< Estere 10 >
1 Mfumu Ahasiwero anakhometsa msonkho mʼdziko lake lonse mpaka ku zilumba zonse.
Puis le roi Assuérus imposa un tribut au pays et aux îles de la mer.
2 Ndipo ntchito zonse zochitika ndi mphamvu zake komanso ndi zonse zofotokoza za ukulu wa Mordekai, kukwezedwa kwake ndi mfumu, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Mediya ndi Peresiya?
Or, quant à tous les actes de sa puissance et à ses exploits, et à la description de la grandeur à laquelle le roi éleva Mardochée, ces choses ne sont-elles pas écrites dans le livre des Chroniques des rois de Médie et de Perse?
3 Pakuti Mordekai Myuda uja anali wachiwiri wa mfumu Ahasiwero. Kwa Ayuda onse Mordekai anali munthu wamkulu ndipo ankamukonda chifukwa ankachitira zabwino mtundu wake ndi kufunira mtendere abale ake.
Car le Juif Mardochée fut le second après le roi Assuérus, et il fut grand parmi les Juifs et agréable à la multitude de ses frères, recherchant le bien de son peuple, et parlant pour le bonheur de toute sa race.