< Estere 3 >
1 Zitachitika izi, mfumu Ahasiwero anamukweza Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, anamulemekeza ndikumupatsa mpando wa ulemu kuposa nduna zina zonse.
After these things, King Ahasuerus promoted Haman son of Hammedatha the Agagite, and placed his seat of authority above all the officials who were with him.
2 Atumiki onse a mfumu amene anali pa chipata cha nyumba ya mfumu ankagwadira ndi kuweramira Hamani monga mwa lamulo la mfumu. Koma Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira.
All the king's servants who were at the king's gate always knelt and prostrated themselves to Haman, as the king had ordered them to do. But Mordecai neither knelt nor prostrated himself.
3 Kenaka atumiki a mfumu amene anali pa chipata anafunsa Mordekai kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani sumvera lamulo la mfumu?”
Then the king's servants who were at the king's gate said to Mordecai, “Why do you disobey the king's command?”
4 Tsiku ndi tsiku ankayankhula naye koma iye sanamverebe. Choncho anamuwuza Hamani kuti aone ngati angavomereze khalidwe lotere la Mordekai, popeza anawawuza kuti anali Myuda.
They spoke with him day after day, but he refused to comply with their demands. So they spoke with Haman to see if the matter about Mordecai would remain like that, for he had told them that he was a Jew.
5 Hamani ataona kuti Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira, anapsa mtima kwambiri.
When Haman saw that Mordecai did not kneel and bow down to him, Haman was filled with rage.
6 Hamani atamva kuti Mordekai anali Myuda, anatsimikiza kuti ndi kosakwanira kulanga Mordekai yekha. Mʼmalo mwake anapeza njira yowonongera Ayuda onse okhala mʼdziko lonse limene mfumu Ahasiwero ankalamulira.
He had contempt for the idea of killing only Mordecai, for the king's servants had told him who Mordecai's people were. Haman wanted to exterminate all the Jews, the people of Mordecai, who were in the entire kingdom of Ahasuerus.
7 Mwezi woyamba, umene ndi mwezi wa Nisani, chaka cha khumi ndi chiwiri cha ufumu wa Ahasiwero anachita maere, otchedwa Purimu pamaso pa Hamani kuti apeze tsiku ndi mwezi woyenera. Ndipo maere anagwera pa mwezi wa khumi ndi chiwiri ndiwo mwezi wa Adara.
In the first month (which is the month of Nisan), in the twelfth year of King Ahasuerus, the Pur—that is the lot—was thrown before Haman, to select a day and month. They cast the lot over and over until the lot fell on the twelfth month (which is the month of Adar).
8 Kenaka Hamani anakawuza mfumu Ahasiwero kuti, “Pali mtundu wina wa anthu umene unabalalika ndipo wamwazikana pa mitundu ina mʼzigawo zonse za ufumu wanu umene miyambo yawo ndi yosiyana ndi ya anthu ena onse ndiponso amene safuna kumvera malamulo a mfumu, kotero si chinthu cha phindu kuti mfumu iwalekerere anthu otere.
Then Haman said to King Ahasuerus, “There is a certain people scattered and distributed among all the provinces of your kingdom. Their laws are different from those of other people, and they do not keep the king's laws, so it is not suitable for the king to let them stay.
9 Ngati chingakukomereni mfumu, ikani lamulo kuti tiwawononge, ndipo ndidzalipira matalente 10,000 asiliva mosungiramo chuma cha mfumu za anthu amene adzachite ntchito imeneyi.”
If it please the king, give a command to kill them, and I will weigh out ten thousand talents of silver into the hands of those who are in charge of the king's business, for them to put it into the king's treasury.”
10 Choncho mfumu inavula mphete yodindira ku chala chake ndi kumupatsa Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, mdani wa Ayuda.
Then the king took the signet ring from his hand and gave it to Haman son of Hammedatha the Agagite, the enemy of the Jews.
11 Mfumu inati kwa Hamani, “Sunga ndalamazo, ndipo uchite ndi anthuwo monga ufunira.”
The king said to Haman, “I will see that the money is given back to you and your people. You will do with it whatever you wish.”
12 Alembi analemba zonse zimene Hamani analamula mʼmakalata opita kwa akazembe a mfumu, abwanamkubwa a zigawo zonse ndi kwa oyangʼanira mtundu uliwonse wa anthu. Kalatazo zinali za mʼchiyankhulo cha mtundu uliwonse ndipo zinalembedwa mʼdzina la Mfumu Ahasiwero ndi kusindikizidwa ndi mphete yake.
Then the king's scribes were summoned on the thirteenth day of the first month, and a decree containing all that Haman had commanded was written to the king's provincial governors, those who were over all the provinces, to the governors of all the various peoples, and to the officials of all the people, to every province in their own writing, and to every people in their own language. It was written in the name of King Ahasuerus and was sealed with his ring.
13 Makalatawa anawatumiza amithenga ku zigawo zonse za mfumu kuti awononge, aphe ndi kufafaniziratu a Yuda onse, anyamata, anthu okalamba, ana ndi amayi, pa tsiku limodzi la 13 la mwezi wa Adara ndipo alande katundu wawo.
Documents were hand-delivered by couriers to all the king's provinces, to annihilate, kill, and destroy all Jews, from young to old, children and women, in one day—on the thirteenth day of the twelfth month (which is the month of Adar)—and to plunder their possessions.
14 Mwachidule kalatayi inanena kuti mawu olembedwamowo anayenera kuperekedwa ngati lamulo mʼchigawo chilichonse ndi kuti anthu a mtundu uliwonse adziwe ndi kukhala okonzeka pa tsikulo.
A copy of the letter was made law in every province. In every province it was made known to all the people that they should prepare for this day.
15 Potsata lamulo la mfumu, amithenga aja anapita mwachangu ndipo lamuloli linaperekedwanso ku Susa, likulu la dziko. Mfumu ndi Hamani anakhala pansi ndikumamwa, koma mzinda onse wa Susa unasokonezeka.
The couriers went out and hurried to distribute the king's order. The decree was also distributed within the fortress of Susa. The king and Haman sat down to drink, but the city of Susa was in turmoil.