< Aefeso 3 >

1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
អតោ ហេតោ រ្ភិន្នជាតីយានាំ យុឞ្មាកំ និមិត្តំ យីឝុខ្រីឞ្ដស្យ ពន្ទី យះ សោៜហំ បៅលោ ព្រវីមិ។
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
យុឞ្មទត៌្ហម៑ ឦឝ្វរេណ មហ្យំ ទត្តស្យ វរស្យ និយមះ កីទ្ឫឝស្តទ៑ យុឞ្មាភិរឝ្រាវីតិ មន្យេ។
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
អត៌្ហតះ បូវ៌្វំ មយា សំក្ឞេបេណ យថា លិខិតំ តថាហំ ប្រកាឝិតវាក្យេនេឝ្វរស្យ និគូឍំ ភាវំ ជ្ញាបិតោៜភវំ។
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
អតោ យុឞ្មាភិស្តត៑ បឋិត្វា ខ្រីឞ្ដមធិ តស្មិន្និគូឍេ ភាវេ មម ជ្ញានំ កីទ្ឫឝំ តទ៑ ភោត្ស្យតេ។
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
បូវ៌្វយុគេឞុ មានវសន្តានាស្តំ ជ្ញាបិតា នាសន៑ កិន្ត្វធុនា ស ភាវស្តស្យ បវិត្រាន៑ ប្រេរិតាន៑ ភវិឞ្យទ្វាទិនឝ្ច ប្រត្យាត្មនា ប្រកាឝិតោៜភវត៑;
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
អត៌្ហត ឦឝ្វរស្យ ឝក្តេះ ប្រកាឝាត៑ តស្យានុគ្រហេណ យោ វរោ មហ្យម៑ អទាយិ តេនាហំ យស្យ សុសំវាទស្យ បរិចារកោៜភវំ,
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
តទ្វារា ខ្រីឞ្ដេន ភិន្នជាតីយា អន្យៃះ សាទ៌្ធម៑ ឯកាធិការា ឯកឝរីរា ឯកស្យាះ ប្រតិជ្ញាយា អំឝិនឝ្ច ភវិឞ្យន្តីតិ។
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
សវ៌្វេឞាំ បវិត្រលោកានាំ ក្ឞុទ្រតមាយ មហ្យំ វរោៜយម៑ អទាយិ យទ៑ ភិន្នជាតីយានាំ មធ្យេ ពោធាគយស្យ គុណនិធេះ ខ្រីឞ្ដស្យ មង្គលវាត៌្តាំ ប្រចារយាមិ,
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn g165)
កាលាវស្ថាតះ បូវ៌្វស្មាច្ច យោ និគូឍភាវ ឦឝ្វរេ គុប្ត អាសីត៑ តទីយនិយមំ សវ៌្វាន៑ ជ្ញាបយាមិ។ (aiōn g165)
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
យត ឦឝ្វរស្យ នានារូបំ ជ្ញានំ យត៑ សាម្ប្រតំ សមិត្យា ស្វគ៌េ ប្រាធាន្យបរាក្រមយុក្តានាំ ទូតានាំ និកដេ ប្រកាឝ្យតេ តទត៌្ហំ ស យីឝុនា ខ្រីឞ្ដេន សវ៌្វាណិ ស្ឫឞ្ដវាន៑។
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn g165)
យតោ វយំ យស្មិន៑ វិឝ្វស្យ ទ្ឫឍភក្ត្យា និព៌្ហយតាម៑ ឦឝ្វរស្យ សមាគមេ សាមត៌្ហ្យញ្ច
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
ប្រាប្តវន្តស្តមស្មាកំ ប្រភុំ យីឝុំ ខ្រីឞ្ដមធិ ស កាលាវស្ថាយាះ បូវ៌្វំ តំ មនោរថំ ក្ឫតវាន៑។ (aiōn g165)
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
អតោៜហំ យុឞ្មន្និមិត្តំ ទុះខភោគេន ក្លាន្តិំ យន្ន គច្ឆាមីតិ ប្រាត៌្ហយេ យតស្តទេវ យុឞ្មាកំ គៅរវំ។
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
អតោ ហេតោះ ស្វគ៌ប្ឫថិវ្យោះ ស្ថិតះ ក្ឫត្ស្នោ វំឝោ យស្យ នាម្នា វិខ្យាតស្តម្
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
អស្មត្ប្រភោ រ្យីឝុខ្រីឞ្ដស្យ បិតរមុទ្ទិឝ្យាហំ ជានុនី បាតយិត្វា តស្យ ប្រភាវនិធិតោ វរមិមំ ប្រាត៌្ហយេ។
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
តស្យាត្មនា យុឞ្មាកម៑ អាន្តរិកបុរុឞស្យ ឝក្តេ រ្វ្ឫទ្ធិះ ក្រិយតាំ។
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
ខ្រីឞ្ដស្តុ វិឝ្វាសេន យុឞ្មាកំ ហ្ឫទយេឞុ និវសតុ។ ប្រេមណិ យុឞ្មាកំ ពទ្ធមូលត្វំ សុស្ថិរត្វញ្ច ភវតុ។
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
ឥត្ថំ ប្រស្ថតាយា ទីគ៌្ហតាយា គភីរតាយា ឧច្ចតាយាឝ្ច ពោធាយ សវ៌្វៃះ បវិត្រលោកៃះ ប្រាប្យំ សាមត៌្ហ្យំ យុឞ្មាភិ រ្លភ្យតាំ,
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
ជ្ញានាតិរិក្តំ ខ្រីឞ្ដស្យ ប្រេម ជ្ញាយតាម៑ ឦឝ្វរស្យ សម្បូណ៌វ្ឫទ្ធិបយ៌្យន្តំ យុឞ្មាកំ វ្ឫទ្ធិ រ្ភវតុ ច។
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
អស្មាកម៑ អន្តរេ យា ឝក្តិះ ប្រកាឝតេ តយា សវ៌្វាតិរិក្តំ កម៌្ម កុវ៌្វន៑ អស្មាកំ ប្រាត៌្ហនាំ កល្បនាញ្ចាតិក្រមិតុំ យះ ឝក្នោតិ
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
ខ្រីឞ្ដយីឝុនា សមិតេ រ្មធ្យេ សវ៌្វេឞុ យុគេឞុ តស្យ ធន្យវាទោ ភវតុ។ ឥតិ។ (aiōn g165)

< Aefeso 3 >