< Aefeso 3 >
1 Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
Radi toga ja, Pavao, sužanj Krista Isusa za vas pogane...
2 Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
Zacijelo ste čuli za rasporedbu milosti Božje koja mi je dana za vas:
3 ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
objavom mi je obznanjeno otajstvo, kako netom ukratko opisah.
4 Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
Čitajući to, možete dokučiti kako ja shvaćam Kristovo otajstvo,
5 chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
koje nije bilo obznanjeno sinovima ljudskim drugih naraštaja. Ono je sada u Duhu objavljeno svetim njegovim apostolima i prorocima:
6 Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
da su pogani subaštinici i “sutijelo” i sudionici obećanja u Kristu Isusu - po evanđelju,
7 Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
kojega postadoh poslužiteljem darom milosti Božje koja mi je dana djelotvornošću snage njegove.
8 Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
Meni, najmanjemu od svih svetih, dana je ova milost: poganima biti blagovjesnikom neistraživog bogatstva Kristova
9 Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn )
i osvijetliti rasporedbu otajstva, pred vjekovima skrivena u Bogu, koji sve stvori, (aiōn )
10 Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
da sada - po Crkvi - Vrhovništvima i Vlastima na nebesima bude obznanjena mnogolika mudrost Božja
11 Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn )
zasnovana - po naumu o vjekovima - u Kristu Isusu Gospodinu našemu. (aiōn )
12 Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
U njemu, s pouzdanjem po vjeri u njega, imamo slobodan pristup.
13 Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
Zato ne klonite, molim, s nevolja mojih za vas! One su slava vaša!
14 Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
Zato prigibam koljena pred Ocem,
15 amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
od koga ime svakom očinstvu na nebu i na zemlji:
16 Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
neka vam dadne po bogatstvu Slave svoje ojačati se po Duhu njegovu u snazi za unutarnjeg čovjeka
17 kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
da po vjeri Krist prebiva u srcima vašim te u ljubavi ukorijenjeni i utemeljeni
18 kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
mognete shvatiti sa svima svetima što je Dužina i Širina i Visina i Dubina
19 Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
te spoznati nadspoznatljivu ljubav Kristovu da se ispunite do sve Punine Božje.
20 Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
Onomu pak koji snagom u nama djelatnom može učiniti mnogo izobilnije nego li mi moliti ili zamisliti -
21 Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Njemu slava u Crkvi i u Kristu Isusu za sva pokoljenja vijeka vjekovječnoga! Amen. (aiōn )