< Estere 4 >
1 Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
Kwathi uModekhayi esezwile ngakho konke okwasekwenziwe, wadabula iziqgoko zakhe, wagqoka amasaka okulila, wazihuqa ngomlotha, waphuma wangena phakathi komuzi ekhala kakhulu njalo kabuhlungukazi.
2 Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
Kodwa wahamba wayafika esangweni lenkosi, ngoba akulamuntu owayevunyelwa ukungena egqoke amasaka okulila.
3 Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
Kuzozonke izabelo lapho isimiso somthetho lomlayo wenkosi okwafika khona, kwaba lokulila okukhulu kubaJuda, bazila ukudla, bakhala njalo belila. Abanengi balala emlotheni begqoke amasaka okulila.
4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
Kwathi izinceku zika-Esta kanye labathenwa bakhe befika bemtshela ngoModekhayi, waba lokudabuka okukhulu. Wamthumela izembatho zokuthi agqoke endaweni yamasaka okulila, kodwa wala ukuzamukela.
5 Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
U-Esta wasebiza uHathakhi, omunye wabathenwa benkosi owayekhethwe ukuba yinceku yakhe, wamlaya ukuba ayedingisisa lokho okwakukhathaza uModekhayi lembangela yakho.
6 Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
Ngakho uHathakhi waya kuModekhayi egcekeni ledolobho phambi kwesango lenkosi.
7 Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
UModekhayi wamtshela konke okwakwenzakale kuye, kugoqela inani lemali uHamani ayethembise ukulibhadala lingene enothweni yenkosi kusenzelwa ukubhujiswa kwamaJuda.
8 Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
Wamupha njalo amazwi esimemezelo leso ayesekhutshwe aba ngumthetho omisiweyo wokubhujiswa kwabo, owawumenyezelwe eSusa, ukuze awutshengise u-Esta njalo amchazele ngawo; njalo wamtshela ukuthi amkhuthaze ukuba aye enkosini ukuyacela isihawu sayo encengela abantu bakibo.
9 Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
UHathakhi wabuyela wayamtshela u-Esta lokho okwakukhulunywe nguModekhayi.
10 Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
Yena wasemlaya ukuba athi kuModekhayi,
11 “Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
“Zonke iziphathamandla zenkosi kanye labasezigodlweni ezabelweni bayakwazi ukuthi inkosi ilomthetho owodwa zwi kuloba yiphi indoda loba owesifazane osondela enkosini angene endlini ephakathi engabizwanga; kufanele abulawe, ngaphandle kokuba inkosi yelule intonga yayo yegolide imkhombe ngayo ukuze impilo yakhe iphephe. Kodwa, sekwedlule amalanga angamatshumi amathathu selokhu ngacina ukubizelwa enkosini.”
12 Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
Kwathi amazwi ka-Esta ebikwa kuModekhayi,
13 Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
waphendula wathi: “Ungacabangi ukuthi ngoba wena usendlini yenkosi nguwe wedwa kuwo wonke amaJuda ozaphepha.
14 Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
Nxa ungala uthule ngalesisikhathi, usizo lokukhululwa kwamaJuda kuzavela kwenye indawo, kodwa wena kanye lemuli kayihlo lizabhubha. Njalo kwazi bani, ukuthi uze kulesi sikhundla sobukhosi ngenxa yesikhathi esinjengalesi na?”
15 Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
U-Esta wasethumela impendulo le kuModekhayi:
16 “Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
“Hamba uyebuthanisa ndawonye wonke amaJuda aseSusa, lingizilele ukudla. Lingaze ladla loba ukunatha okwensuku ezintathu, ebusuku lemini. Mina kanye lezincekukazi zami sizazila njengani. Nxa lokhu sekwenziwe, ngizakuya enkosini loba nje lokho kungekho emthethweni. Nxa ngisifa, ngiyabe ngifile.”
17 Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.
Ngakho uModekhayi wasuka wayakwenza lokho okwakulaywe ngu-Esta.