< Estere 6 >

1 Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
That night the king was unable to sleep, so he [summoned] a servant [and] told [him] to bring the records of what had happened during all the time he had been king. [So the servant brought the records] and read some of them to the king.
2 Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
[The servant read about] Bigthana and Teresh, the two men who had guarded the entrance to the king’s rooms. He read the account of when Mordecai had found out that they planned to assassinate the king [and that he had told the king about it].
3 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
The king asked [some of his servants], “What did we do to reward Mordecai or show that we appreciate what he did?” The servants replied, “We did not do anything for him.”
4 Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
At that moment, Haman entered the outer courtyard of the palace. He wanted to talk to the king about hanging Mordecai on the gallows that he had [just] set up. The king [saw him and] said, “Who is [that out there] in the courtyard?”
5 Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
His servants replied, “That is Haman standing there in the courtyard.” The king said, “Bring him in [here]!”
6 Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
When Haman came in, the king asked him, “What should I do for a man whom I want to honor?” Haman thought to himself, “(Whom would the king like to honor more than me?/I think there is no one whom the king would like to honor more than me!)” [RHQ]
7 Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
So he replied to the king, “If there is someone you wish to honor,
8 Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
you should [tell your servants to] bring him one of the robes you wear [you to show that you are] the king. Also tell them to bring one of the horses you have ridden. Tell them to put a fancy headdress on the horse’s head to show that it belongs to you, the king.
9 Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
Then tell one of your very important officials to put the robe on the man whom you want to honor, and tell that man to sit on the horse, and then lead the horse through the city streets. And tell that official to keep shouting, ‘This is what (the king does/is doing) for the man whom he wants to honor!’”
10 Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
The king replied to Haman, “[Fine]! Go and do what you said immediately! Get my robe and my horse, and do just what you suggested! Do it for Mordecai, the Jew, who is sitting [outside] at the gate of the palace. Do not forget anything that you suggested!”
11 Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
So Haman did what the king said. He got the robe and the horse. He put the robe on Mordecai, and as Mordecai sat on the horse, Haman led the horse through the city streets proclaiming “This is what the king (does/is doing) for the man whom the king wants to honor!”
12 Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
Then, Mordecai returned [and sat] at the gate of the palace. But Haman hurried home, covering his face [because he felt] completely disgraced/humiliated.
13 Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
He told his wife Zeresh and his friends everything that had happened to him that day. Then his wife and his friends said to him, “Mordecai, the man who has caused you to be completely disgraced/humiliated, is a Jew. [It is clear that the God whom the Jews worship is fighting for them.] So you will never be able to defeat Mordecai. He will defeat you!”
14 Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.
And while they were still talking, some of the king’s officials arrived to take Haman quickly to the banquet/feast that Esther had prepared.

< Estere 6 >