< Aefeso 6 >
1 Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera.
Otroci, ubogajte svoje starše v Gospodu, kajti to je prav.
2 “Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo.
Spoštuj svojega očeta in mater (kar je prva zapoved z obljubo),
3 Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.”
da bo lahko dobro s teboj in boš lahko dolgo živel na zemlji.
4 Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.
In vi očetje, ne provocirajte svojih otrok do besa, temveč jih vzgajajte v Gospodovem poučevanju in svarilu.
5 Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu.
Služabniki, bodite poslušni tem, ki so vaši gospodarji glede na meso, s strahom in trepetom, v iskrenosti svojega srca kakor Kristusu;
6 Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu.
ne z navidezno vdanostjo, kakor bi raje ugajali ljudem, temveč kot Kristusovi služabniki iz srca izpolnjujte Božjo voljo;
7 Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu.
z dobro voljo izvršujte službo kakor Gospodu in ne ljudem,
8 Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.
ker veste, da katerokoli dobro stvar kdorkoli stori, isto bo prejel od Gospoda, bodisi je suženj ali svoboden.
9 Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.
In vi, gospodarji, jim storite iste stvari in prizanašajte grožnjam, ker veste, da je tudi vaš Gospodar v nebesih; niti pri njem ni oziranja na osebe.
10 Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu.
Končno, moji bratje, bodite močni v Gospodu in v sili njegove moči.
11 Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana.
Nadenite si vso Božjo bojno opremo, da boste zmožni obstati proti hudičevim zvijačam.
12 Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn )
Kajti ne borimo se proti mesu in krvi, temveč proti kneževinam, proti oblastem, proti vladarjem teme tega sveta, proti duhovni zlobnosti na visokih položajih. (aiōn )
13 Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu.
Zato vzemite nase celotno Božjo bojno opremo, da se boste zmožni na hudoben dan zoperstaviti in vse storiti ter obstati.
14 Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa.
Stojte torej in imejte svoja ledja opasana z resnico in na sebi imejte prsni oklep pravičnosti
15 Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato.
in svoja stopala, obuta s pripravljenostjo evangelija miru;
16 Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo.
predvsem vzemite ščit vere, s katerim boste zmožni pogasiti vse ognjene puščice zlobnega.
17 Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu.
In vzemite čelado rešitve duše in meč Duha, kar je Božja beseda;
18 Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.
in vedno molíte z vso molitvijo in ponižno prošnjo v Duhu in k temu bedite z vso vztrajnostjo in ponižno prošnjo za vse svete;
19 Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha.
in zame, da mi bo lahko dana izgovarjava, da bom lahko pogumno odpiral svoja usta, da se razglasi skrivnost evangelija,
20 Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.
za katerega sem predstavnik v vezeh, da bom v tem lahko pogumno govoril, kakor bi moral govoriti.
21 Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita.
Toda, da boste lahko poznali tudi moje zadeve in kako delam, vam bo Tihik, moj ljubljeni brat in zvesti služabnik v Gospodu, oznanil vse stvari;
22 Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.
katerega sem poslal k vam zaradi istega namena, da bi vi lahko spoznali naše zadeve in da bi on lahko potolažil vaša srca.
23 Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse.
Mir bodi bratom in ljubezen z vero od Boga Očeta in Gospoda Jezusa Kristusa.
24 Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.
Milost bodi z vsemi tistimi, ki z iskrenostjo ljubijo našega Gospoda Jezusa Kristusa. Amen. [Napisano iz Rima Efežanom po Tihiku.]