< Aefeso 3 >

1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
Ngenxa yalesisizatho, mina Phawuli, isibotshwa sikaKhristu uJesu ngenxa yenu lina bantu beZizweni.
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
Ngeqiniso selizwile ngokuphathwa komusa kaNkulunkulu engawuphiwayo ngenxa yenu,
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
ukuthi ngaziswa imfihlakalo ngokwambulelwa njengoba sengabhala ngamafitshane.
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
Nxa libala lokhu lizenelisa ukuzwisisa umbono wami ngemfihlakalo kaKhristu,
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
engazange yaziswe abantu kwezinye izizukulwane njengoba khathesi isiveziwe nguMoya kubapostoli abangcwele bakaNkulunkulu lakubaphrofethi.
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
Imfihlakalo le iyikuthi ngevangeli abeZizweni bazindlalifa bekanye labako-Israyeli, amalunga omzimba munye ndawonye, labahlanganyeli kuso isithembiso kuKhristu uJesu.
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
Mina ngaba yinceku yevangeli leli ngesipho somusa kaNkulunkulu engasiphiwa ngokusebenza kwamandla akhe.
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
Lanxa ngimncane kulabancane bonke babantu bakaNkulunkulu, umusa lo ngawunikwa: ukuba ngitshumayele kwabeZizweni inotho kaKhristu engacubungulekiyo,
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn g165)
njalo ngikubeke obala ukuphatha kwami imfihlakalo le eyayifihliwe okweminyaka eminengi eyedlulayo kuNkulunkulu, owadala izinto zonke. (aiōn g165)
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
Injongo yakhe yayiyikuthi ibandla lazise ababusi leziphathamandla zemibuso yasezulwini ngenhlakanipho emangalisayo kaNkulunkulu,
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn g165)
ngokwenhloso yakhe engulaphakade ayifeza kuKhristu uJesu iNkosi yethu. (aiōn g165)
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
Kuye langokukholwa kuye singasondela kuNkulunkulu ngokukhululeka langesibindi.
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
Ngakho, ngiyalicela ukuba lingalahli ithemba ngenxa yokulihluphekela kwami, okuludumo kini.
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
Ngenxa yalokhu ngiyaguqa phambi kukaBaba,
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
lapho yonke imuli yamakholwa asezulwini lasemhlabeni ethola khona ibizo layo.
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
Ngikhulekela ukuthi ngenotho yobukhosi bakhe aliqinise ngamandla ngoMoya wakhe ezinhliziyweni zenu
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
ukuze uKhristu ahlale ezinhliziyweni zenu ngokukholwa. Ngikhulekela ukuba ligxile njalo liqine othandweni,
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
libe lamandla kanye labangcwele beNkosi bonke ukuba liqedisise ububanzi lobude lokujula kanye lokuzika kothando lukaKhristu,
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
lokuba lilwazi uthando lolu oludlula ukwazi ukuze ligcwaliswe ngesilinganiso sokugcwala okupheleleyo kukaNkulunkulu.
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
Ngakho-ke, kuye lowo oyenza okukhulu kakhulu kulalokho esikucelayo kumbe esikucabangayo, ngokwamandla akhe asebenza phakathi kwethu,
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
udumo kalube kuye ebandleni lakuKhristu uJesu kuzizukulwane zonke kuze kube nini lanini! Ameni. (aiōn g165)

< Aefeso 3 >