< Estere 4 >
1 Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
Kad nu Mardakajs dabūja zināt visu, kas bija noticis, tad Mardakajs saplosīja savas drēbes un apvilka maisu ar pelniem, un gāja pilsētas vidū, un brēca ar lielu un rūgtu brēkšanu.
2 Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
Un viņš nāca priekš ķēniņa vārtiem; jo (pašos) ķēniņa vārtos neviens nevarēja ieiet ar maisu apģērbies.
3 Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
Un visās valstīs un vietās, kurp ķēniņa vārds un viņa pavēle nonāca, bija lielas bēdas Jūdiem ar gavēšanu un raudāšanu un bēdāšanos, un daudzi gulēja maisos un pelnos.
4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
Tad Esteres meitas un viņas kambarjunkuri nāca un viņai to stāstīja, un ķēniņiene iztrūcinājās ļoti un viņa sūtīja drēbes, Mardakaju apģērbt un to maisu viņam atņemt, bet viņš tās nepieņēma.
5 Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
Tad Estere aicināja Ataku, vienu no ķēniņa kambarjunkuriem, kas viņai bija iedots, un viņa pavēlēja Mardakaju izvaicāt, kas un kāpēc tas esot?
6 Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
Un Ataks izgāja pie Mardakaju uz pilsētas ielu priekš ķēniņa vārtiem.
7 Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
Tad Mardakajs viņam stāstīja visu, kas tam bija noticis, un to nospriesto sudrabu, ko Amans bija solījis ķēniņa mantu namā iesvērt par Jūdiem, ka tie taptu izdeldēti.
8 Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
Un viņš tam deva tās rakstītās pavēles norakstu, kas Sūsanā bija dota, ka tie taptu izdeldēti, lai viņš to Esterei rādītu un viņai stāstītu, un viņai pavēlētu, iet pie ķēniņa, viņu piesaukt un lūgt savas tautas dēļ.
9 Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
Tad Ataks nāca un sacīja Esterei Mardakaja vārdus.
10 Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
Un Estere sacīja uz Ataku un lika Mardakajam teikt:
11 “Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
Visi ķēniņa kalpi un visi ķēniņa valsts ļaudis zina, ka ikkatrs, vīrs vai sieva, kas pie ķēniņa nāk iekšējā pagalmā, kas nav aicināts, tam nospriests, to nokaut, (bez vien, kad ķēniņš to zelta scepteri viņam piesniedz, ka viņš paliek dzīvs). Bet es neesmu aicināta pie ķēniņa nākt nu jau trīsdesmit dienas.
12 Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
Un Esteres vārdus atsacīja Mardakajam.
13 Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
Tad Mardakajs Esterei atkal lika sacīt: nedomā savā prātā, ka tu savu dzīvību ķēniņa namā labāki izglābsi nekā tie citi Jūdi.
14 Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
Jo ja tu šinī laikā klusu cietīsi, tad Jūdiem nāks palīdzība un izglābšana no citas vietas, bet tu un tava tēva nams iesiet bojā. Un kas zina, vai tu šī laika labad neesi iecelta par ķēniņieni?
15 Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
Tad Estere Mardakajam lika sacīt:
16 “Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
Ej un sapulcē visus Jūdus, kas Sūsanā atrodas, un gavējiet priekš manis un neēdiet, nedz dzeriet trīs dienas, ne dienu ne nakti; es ar savām meitām, mēs tāpat gavēsim, un tā es iešu pie ķēniņa, jebšu tas nav pēc likuma; ja tad jāiet bojā, tad jāiet bojā.
17 Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.
Tad Mardakajs nogāja un darīja visu, ko Estere viņam bija pavēlējusi.