< Estere 4 >

1 Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
When Mordecai learned of all that had been done, he tore his clothes and put on sackcloth and ashes. He went out into the middle of the city, and cried out with a loud and a bitter cry.
2 Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
He went up only as far as the king's gate, because no one was allowed to go through it clothed in sackcloth.
3 Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
In every province, wherever the king's command and decree reached, there was great mourning among the Jews, with fasting, weeping, and lamenting. Many of them lay in sackcloth and ashes.
4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
When Esther's young women and her servants came and told her, the queen was in great distress. She sent garments to clothe Mordecai (so he could take off his sackcloth), but he would not accept them.
5 Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
Then Esther called for Hathak, one of the king's officials who had been assigned to serve her. She ordered him to go to Mordecai to learn what had happened and what it meant.
6 Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
So Hathak went to Mordecai in the city square in front of the king's gate.
7 Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
Mordecai reported to him all that had happened to him, and the total amount of the silver that Haman had promised to weigh out and put into the king's treasuries in order to put the Jews to death.
8 Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
He also gave him a copy of the decree that was issued in Susa for the Jews' destruction. He did this so that Hathak could show it to Esther, and that he should give her the responsibility of going to the king to beg for his favor, and to plead with him on behalf of her people.
9 Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
So Hathak went and told Esther what Mordecai had said.
10 Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
Then Esther spoke to Hathak and told him to go back to Mordecai.
11 “Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
She said, “All the king's servants and the people of the king's provinces know that if any man or woman goes to the king inside the inner courtyard without being summoned, there is only one law: That he must be put to death—except for anyone to whom the king holds out the golden scepter so that he may live. I have not been called to come to the king these thirty days.”
12 Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
So Hathak reported Esther's words to Mordecai.
13 Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
Mordecai sent back this message: “You must not think that in the king's palace, you will escape any more than all the other Jews.
14 Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
If you remain silent at this time, relief and rescue will rise up for the Jews from another place, but you and your father's house will perish. Who knows whether you have come to this royal position for such a time as this?”
15 Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
Then Esther sent this message to Mordecai,
16 “Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
“Go, gather together all the Jews who live in Susa, and fast for me. Do not eat nor drink for three days, night or day. My young girls and I will fast in the same way. Then I will go to the king, even though it is against the law, and if I perish, I perish.”
17 Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.
Mordecai went and did all that Esther told him to do.

< Estere 4 >