la colère du roi fut apaisée.

< Estere 7 >