< Aefeso 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
Píšu vám jako Bohem ustanovený apoštol Ježíše Krista.
2 Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
Přeji vám Boží milost a pokoj a chválím Boha za všechno požehnání,
3 Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
kterým nás obdařil z toho důvodu, že náležíme Kristu.
4 Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
Už dávno před stvořením světa rozhodl se Bůh získat si nás prostřednictvím Kristovým, aby z nás učinil své děti a přiznal nám svou dokonalost.
5 Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
Dík Bohu za jeho nekonečnou laskavost, kterou nám prokázal v osobě Ježíšově!
6 Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
Jeho milost k nám je tak nesmírná,
7 Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
že nám pro jeho oběť odpustil všechno zlé a zachránil nás od jisté smrti.
8 chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
Ve své moudrosti a prozíravosti nám odhalil svůj velkorysý záměr, který po staletí zůstával lidem ukryt,
9 Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
že totiž ve stanovenou dobu pošle svého Syna, aby nás ze všech stran, živé i mrtvé shromáždil navždy k sobě.
10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
A tak nás, přesně podle svého rozhodnutí, učinil svým majetkem, abychom ho chválili a oslavovali, kdo jsme svou naději upnuli ke Kristu.
11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
Vždyť Kristovou zásluhou jste do tohoto záměru byli zahrnuti i vy,
12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
když jste uslyšeli jeho poselství a uvěřili.
13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
Na důkaz toho vás Bůh poznamenal svou pečetí, totiž Duchem svatým, který byl dávno zaslíben. Jeho přítomnost v nás je zárukou, že Bůh nám skutečně dá všechno, co slíbil.
14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
Je to i jakási pečeť, že jsme jeho vlastnictvím a že nás vezme k sobě. Což je možné nechválit a neoslavovat ho za to?
15 Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
Proto také od chvíle, kdy jsem uslyšel o vaší důvěře ke Kristu a o vaší lásce ke všem jeho vyznavačům,
16 ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
nepřestal jsem nikdy za vás Bohu děkovat ve svých modlitbách.
17 Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
Prosím ho, aby vám dal plné a jasné pochopení Kristova významu a dosahu jeho díla pro nás.
18 Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
Modlím se, aby ve vašem srdci zazářil odlesk slavné budoucnosti, k níž jsme pozváni, abyste si uvědomili, jak fantastického bohatství se stáváte plnoprávnými spolupodílníky.
19 Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
Vždyť vše, co patří Bohu, je i vaše! A prosím i o to, abyste se přesvědčili, jak neuvěřitelně velká je moc, která ve vás působí.
20 imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
Je to táž moc, která vzkřísila Krista z mrtvých a vyzdvihla ho vysoko nad všechny krále a vlády, velitele i diktátory, až na čestné místo po pravici Boží.
21 Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
Jeho sláva nemá obdoby v minulosti ani budoucnosti. (aiōn g165)
22 Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
Všechno je mu podřízeno. On je hlavou církve,
23 umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.
církev je jeho tělem, naplněná jím samým, původcem a dárcem všeho.

< Aefeso 1 >