< Estere 7 >

1 Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
Kralj i Haman dođoše na gozbu kraljici Esteri.
2 Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
I toga drugoga dana, dok se pilo vino, reče kralj Esteri: "Koja ti je molba, kraljice Estero? Bit će ti udovoljena! Koja je tvoja želja? Ako je i pola kraljevstva, bit će ti!"
3 Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
Kraljica Estera odgovori: "Ako sam, kralju, našla milost u tvojim očima i ako ti je s voljom, neka mi se u ime molbe pokloni život, a u ime želje moj narod!
4 Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
Jer smo ja i narod moj predani za zator, klanje, uništenje. Da smo predani u roblje, šutjela bih jer nevolja ne bi bila štetna po kralja."
5 Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
Ali kralj Ahasver upade kraljici Esteri u riječ pa je upita: "Tko je taj? Gdje je taj koji je namislio takvo što učiniti?" Estera tada odgovori: "Progonitelj i neprijatelj jest Haman, ovaj zlikovac!"
6 Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
Haman se zaprepasti pred kraljem i kraljicom.
7 Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
Kralj, gnjevan, ostavi vino te ode u vrt palače. Haman osta uz kraljicu da je moli za svoj život, jer je uvidio da je njegova nesreća pred kraljem gotova.
8 Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
Kralj se vrati iz vrta u dvoranu gdje se pilo vino. Dotle Haman bijaše pao na počivaljku na kojoj se nalazila Estera. "Pokušavaš još i nasilje nad kraljicom, i to u mome vlastitom domu?" - povika kralj. Tek što su te riječi izletjele iz kraljevih usta, pokriše lice Hamanu.
9 Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
Tada kaza Harbona, jedan od dvorana koji su stajali u službi kraljevoj: "Eno i vješala što ih je Haman pripravio za Mordokaja koji je govorio u korist kraljevu. Nalaze se kraj Hamanove kuće i visoka su pedeset lakata." Kralj zapovjedi: "Objesite ga na njih!"
10 Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.
Hamana objesiše na vješala koja bijaše pripravio Mordokaju, i kraljeva se srdžba utiša.

< Estere 7 >