< Estere 7 >

1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
And so the king and Haman entered to drink with the queen.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
And the king said to her again on the second day, after he was warmed with wine, “What is your request, Esther, so that it may be given to you? And what do you want done? Even if you ask for half of my kingdom, you will obtain it.”
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
She answered him, “If I have found favor in your eyes, O king, and if it pleases you, spare my soul, I ask you, and spare my people, I beg you.
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
For I and my people have been handed over to be crushed, to be slain, and to perish. And if we were only being sold as servants and slaves, the evil might be tolerable, and I would have mourned in silence. But now our enemy is one whose cruelty overflows upon the king.”
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
And king Artaxerxes answered and said, “Who is this, and of what power, that he would dare to do these things?”
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
And Esther said, “This is our most wicked enemy and foe: Haman!” Hearing this, Haman was suddenly dumbfounded, unable to bear the faces of the king and the queen.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
But the king, being angry, rose up and, from the place of the feast, entered into the arboretum of the garden. Haman likewise rose up to entreat Esther the queen for his soul, for he understood that evil was prepared for him by the king.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
When the king returned from the arboretum of the garden and entered into the place of the feast, he found Haman collapsed on the couch on which Esther lay, and he said, “And now he wishes to oppress the queen, in my presence, in my house!” The word had not yet gone out of the king’s mouth, and immediately they covered his face.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
And Harbona, one of the eunuchs who stood in ministry to the king, said, “Behold the wood, which he had prepared for Mordecai, who spoke up on behalf of the king, stands in Haman’s house, having a height of fifty cubits.” The king said to him, “Hang him from it.”
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
And so Haman was hanged on the gallows, which he had prepared for Mordecai, and the king’s anger was quieted.

< Estere 7 >