< Estere 5 >

1 Tsiku lachitatu Estere anavala zovala zake zaufumu ndipo anayima mʼbwalo la mʼkati la nyumba yaufumu choyangʼana ku chipinda chachikulu cha mfumu. Mfumu inakhala pa mpando waufumu mʼchipinda chachikulu moyangʼana ku chipata cholowera mʼnyumba yaufumu.
A dnia trzeciego ubrawszy się Ester w ubiór królewski, stanęła w sieni wewnętrznej domu królewskiego przeciw pałacowi królewskiemu. A król siedział na stolicy królewskiej swojej w pałacu królewskim przeciwko drzwiom domu.
2 Mfumu itaona Estere atayima mʼbwalomo inakondwera naye ndipo anamuloza ndi ndodo yagolide imene inali mʼdzanja lake. Choncho Estere anayandikira ndi kukhudza msonga ya ndodoyo.
A gdy ujrzał król Esterę królowę stojącą w sieni, znalazła łaskę w oczach jego, i wyciągnął król do Estery sceptr złoty, który trzymał w ręce swej. Tedy przystąpiwszy Ester dotknęła się końca sceptru.
3 Kenaka mfumu inati kwa iye, “Kodi mukufuna chiyani, inu mfumukazi Estere? Nanga pempho lanu ndi chiyani? Ngakhale mutapempha theka la ufumu, ndidzakupatsani.”
I rzekł do niej król: Cóż ci królowa Ester? a co za prośba twoja? Choćbyś też i o połowę królestwa prosiła, tedyć będzie dano.
4 Ndipo Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni, mfumu, mubwere lero pamodzi ndi Hamani kuphwando limene ndakonzera inu mfumu.”
I odpowiedziała Ester: Jeźli się królowi podoba, niech przyjdzie król i Haman dzisiaj na ucztę, którąm dla niego nagotowała.
5 Mfumu inati, “Muwuzeni abwere Hamani msanga, kotero kuti tichite monga Estere wapempha.” Choncho mfumu ndi Hamani anafika kuphwando limene Estere anakonza.
I rzekł król: Zawołajcie co rychlej Hamana, aby dosyć uczynił woli Estery. Przyszedł tedy król i Haman na onę ucztę, którą była sprawiła Ester.
6 Akumwa vinyo, mfumu inamufunsano Estere kuti, “Kodi ukupempha chiyani tsopano? Chimene uti upemphe ndikupatsa. Chopempha chako ndi chiti? Ngakhale utafuna mpaka theka la ufumu, ndidzakupatsa.”
Potem król rzekł do Estery, napiwszy się wina: Cóż za prośba twoja? a będzieć dano; co za żądość twoja? Choćbyś i o połowę królestwa prosiła, będzieć dano.
7 Estere anayankha kuti, “Pempho langa ndi chofuna changa ndi ichi:
Na to odpowiedziała Ester, i rzekła: Żądość moja, i prośba moja ta jest:
8 Ngati mwandikomera mtima mfumu ndiponso ngati chingakukondweretseni mfumu kundipatsa chimene ndapempha ndi kuchita zimene ndifuna, mubwere mawa inu mfumu ndi Hamani ku phwando limene ndidzakukonzerani. Ndipo ndidzakuyankhani mfumu funso lanu.”
Jeźlim znalazła łaskę w oczach królewskich, a jeźli się królowi podoba, aby przyzwolił na prośbę moję, i wypełnił żądość moję, aby jeszcze przyszedł król i Haman na ucztę, którą im zgotuję, a jutro uczynię według słowa królewskiego.
9 Tsiku limenelo Hamani anatuluka wokondwa ndi wosangalala kwambiri. Koma ataona Mordekai pa chipata cha mfumu ndi kuti sanayimirire kapena kumupatsa ulemu pamene iye amadutsa, Hamani anamukwiyira kwambiri,
A tak wyszedł Haman dnia onego wesoły, i z dobrą myślą; ale gdy ujrzał Haman Mardocheusza w bramie królewskiej, że ani powstał, ani się ruszył przed nim, napełniony był Haman przeciwko Mardocheuszowi popędliwością.
10 komabe Hamani anadziletsa ndipo anapita ku nyumba kwake. Anayitana abwenzi ake pamodzi ndi mkazi wake Zeresi.
Wszakże zatrzymał się Haman, aż przyszedł do domu swego, a posławszy wezwał przyjaciół swoich, i Zeres, żony swej.
11 Hamani anawawuza za kuchuluka kwa chuma chake ndi kuti anali ndi ana aamuna ambiri. Anawawuzanso za mmene mfumu inamukwezera ndi kumuyika kukhala woposa nduna ndi olemekezeka onse.
I powiadał im Haman o sławie bogactw swoich, i o mnóstwie synów swych, i o wszystkiem, jako go uwielbił król, i jako go wywyższył nad innych książąt i sług królewskich.
12 Hamani anawonjeza kuti, “Ndipotu si zokhazi. Ndine ndekha amene ndayitanidwa pamodzi ndi mfumu kuphwando limene mfumukazi Estere anatikonzera. Ndipo mawa wandiyitananso pamodzi ndi mfumu.
Nadto rzekł Haman: Nawet nie wezwała Ester królowa z królem na ucztę, którą nagotowała, tylko mnie a jeszcze i na jutro jestem od niej z królem wezwany.
13 Koma zonsezi sindikhutira nazo ndikamaona nthawi zonse Myuda uja Mordekai atakhala pa chipata cha mfumu.”
Ale mi to wszystko za nic, pokąd ja widzę Mardocheusza Żyda, siedzącego u bramy królewskiej.
14 Mkazi wake Zeresi ndi abwenzi ake onse aja anamuwuza kuti, “Anthu apange mtanda wotalika mamita 23 ndipo mmawa upemphe mfumu kuti anthu akhomerepo Mordekai. Kenaka upite ndi mfumu kuphwando mokondwa.” Hamani anakondwera ndi uphungu umenewu ndipo mtanda unapangidwa.
I rzekła mu Zeres, żona jego, i wszyscy przyjaciele jego: Niech postawią szubienicę wysoką na pięćdziesiąt łokci, a rano mów do króla, aby powieszono Mardocheusza na niej, a idź z królem na ucztę z weselem. I upodobała się ta rada Hamanowi, i kazał postawić szubienicę.

< Estere 5 >