< Estere 6 >
1 Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
That night the king wasn't able to sleep, so he ordered the Book of Records of the King's Reign brought in so it could be read to him.
2 Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
There he discovered the account of what Mordecai had reported about Bigthana and Teresh, the two king's eunuchs who were doorkeepers who had plotted to assassinate King Xerxes.
3 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
“What honor or position did Morcedai receive as a reward for doing this?” asked the king. “Nothing has been done for him,” replied the king's attendants.
4 Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
“Who's here in the court?” the king asked. Haman had just happened to arrive in the outer court of the royal palace to ask the king to have Mordecai impaled on the pole he had set up for him.
5 Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
The king's attendants told him, “Haman is waiting in the court.” “Tell him to come in,” the king ordered.
6 Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
When Haman came in, the king asked him, “What should be done for a man the king wants to honor?” Haman said to himself, “Who would the king want to honor except me?”
7 Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
So Haman said to the king, “A man whom the king wants to honor
8 Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
should be brought royal robes the king has worn, a horse the king has ridden and which has a royal headdress on its head.
9 Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
Have the robes and the horse handed over to one of the king's highest officials and nobles. Let him make sure the man the king wishes to honor is dressed in the royal robes and that he rides on the horse through the city streets, and have the official announce before him, ‘This is what is done for the man the king wishes to honor!’”
10 Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
Then the king told Haman, “Right! Off you go! Quickly get the royal robes and the horse, and do just what you've said for Mordecai the Jew sitting at the palace gate. Don't leave out anything that you mentioned.”
11 Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
Haman went and got the robes and the horse. He dressed Mordecai and placed him on the horse, and led him through the streets of the city, shouting before him, “This is what is done for the man the king wishes to honor!”
12 Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
Mordecai went back to the palace gate, but Haman rushed home, crying and covering his head in shame.
13 Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
Haman explained to his wife Zeresh and all his friends what had happened to him. These wise friends and his wife Zeresh told him, “If Mordecai is one of the Jewish people, and you have already begun to lose status before him—you won't be able to beat him! You're going to lose to him, you're going to fall!”
14 Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.
While they were still talking to him, the king's eunuchs arrived and quickly took Haman to the dinner which Esther had prepared.