< Aefeso 5 >

1 Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.
Estote ergo imitatores Dei, sicut filii charissimi:
2 Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu.
et ambulate in dilectione, sicut et Christus dilexit nos, et tradidit semetipsum pro nobis oblationem, et hostiam Deo in odorem suavitatis.
3 Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu.
Fornicatio autem, et omnis immunditia, aut avaritia nec nominetur in vobis, sicut decet sanctos:
4 Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.
aut turpitudo, aut stultiloquium, aut scurrilitas, quae ad rem non pertinet: sed magis gratiarum actio.
5 Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.
Hoc enim scitote intelligentes: quod omnis fornicator, aut immundus, aut avarus, quod est idolorum servitus, non habet hereditatem in regno Christi, et Dei.
6 Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera.
Nemo vos seducat inanibus verbis: propter haec enim venit ira Dei in filios diffidentiae.
7 Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere.
Nolite ergo effici participes eorum.
8 Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika
Eratis enim aliquando tenebrae: nunc autem lux in Domino. Ut filii lucis ambulate:
9 (pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi).
fructus enim lucis est in omni bonitate, et iustitia, et veritate:
10 Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye.
probantes quid sit beneplacitum Deo:
11 Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse.
et nolite communicare operibus infructuosis tenebrarum, magis autem redarguite.
12 Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.
Quae enim in occulto fiunt ab ipsis, turpe est et dicere.
13 Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala.
Omnia autem, quae arguuntur, a lumine manifestantur: omne enim, quod manifestatur, lumen est.
14 Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”
Propter quod dicit: Surge qui dormis, et exurge a mortuis, et illuminabit te Christus.
15 Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru.
Videte itaque fratres, quomodo caute ambuletis: non quasi insipientes,
16 Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa.
sed ut sapientes: redimentes tempus, quoniam dies mali sunt.
17 Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.
Propterea nolite fieri imprudentes: sed intelligentes quae sit voluntas Dei.
18 Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.
Et nolite inebriari vino, in quo est luxuria: sed implemini Spiritu sancto,
19 Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu.
loquentes vobismetipsis in psalmis, et hymnis, et canticis spiritualibus, cantantes, et psallentes in cordibus vestris Domino,
20 Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
gratias agentes semper pro omnibus, in nomine Domini nostri Iesu Christi Deo et Patri.
21 Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.
Subiecti invicem in timore Christi.
22 Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye.
Mulieres viris suis subditae sint, sicut Domino:
23 Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake.
quoniam vir caput est mulieris: sicut Christus caput est Ecclesiae: Ipse, salvator corporis eius.
24 Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.
Sed sicut Ecclesia subiecta est Christo, ita et mulieres viris suis in omnibus.
25 Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo
Viri, diligite uxores vestras, sicut et Christus dilexit Ecclesiam, et seipsum tradidit pro ea,
26 kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake.
ut illam sanctificaret, mundans eam lavacro aquae in verbo vitae,
27 Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro.
ut exhiberet ipse sibi in gloriosam Ecclesiam, non habentem maculam, aut rugam, aut aliquid huiusmodi, sed ut sit sancta et immaculata.
28 Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha.
Ita et viri debent diligere uxores suas ut corpora sua. Qui suam uxorem diligit, seipsum diligit.
29 Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake
Nemo enim umquam carnem suam odio habuit: sed nutrit, et fovet eam, sicut et Christus Ecclesiam:
30 pakuti ndife ziwalo za thupi lake.
quia membra sumus corporis eius, de carne eius, et de ossibus eius.
31 “Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
Propter hoc relinquet homo patrem, et matrem suam, et adhaerebit uxori suae: et erunt duo in carne una.
32 Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo.
Sacramentum hoc magnum est, ego autem dico in Christo et in Ecclesia.
33 Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.
Verumtamen et vos singuli, unusquisque uxorem suam sicut seipsum diligat: uxor autem timeat virum suum.

< Aefeso 5 >