< Aefeso 3 >

1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
Because [God has done all this for] you non-Jews, I, Paul, [pray for you. I want you to know that it is because I serve] Christ Jesus for your sake that I am in prison.
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
I (assume that/think that probably) someone has told you how God acted very kindly toward me, appointing me [so that I would proclaim the gospel to you non-Jews].
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
God revealed to me the message that he had not revealed to others. When you read what I have already written briefly about that,
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
you will be able to understand that I understand clearly that message about Christ.
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
Formerly, [God] did not reveal that message to anyone, but now his Spirit has revealed that message to (his holy apostles and prophets/people who tell messages that come directly from God).
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
That message, which he has now revealed, is that because of our [(inc)] relationship with Christ Jesus, [all of us], non-Jews as well as Jews [MTY], will receive the [great spiritual blessings that God has] promised as we all form one group [MET] [as a result of our believing] the good news [about Christ].
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
By God powerfully enabling me, and because God acted kindly toward me, doing what I did not deserve, and chose me [to do that work], I became someone who tells others this good message.
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
Although I am the least [worthy] of all God’s people, God kindly [appointed] me to proclaim to the non-Jews the message about the great spiritual blessings that [they can receive] from Christ,
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn g165)
and to enable everyone to understand clearly how God accomplished what he planned. God, who created everything, [has now revealed] this message, which he never revealed to anyone before. (aiōn g165)
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
[What he planned] was that all (believers/people who belong to Christ) would be the ones who would reveal to all the ranks [DOU] of spiritual beings in heaven that what God had planned is wise in every way.
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn g165)
That is what God had always planned, and it is what he accomplished by what our Lord Jesus [has done]. (aiōn g165)
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
Because of what he has done and because of our relationship with him, [when we pray] we can approach God confidently and without being afraid.
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
So I ask that you do not be discouraged because of my suffering many things for you [here in prison]. You should feel honored that I am [willing to] suffer [these things for your sake].
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
Because [God has done all this for you], I kneel [and pray] [MTY] to [God our] Father.
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
He is the one who is [like] a father of all [the believers who are now in] heaven and those who are still on the earth.
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
I pray that, using his unlimited resources, he will cause you to be strengthened by his Spirit {cause his Spirit to strengthen you} in your (inner beings/hearts) with all [God’s] power.
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
That is, I pray that because of your trusting in Christ, his [Spirit] may live in your (inner beings/hearts) (OR, he may live in your hearts). And I pray that because you love [Christ] firmly and faithfully/continually [MET], you,
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
along with all other believers, may be able to know how very [DOU] much Christ loves [us(inc)].
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
I want you to experience how very deeply he loves us, even though it is not possible for us to understand fully [how much he loves us]. And I pray that God will enable you to be filled with {have a full measure of} all the [qualities of his character that] he himself has.
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
[God] is able to do much (greater things/more) than we could ask him to do, or even that we might think that he can do, by his power that is working within us.
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Because of our relationship with Christ Jesus, may all (believers/those who belong to him) praise him forever. (Amen!/May it be so!) (aiōn g165)

< Aefeso 3 >