< Aefeso 5 >

1 Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.
Therefore be imitators of God, as His dear children.
2 Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu.
And live and act lovingly, as Christ also loved you and gave Himself up to death on our behalf as an offering and sacrifice to God, yielding a fragrant odor.
3 Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu.
But fornication and every kind of impurity, or covetousness, let them not even be mentioned among you, for they ought not to be named among God's people.
4 Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.
Avoid shameful and foolish talk and low jesting--they are all alike discreditable--and in place of these give thanks.
5 Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.
For be well assured that no fornicator or immoral person and no money-grubber--or in other words idol-worshipper--has any share awaiting him in the Kingdom of Christ and of God.
6 Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera.
Let no one deceive you with empty words, for it is on account of these very sins that God's anger is coming upon the disobedient.
7 Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere.
Therefore do not become sharers with them.
8 Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika
There was a time when you were nothing but darkness. Now, as Christians, you are Light itself.
9 (pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi).
Live and act as sons of Light--for the effect of the Light is seen in every kind of goodness, uprightness and truth--
10 Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye.
and learn in your own experiences what is fully pleasing to the Lord.
11 Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse.
Have nothing to do with the barren unprofitable deeds of darkness, but, instead of that, set your faces against them;
12 Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.
for the things which are done by these people in secret it is disgraceful even to speak of.
13 Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala.
But everything can be tested by the light and thus be shown in its true colors; for whatever shines of itself is light.
14 Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”
For this reason it is said, "Rise, sleeper; rise from among the dead, and Christ will shed light upon you."
15 Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru.
Therefore be very careful how you live and act. Let it not be as unwise men, but as wise.
16 Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa.
Buy up your opportunities, for these are evil times.
17 Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.
On this account do not prove yourselves wanting in sense, but try to understand what the Lord's will is.
18 Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.
Do not over-indulge in wine--a thing in which excess is so easy--
19 Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu.
but drink deeply of God's Spirit. Speak to one another with psalms and hymns and spiritual songs. Sing and offer praise in your hearts to the Lord.
20 Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
Always and for everything let your thanks to God the Father be presented in the name of our Lord Jesus Christ;
21 Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.
and submit to one another out of reverence for Christ.
22 Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye.
Married women, submit to your own husbands as if to the Lord;
23 Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake.
because a husband is the Head of his wife as Christ also is the Head of the Church, being indeed the Saviour of this His Body.
24 Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.
And just as the Church submits to Christ, so also married women should be entirely submissive to their husbands.
25 Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo
Married men, love your wives, as Christ also loved the Church and gave Himself up to death for her;
26 kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake.
in order to make her holy, cleansing her with the baptismal water by the word,
27 Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro.
that He might present the Church to Himself a glorious bride, without spot or wrinkle or any other defect, but to be holy and unblemished.
28 Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha.
So too married men ought to love their wives as much as they love themselves. He who loves his wife loves himself.
29 Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake
For never yet has a man hated his own body. On the contrary he feeds and cherishes it, just as Christ feeds and cherishes the Church;
30 pakuti ndife ziwalo za thupi lake.
because we are, as it were, parts of His Body.
31 “Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
"For this reason a man is to leave his father and his mother and be united to his wife, and the two shall be as one."
32 Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo.
That is a great truth hitherto kept secret: I mean the truth concerning Christ and the Church.
33 Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.
Yet I insist that among you also, each man is to love his own wife as much as he loves himself, and let a married woman see to it that she treats her husband with respect.

< Aefeso 5 >