< Estere 2 >

1 Pambuyo pake mtima wa Ahasiwero utatsika, Ahasiwero anakumbukira Vasiti ndi zimene anachita Vasitiyo. Anakumbukiranso lamulo lomukhudza limene anasindikiza.
Emva kwalezizinto, ulaka lwenkosi uAhasuwerusi seludedile, wamkhumbula uVashiti, lalokho ayekwenzile, lalokho okwaqunywa ngaye.
2 Tsono anyamata a mfumu amene ankamutumikira anati, “Mfumu, akufunireni anamwali okongola.
Izinceku zenkosi ezaziyisebenzela zasezisithi: Kakudingelwe inkosi amantombazana, izintombi ezikhangeleka kuhle.
3 Mfumu isankhe oyangʼanira pa chigawo chilichonse cha ufumu wake kuti abwere nawo pamodzi anamwali onse okongola ku nyumba yosungira akazi ku Susa. Hegai, mdindo wofulidwa wa mfumu, amene amayangʼanira amayi, akhale wosamalira anamwaliwa ndipo aziwapatsa mafuta odzola.
Inkosi imise-ke ababonisi kuzo zonke izabelo zombuso, ukuze babuthanise wonke amantombazana, izintombi ezikhangeleka kuhle, eShushani isigodlo, endlini yabesifazana, esandleni sikaHegayi, umthenwa wenkosi, umlondolozi wabesifazana, lokunika okokuqhola kwawo.
4 Ndipo namwali amene mfumu yakondwera naye akhale mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.” Mfumu inakondwera ndi uphunguwu, ndipo inachita momwemo.
Kuthi intombazana enhle emehlweni enkosi ibe yindlovukazi esikhundleni sikaVashiti. Indaba yayilungile-ke emehlweni enkosi, yenza njalo.
5 Myuda wina wa fuko la Benjamini, dzina lake Mordekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi, anali mu mzinda wa Susa.
Kwakukhona indoda engumJuda eShushani isigodlo, obizo layo lalinguModekhayi indodana kaJayiri indodana kaShimeyi indodana kaKishi, umBhenjamini,
6 Iyeyu anali mmodzi mwa anthu amene anatengedwa ukapolo ndi Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda.
owayethunjwe eJerusalema kanye labathunjwa ababethunjwe loJekoniya inkosi yakoJuda, uNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni owayebathumbile.
7 Mordekai nʼkuti atalera Hadasa, amene ankatchedwanso Estere, mwana wamkazi wa amalume ake chifukwa analibe abambo kapena amayi. Mtsikanayu anali wokongola ndi wooneka bwino ndipo Mordekai ankamutenga ngati mwana wake weniweni pamene abambo ndi amayi ake anamwalira.
Njalo wayesondla uHadasa, onguEsta, umntakamalumakhe, ngoba wayengelayise kumbe unina; njalo intombi yayinhle ngesimo njalo ikhangeleka kuhle; ekufeni-ke kukayise lonina uModekhayi wayithatha yaba yindodakazi yakhe.
8 Lamulo la mfumu atalilengeza ndi kubwera nawo pamodzi anamwali ambiri ku mzinda wa Susa kuti akasamalidwe ndi Hegai, Estere nayenso anatengedwa kupita naye ku nyumba ya mfumu kuti akasamalidwe ndi Hegai woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi uja.
Kwasekusithi sekuzwakele ilizwi lenkosi lomthetho wayo, lapho sekubuthaniswe izintombi ezinengi eShushani isigodlo esandleni sikaHegayi, uEsta laye wathathwa wasiwa endlini yenkosi esandleni sikaHegayi, umlondolozi wabesifazana.
9 Hegai anasangalatsidwa naye namwaliyo ndipo anamukomera mtima. Mosataya nthawi anamupatsa mafuta ake odzola ndi chakudya chapadera. Anamusankhiranso anamwali asanu ndi awiri a ku nyumba ya mfumu kuti azimutumikira, ndipo iye pamodzi ndi anamwali omutumikira aja anawapatsa malo abwino koposa mʼnyumba yosungira akazi.
Lentombi yayinhle emehlweni akhe, yazuza umusa phambi kwakhe; wasehle eyinika amakha ayo lezabelo zayo, lamantombazana akhethiweyo ayisikhombisa ukuyinika avela endlini yenkosi; wayisusa wayifaka yona lamantombazana ayo endaweni enhle yendlu yabesifazana.
10 Estere sanawulule mtundu wake ndi abale ake chifukwa Mordekai anamuletsa kutero.
UEsta wayengakhulumanga abantu bakwabo lomhlobo wakhe, ngoba uModekhayi wayemlayile ukuthi angakukhulumi.
11 Tsiku ndi tsiku Mordekai ankayendayenda pafupi ndi bwalo la nyumba yosungiramo akazi ija kuti adziwe za moyo wa Estere ndi kuti zinthu zikumuyendera bwanji.
Langalo lonke usuku ngosuku uModekhayi wayehambahamba phambi kweguma lendlu yabesifazana ukwazi impilakahle kaEsta lokuthi kuyini okuzakwenzeka kuye.
12 Tsono nthawi inkafika kuti namwali aliyense akaonekere kwa mfumu Ahasiwero, pakutha pa miyezi khumi ndi iwiri yomwe inakhazikitsidwa kuti amayi azidzikongoletsa. Pa miyezi isanu ndi umodzi ankadzola mafuta a mure ndipo pa miyezi isanu ndi umodzi inayo ankadzola zonunkhira ndi zokongoletsa.
