< Aefeso 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
īśvarasyecchayā yīśukhrīṣṭasya preritaḥ paula iphiṣanagarasthān pavitrān khrīṣṭayīśau viśvāsino lokān prati patraṁ likhati|
2 Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
asmākaṁ tātasyeśvarasya prabho ryīśukhrīṣṭasya cānugrahaḥ śāntiśca yuṣmāsu varttatāṁ|
3 Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
asmākaṁ prabho ryīśoḥ khrīṣṭasya tāta īśvaro dhanyo bhavatu; yataḥ sa khrīṣṭenāsmabhyaṁ sarvvam ādhyātmikaṁ svargīyavaraṁ dattavān|
4 Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
vayaṁ yat tasya samakṣaṁ premnā pavitrā niṣkalaṅkāśca bhavāmastadarthaṁ sa jagataḥ sṛṣṭe pūrvvaṁ tenāsmān abhirocitavān, nijābhilaṣitānurodhācca
5 Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
yīśunā khrīṣṭena svasya nimittaṁ putratvapade'smān svakīyānugrahasya mahattvasya praśaṁsārthaṁ pūrvvaṁ niyuktavān|
6 Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
tasmād anugrahāt sa yena priyatamena putreṇāsmān anugṛhītavān,
7 Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
vayaṁ tasya śoṇitena muktim arthataḥ pāpakṣamāṁ labdhavantaḥ|
8 chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
tasya ya īdṛśo'nugrahanidhistasmāt so'smabhyaṁ sarvvavidhaṁ jñānaṁ buddhiñca bāhulyarūpeṇa vitaritavān|
9 Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
svargapṛthivyo ryadyad vidyate tatsarvvaṁ sa khrīṣṭe saṁgrahīṣyatīti hitaiṣiṇā
10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
tena kṛto yo manorathaḥ sampūrṇatāṁ gatavatsu samayeṣu sādhayitavyastamadhi sa svakīyābhilāṣasya nigūḍhaṁ bhāvam asmān jñāpitavān|
11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
pūrvvaṁ khrīṣṭe viśvāsino ye vayam asmatto yat tasya mahimnaḥ praśaṁsā jāyate,
12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
tadarthaṁ yaḥ svakīyecchāyāḥ mantraṇātaḥ sarvvāṇi sādhayati tasya manorathād vayaṁ khrīṣṭena pūrvvaṁ nirūpitāḥ santo'dhikāriṇo jātāḥ|
13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
yūyamapi satyaṁ vākyam arthato yuṣmatparitrāṇasya susaṁvādaṁ niśamya tasminneva khrīṣṭe viśvasitavantaḥ pratijñātena pavitreṇātmanā mudrayevāṅkitāśca|
14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
yatastasya mahimnaḥ prakāśāya tena krītānāṁ lokānāṁ mukti ryāvanna bhaviṣyati tāvat sa ātmāsmākam adhikāritvasya satyaṅkārasya paṇasvarūpo bhavati|
15 Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
prabhau yīśau yuṣmākaṁ viśvāsaḥ sarvveṣu pavitralokeṣu prema cāsta iti vārttāṁ śrutvāhamapi
16 ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
yuṣmānadhi nirantaram īśvaraṁ dhanyaṁ vadan prārthanāsamaye ca yuṣmān smaran varamimaṁ yācāmi|
17 Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
asmākaṁ prabho ryīśukhrīṣṭasya tāto yaḥ prabhāvākara īśvaraḥ sa svakīyatattvajñānāya yuṣmabhyaṁ jñānajanakam prakāśitavākyabodhakañcātmānaṁ deyāt|
18 Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
yuṣmākaṁ jñānacakṣūṁṣi ca dīptiyuktāni kṛtvā tasyāhvānaṁ kīdṛśyā pratyāśayā sambalitaṁ pavitralokānāṁ madhye tena datto'dhikāraḥ kīdṛśaḥ prabhāvanidhi rviśvāsiṣu cāsmāsu prakāśamānasya
19 Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
tadīyamahāparākramasya mahatvaṁ kīdṛg anupamaṁ tat sarvvaṁ yuṣmān jñāpayatu|
20 imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
yataḥ sa yasyāḥ śakteḥ prabalatāṁ khrīṣṭe prakāśayan mṛtagaṇamadhyāt tam utthāpitavān,
21 Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
adhipatitvapadaṁ śāsanapadaṁ parākramo rājatvañcetināmāni yāvanti padānīha loke paraloke ca vidyante teṣāṁ sarvveṣām ūrddhve svarge nijadakṣiṇapārśve tam upaveśitavān, (aiōn g165)
22 Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
sarvvāṇi tasya caraṇayoradho nihitavān yā samitistasya śarīraṁ sarvvatra sarvveṣāṁ pūrayituḥ pūrakañca bhavati taṁ tasyā mūrddhānaṁ kṛtvā
23 umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.
sarvveṣām uparyyupari niyuktavāṁśca saiva śaktirasmāsvapi tena prakāśyate|

< Aefeso 1 >