< Aefeso 2 >

1 Kunena za inu, kale munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu,
Vous aussi, vous étiez morts par les fautes, par les péchés
2 mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. (aiōn g165)
auxquels vous vous êtes autrefois livrés sous l'influence de notre siècle mondain, sous l'influence de celui qui commande aux puissances qui sont dans l'air, je parle de cet Esprit qui agit aujourd'hui dans les hommes rebelles. (aiōn g165)
3 Nthawi ina tonsefe tinalinso ndi moyo wonga wawo, tinkachitanso zilizonse zimene matupi ndi maganizo athu ankafuna. Mwachibadwa chathu, tinali oyenera chilango monga anthu ena onse.
Oui, nous tous, nous cédions autrefois à nos passions charnelles, nous obéissions à tous les caprices de la chair et des sens, et nous étions naturellement enfants de colère comme les autres hommes.
4 Koma chifukwa cha chikondi chake chachikulu pa ife, Mulungu amene ndi olemera mʼchifundo,
Mais Dieu, dans la richesse de sa miséricorde et au nom du grand amour dont il nous aimait,
5 anatipanga kukhala amoyo ndi Khristu ngakhale pamene ife tinali akufa mu zolakwa zathu. Koma tinapulumutsidwa mwachisomo.
nous a fait revivre avec le Christ, nous que nos fautes avaient déjà fait mourir (c'est par grâce que vous êtes sauvés);
6 Ndipo Mulungu anatiukitsa pamodzi ndi Khristu ndi kutikhazika pamodzi ndi Iye mmwamba mwa Khristu Yesu,
il nous a ressuscités, et nous a assigné une place dans les cieux par Jésus-Christ.
7 ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. (aiōn g165)
Ainsi montre-t-il à tous les âges à venir l'extraordinaire richesse de sa grâce, par la bonté qu'il a eue pour nous en Jésus-Christ; (aiōn g165)
8 Pakuti mwapulumutsidwa mwachisomo, kudzera mʼchikhulupiriro ndipo izi sizochokera mwa inu eni, koma ndi mphatso ya Mulungu,
car c'est par la grâce que vous êtes sauvés, au moyen de la foi; et cela ne vient pas de vous, c'est un don de Dieu.
9 osati ndi ntchito, kuti wina aliyense asadzitamandire.
Ce n'est pas l'effet de vos oeuvres, et personne n'a à s'en glorifier;
10 Pakuti ndife ntchito ya Mulungu, olengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anazikonzeratu kale kuti tizichite.
car nous sommes son ouvrage; nous avons été créés en Jésus-Christ pour faire de bonnes oeuvres, et Dieu nous a rendus d'avance capables de les pratiquer.
11 Chifukwa chake kumbukirani kuti poyamba inu amene munali anthu a mitundu ina mwachibadwa ndipo munkatchedwa “osachita mdulidwe” ndi amene amadzitcha okha “a mdulidwe” (zimene zinachitika mʼthupi ndi manja a anthu).
Souvenez-vous donc qu'autrefois, vous, païens de naissance, ceux qui s'appelaient les circoncis, parce qu'ils l'étaient de main d'homme dans leur corps, vous appelaient les incirconcis;
12 Kumbukirani kuti nthawi imene inu munali wopanda Khristu, simunkawerengedwa ngati nzika za Israeli ndipo munali alendo pa pangano la lonjezo, wopanda chiyembekezo ndi opanda Mulungu mʼdziko lapansi.
souvenez-vous, dis-je, que vous étiez alors sans Christ, privés du droit de cité en Israël, étrangers aux alliances et aux promesses, n'ayant ni espérance ni Dieu dans le monde.
13 Koma tsopano mwa Khristu Yesu, inu amene nthawi ina munali kutali, mwabweretsedwa pafupi kudzera mʼmagazi a Khristu.
Maintenant, au contraire, étant en Jésus-Christ, vous qui étiez autrefois éloignés, vous vous êtes rapprochés par le sang du Christ.
14 Pakuti Iye mwini ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti awiri akhale mmodzi ndipo anagumula chotchinga, khoma la udani lotilekanitsa,
Car c'est lui qui est notre paix; il a réuni les deux peuples, il a abattu le mur de séparation, il a fait disparaître leur inimitié
15 pothetsa mʼthupi lake lamulo pamodzi ndi zolamulira zake ndi malangizo. Cholinga chake chinali chakuti alenge mwa Iye mwini, munthu mmodzi watsopano kuchokera kwa abwino, motero nʼkupanga mtendere,
en anéantissant par sa mort, la Loi, les ordonnances, les commandements; de la sorte il a formé en lui-même, avec les deux hommes, un seul homme nouveau, il a fait, la paix,
16 ndi kuyanjanitsa onse awiriwa mʼthupi lake kwa Mulungu, kudzera pa mtanda, umene Iye anaphapo udani wawo.
et, tous deux, réunis en un seul corps, il les a réconciliés avec Dieu par la croix, sur laquelle il fit mourir en sa personne leur inimitié.
17 Iye anabwera ndipo analalikira mtendere kwa inu amene munali kutali ndi mtendere ndiponso kwa iwonso amene anali pafupi.
Il est venu vous annoncer «La paix» à vous «qui étiez au loin comme à ceux qui étaient près».
18 Pakuti mwa Iye, ife tonse titha kufika kwa Atate mwa Mzimu mmodzi.
Car, grâce à lui, nous pouvons avoir, tous les deux, accès auprès du Père dans un même Esprit.
19 Kotero kuti, inu sindinunso alendo ndi adani, koma nzika pamodzi ndi anthu a Mulungu ndiponso a mʼbanja la Mulungu.
Vous n'êtes donc plus ni étrangers, ni intrus, vous êtes concitoyens des saints et membres de la famille de Dieu;
20 Ndinu okhazikika pa maziko a atumwi ndi a aneneri, pamodzi ndi Khristu Yesu mwini ngati mwala wa pa ngodya.
vous avez été édifiés sur le fondement posé par les apôtres qui sont aussi prophètes, fondement dont la pierre angulaire est Jésus-Christ.
21 Mwa Iyeyo, nyumba yonse yalumikizidwa pamodzi ndipo yakwezedwa kukhala Nyumba yoyera mwa Ambuye.
L'édifice entier, solidement élevé sur elle, deviendra un saint temple dans le Seigneur;
22 Ndipo mwa Iye, inunso mukamangidwa pamodzi ndi ena onse kukhala nyumba yokhalamo imene Mulungu amakhala mwa Mzimu wake.
et c'est sur elle que vous aussi avez été élevés pour servir à Dieu d'habitation spirituelle.

< Aefeso 2 >