< Aefeso 3 >
1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
For this cause I Paul am the prisoner of Jesus Christ for the sake of you Gentiles:
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
as ye have heard the dispensation of the grace of God, which was given me to preach unto you:
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
that by immediate revelation He made known to me the mystery, (as I wrote before in brief, by which,
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
when ye read it, ye may perceive my knowledge in the mystery of Christ, )
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
which in other generations was not made known to men, as it is now revealed to his holy apostles and prophets by the Spirit; that the Gentiles should be co-heirs,
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
and of the same body, and joint-partakers of his promise in Christ, by the gospel:
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
of which I was made a minister, according to the gift of the grace of God conferred on me by the effectual operation of his power.
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
On me, who am less than the least of all saints, was this grace bestowed, that I should preach among the Gentiles the unsearchable riches of Christ,
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn )
and make all men to see the communication of the mystery, which from the ages past hath been hid in God, who created all things by Jesus Christ; (aiōn )
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
that the manifold wisdom of God might now be made known by the church to the principalities and powers in the heavenly regions;
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn )
according to the ancient purpose, which He executed in Christ Jesus our Lord: (aiōn )
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
by whom we have freedom and access with confidence through faith in Him.
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
Wherefore I desire that ye would not be discouraged at my afflictions on your account, which is your glory.
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
For this cause I bow my knees to the Father of our Lord Jesus Christ,
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
from whom the whole family in heaven and on earth is named,
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
that He would grant you, according to his glorious riches, to be strengthened with might by his Spirit, as to the inner man;
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
that Christ may dwell in your hearts by faith: and be ye rooted and grounded in love,
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
that ye may be able, with all the saints, to comprehend what is the breadth, and length, and depth,
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
and height, and to know the love of Christ, which surpasseth knowledge; that ye may be filled according to the abundant fulness of God.
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
Now to Him that is able to do exceeding abundantly above all that we can ask or think, according to the power operating in us,
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
to Him be glory in the church by Christ Jesus, throughout all the generations of eternal ages. Amen. (aiōn )