< Estere 6 >

1 Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
Ону ноћ не могаше цар спавати, и заповеди те му донесоше књигу од знаменитих догађаја, дневнике, те је читаше цару.
2 Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
И нађе се записано како је Мардохеј проказао за Вихтана и Тереса, два дворанина, који чуваху стражу на прагу, да гледају да дигну руке на цара Асвира.
3 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
Тада рече цар: Каква је част и како је добро учињено Мардохеју за то? А момци цареви, слуге његове, рекоше: Није му учињено ништа.
4 Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
А цар рече: Ко је у трему? А Аман беше дошао у спољашњи трем двора царевог да каже цару да се обеси Мардохеј на вешала која му је приправио.
5 Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
А момци цареви рекоше му: Гле, Аман стоји у трему. А цар рече: Нека дође.
6 Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
И Аман дође, а цар му рече: Шта треба учинити човеку ког цар хоће да прослави? А Аман рече у себи: Кога би цар хтео прославити ако не мене?
7 Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
И рече Аман цару: Кога цар хоће да прослави,
8 Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
Треба донети царско одело које цар носи, и довести коња на коме цар јаше, и метнути му на главу венац царски;
9 Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
И одело и коња треба дати коме између највећих кнезова царевих да обуку човека оног ког цар хоће да прослави, па да га проведу на коњу по улицама градским и вичу пред њим: Овако бива човеку кога цар хоће да прослави.
10 Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
Тада рече цар Аману: Брже узми одело и коња као што рече, и учини тако Мардохеју, Јудејцу који седи на вратима царевим; немој изоставити ништа што си рекао.
11 Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
И узе Аман одело и коња, и обуче Мардохеја и проведе га на коњу по улицама градским вичући пред њим: Овако бива човеку кога цар хоће да прослави.
12 Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
Потом се врати Мардохеј на врата царева, а Аман брже отиде кући својој жалостан и покривене главе.
13 Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
И приповеди Аман Сереси, жени својој и свим пријатељима својим све што му се догоди. Тада му рекоше мудраци његови и Сереса жена његова: Кад је од јудејског семена Мардохеј пред којим си почео падати, нећеш му одолети, него ћеш пасти пред њим.
14 Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.
И док они још говораху с њим, дођоше дворани цареви и брже одведоше Амана на обед који зготови Јестира.

< Estere 6 >