Lekufikeni kwezopha lentombi ngentombi ukungena enkosini uAhasuwerusi ekucineni sekwenziwe kuye njengomthetho wabesifazana, inyanga ezilitshumi lambili, ngoba ngokunjalo kwagcwaliseka insuku zamakha awo, inyanga eziyisithupha ngamafutha emure, lenyanga eziyisithupha ngamakha okuqhola, langamanye amakha abesifazana.
13 Ndipo namwali ankapita kwa mfumu motere: Ankaloledwa kutenga chilichonse angafune mʼnyumba yosungiramo akazi kupita nacho ku nyumba ya mfumu.
Ngalokho-ke intombi yangena enkosini; loba kuyini ekutshoyo izakunikwa ukuthi ihambe lakho isuka endlini yabesifazana isiya endlini yenkosi.
14 Ankalowa madzulo kwa mfumu ndi kutuluka mmawa kupita ku nyumba ina yosungira akazi yomwe ankayangʼanira ndi Saasigazi, mdindo wofulidwa wa mfumu amene amayangʼanira akazi a mfumu. Namwali sankabwerera kwa mfumu pokhapokha amukomere mtima ndi kumuyitana potchula dzina lake.
Ntambama yangena, lekuseni ibuyele endlini yesibili yabesifazana, esandleni sikaShashigazi umthenwa wenkosi umlondolozi wabafazi abancinyane; kayingenanga futhi enkosini ngaphandle kokuthi inkosi ithokoze ngayo, ibizwe ngebizo.
15 Tsono inafika nthawi kuti Estere, mwana wamkazi wa Abihaili amenenso analeredwa ndi Mordekai amalume ake, alowe kwa mfumu. Iye sanapemphe kanthu kalikonse, koma anatenga zokhazo zimene ananena Hegai mdindo wofulidwa wa mfumu woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi. Ndipo aliyense amene anamuona Estere, anasangalatsidwa naye.
Kwathi selifikile izopho likaEsta, indodakazi kaAbihayili umalumakhe kaModekhayi owayemthethe waba yindodakazi yakhe, lokuthi angene enkosini, kacelanga lutho ngaphandle kwalokho uHegayi umthenwa wenkosi umlondolozi wabesifazana akutshoyo. UEsta wayesemukela-ke umusa emehlweni abo bonke abambonayo.
16 Anapita naye kwa mfumu Ahasiwero ku nyumba ya ufumu pa mwezi wa khumi, mwezi wa Tebete, chaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wake.
Ngokunjalo uEsta wasiwa enkosini uAhasuwerusi endlini yayo yesikhosini ngenyanga yetshumi, eyinyanga kaTebethi, ngomnyaka wesikhombisa wokubusa kwayo.
17 Ndipo mfumu inamukonda Estere koposa wina aliyense wa akazi aja, kotero inamukonda ndi kumukomera mtima koposa wina aliyense wa anamwali aja. Choncho anamumveka chipewa chaufumu pa mutu pake nakhala mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.
Inkosi yasimthanda uEsta okwedlula bonke abesifazana, wemukela umusa lesihe phambi kwayo okwedlula zonke intombi, yasibeka umqhele wobukhosi ekhanda lakhe, yamenza indlovukazi esikhundleni sikaVashiti.
18 Ndipo mfumu inakonza phwando lalikulu, phwando la Estere, kukonzera anthu olemekezeka ndi nduna zake zonse. Analamuliranso kuti anthu mʼzigawo zonse asapereke msonkho ndipo anapereka mphatso monga mwakukoma mtima kwa mfumu.
Inkosi yasisenzela zonke iziphathamandla zayo lenceku zayo idili elikhulu, idili likaEsta. Yenzela izabelo ikhefu, yapha izipho njengokwamandla enkosi.
19 Anamwali atasonkhanitsidwa pamodzi, Mordekai anakhala pansi pa chipata cha mfumu.
Kwathi intombi sezibuthanisiwe okwesibili, uModekhayi wayehlezi esangweni lenkosi.
20 Koma Estere anali asanawululebe za mtundu wake ndi anthu a pa banja lake monga momwe analamulira Mordekai, chifukwa anapitirira kutsata malangizo a Mordekai monga ankachitira pamene ankamulera.
UEsta wayengakhulumanga umhlobo wakhe labantu bakibo, njengoba uModekhayi wamlaya, ngoba uEsta wenza umlayo kaModekhayi njengalapho esondliwa elaye.
21 Pa nthawi imene Mordekai ankalondera pa chipata cha mfumu, Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa amfumu, olondera pa khomo la nyumba yake, anayipidwa mtima ndipo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
Ngalezozinsuku uModekhayi ehlezi esangweni lenkosi, oBigithani loTereshi abathenwa ababili benkosi, abalindi bombundu, bathukuthela, badinga ukuyithela isandla inkosi uAhasuwerusi.
22 Koma Mordekai atazindikira za chiwembuchi anawuza mfumukazi Estere ndipo iye anakawuza mfumu mʼmalo mwa Mordekai.
Njalo udaba lwaziwa kuModekhayi, waselutshela uEsta indlovukazi; njalo uEsta wayitshela inkosi ebizweni likaModekhayi.
23 Ndipo pamene anafufuza za chiwembuchi kuti zinali zoona, adindo awiriwa anaphedwa monyongedwa. Zinthu izi zinalembedwa mʼbuku la Mbiri ndi kusungidwa ndi Mfumu.
Lolodaba seluhlolwa, lwatholakala lunjalo; ngakho bobabili baphanyekwa esihlahleni. Kwasekubhalwa egwalweni lwemilando phambi kwenkosi.

< Estere 2 >